< Deuteronomy 6 >

1 These ben the comaundementis, and cerymonyes, and domes, whiche youre Lord God comaundide that Y schulde teche you, and that ye do tho in the lond to which ye passen ouer to welde;
Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
2 that thou drede thi Lord God, and kepe alle hise comaundementis, and heestis, whiche Y comaunde to thee, and to thi sones, and sones of sones, in alle the daies of thi lijf, that thi daies be lengthid.
kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
3 Thou Israel, here, and kepe, that thou do tho thingis whiche the Lord comaundide to thee, and that it be wel to thee, and thou be multiplied more, as the Lord God of thi fadris bihiyte, to yyue to thee a lond flowynge with mylk and hony.
Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
4 Thou Israel, here, thi Lord God is o God.
Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
5 Thou schalt loue thi Lord God of al thin herte, and of al thi soule, and of al thi strengthe.
Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
6 And these wordis whiche Y comaunde to thee to dai, schulen be in thin herte;
Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
7 and thou schalt telle tho to thi sones, and thou schalt thenke on tho, sittynge in thin hows, and goynge in the weie, slepynge, and rysinge.
Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
8 And thou schalt bynde tho as a signe in thin hond; and tho schulen be, and schulen be moued bifor thin iyen; and thou schalt write tho in the lyntel,
Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
9 and in the doris of thin hows.
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
10 And whanne thi Lord God hath brouyt thee in to the lond, for which he swoor to thi fadris, to Abraham, Isaac, and Jacob, and hath youe to thee grete citees, and beeste, whiche thou bildidist not,
Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
11 housis fulle of alle richessis, whiche thou madist not, and cisternes, which thou diggedist not, `places of vynes, and `places of olyues, whiche thou plauntidist not,
nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
12 and thou hast ete, and art fillid,
samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
13 be war diligentli, lest thou foryete the Lord, that ladde thee out of the lond of Egipt, fro the hows of seruage. Thou schalt drede thi Lord God, and thou schalt serue hym aloone, `bi seruyce due to God onely, and thou schalt swere bi his name.
Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
14 Ye schulen not go aftir alien goddis, of alle hethen men that ben `in youre cumpas;
Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
15 for God is a feruent louyere, thi Lord God is in the myddis of thee, lest ony tyme the `strong veniaunce of thi Lord God be wrooth ayens thee, and do awei thee fro `the face of the erthe.
pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
16 Thou schalt not tempte thi Lord God, as thou temptidist in the place of temptyng.
Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
17 Kepe thou the comaundementis of thi Lord God, and the witnessyngis, and cerymonyes, whiche he comaundide to thee;
Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
18 and do thou that that is plesaunt and good in the siyt of the Lord, that it be wel to thee, and that thou entre, and welde the beste lond, of which the Lord swoor to thi fadris,
Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
19 that he schulde do awey alle thin enemyes bifor thee, as he spak.
kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
20 And whanne thi sone schal axe thee to morewe, that is, in tyme comyng, and schal seie, What wolen these witnessyngis, and cerymonyes, and domes to hem silf, whiche oure Lord God comaundide to vs?
Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
21 thou schalt seie to hym, We weren `seruauntis of Farao in Egipt, and the Lord ledde vs out of Egipt, in strong hond;
Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
22 and he dide myraclis, and grete wondris, and werste, `that is, moost peyneful veniaunces, in Egipt, ayens Farao and al his hows, in oure siyt.
Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
23 And he ledde vs out therof, that he schulde yyue to vs led yn, the lond of which he swoor to oure fadris.
Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
24 And the Lord comaundide to vs, that we do alle these lawful thingis, and drede oure Lord God, that it be wel to vs in alle the daies of oure lijf, as it is to dai.
Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
25 And he schal be merciful to vs, if we schulen do and kepe alle hise heestis, bifor oure Lord God, as he comaundide to vs.
Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”

< Deuteronomy 6 >