< Deuteronomy 8 >

1 Be thou war diligentli, that thou do ech comaundement which Y comaunde to thee to dai, that ye moun lyue, and be multiplied, and that ye entre, and welde the lond, for which the Lord swoor to youre fadris.
Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
2 And thou schalt haue mynde of al the weie, bi which thi Lord God ledde thee by fourti yeer, bi deseert, that he schulde turmente, and schulde tempte thee; and that tho thingis that weren tretid in `thi soule schulden be knowun, whether thou woldist kepe hise comaundementis, ethir nay.
Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
3 And he turmentide thee with nedynesse, and he yaf to thee meete, manna which thou knewist not, and thi fadris `knewen not, that he schulde schewe to thee, that a man lyueth not in breed aloone, but in ech word that cometh `out of the Lordis mouth, `that is, bi manna, that cam down `at the heest of the Lord.
Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
4 Thi cloth, bi which thou were hilid, failide not for eldnesse, and thi foot was not brokun undernethe, lo!
Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
5 the fourtith yeer is; that thou thenke in thin herte, for as a man techith his sone,
Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
6 so thi Lord God tauyte thee, that thou kepe the comaundementis of thi Lord God, and go in hise weies, and drede hym.
Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
7 For thi Lord God schal lede thee in to a good lond, in to the lond of ryueris, and of `stondynge watris, and of wellis, in whos feeldis and mounteyns the depthis of floodis breken out;
Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
8 in to the lond of wheete, of barli, and of vyneris, in which lond fige trees, and pumgranadis, and `olyue trees comen forth; in to the lond of oile, and of hony;
dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
9 where thow schalt ete thi breed with out nedynesse, and schalt vse the aboundaunce of alle thingis; of which lond the stonys ben yrun, and metals of tyn ben diggid of the hillis therof;
dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
10 that whanne thou hast ete, and art fillid, thou blesse thi Lord God for the beste lond which he yaf to thee.
Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
11 Therfor kepe thou, and be war, lest ony tyme thou foryete thi Lord God, and dispise hise comaundementis, and domes, and cerymonyes, whiche Y comaunde to thee to dai;
Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
12 lest aftir that thou hast ete, and art fillid, hast bildid faire housis, and hast dwellid in tho,
kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
13 and hast droues of oxun, and flockis of scheep, and plente of siluer, and of gold, and of alle thingis, thine herte be reisid,
ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
14 and thenke not on thi Lord God, that ledde thee out of the lond of Egipt, and fro the hous of seruage,
mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
15 and was thi ledere in the greet wildirnesse and ferdful, in which was a serpent brenninge with blast, and scorpioun, and dipsas, and outirli no `watris; which Lord ledde out stremes of the hardeste stoon,
Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
16 and fedde thee with manna in the wildirnesse, which manna thi fadris knewen not. And after that the Lord turmentid thee, and preuede, at the last he hadd mersi on thee,
Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
17 lest thou woldist seie in thin herte, My strengthe, and the myyt of myn hond yaf alle these thingis to me.
Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
18 But thenke thou on thi Lord God, that he yaf strengthis to thee, that he schulde fille his couenaunt, of whiche he swoor to thi fadris, as present dai schewith.
Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
19 Forsothe if thou foryetist thi Lord God, and suest aliene goddis, and worschipist hem `in herte, and onourist `with outforth, lo! now Y biforseie to thee, that thou schalt perische outerli;
Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
20 as hethen men perischiden, whiche the Lord dide awei in thin entryng, so and ye schulen perische, if ye schulen be vnobedient to the vois of youre Lord God.
Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

< Deuteronomy 8 >