< Deuteronomy 28 >

1 Forsothe if thou herist the vois of thi Lord God, that thou do and kepe alle hise comaundementis, whiche Y comaunde to thee to dai, thi Lord God schal make the hiyere than alle folkis that lyuen in erthe.
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 And alle these blessyngis schulen come on thee, and schulen take thee; if netheles thou herist hise comaundementis.
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 Thou schalt be blessid in citee, and blessid in feeld;
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 blessid schal be the fruyt of thi wombe, and the fruyt of thi lond, and the fruit of thi beestis; `blessid schulen be the flockis of thi grete beestis, and the fooldis of thi scheep;
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 blessid schulen be thi bernes, and `blessid schulen be `thi relifs;
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 thou schalt be blessid entrynge, and goynge out.
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 The Lord schal yyue thin enemyes fallynge in thi siyt, that schulen rise ayens thee; bi o weie thei schulen come ayens thee, and by seuene weies thei schulen fle fro thi face.
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 The Lord schal sende out blessyng on thi celeris, and on alle the werkis of thin hondis; and he schal blesse thee in the lond which thou hast take.
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 The Lord schal reise thee to hym silf in to an hooli puple, as he swoor to thee, if thou kepist the heestis of thi Lord God, and goist in his weies.
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 And alle the puples of londis schulen se, that the name of the Lord is inwardli clepid on thee, and thei schulen drede thee.
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 The Lord schal make thee to be plenteuouse in alle goodis, in fruyt of thi wombe, and in fruyt of thi beestis, in the fruyt of thi lond, which the Lord swoor to thi fadris, that he schulde yyue to thee.
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 The Lord schal opene his beste tresour, heuene, that he yyue reyn to thi lond in his tyme; and he schal blesse alle the werkis of thin hondis; and thou schalt leene to many folkis, and of no man thou schalt take borewyng.
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 The Lord God schal sette thee in to the heed, and not in to the tail, and euere thou schalt be aboue, and not bynethe; if netheles thou herist the comaundementis of thi Lord God, whiche Y comaunde to thee to day, and kepist,
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 and doist, and bowist not awey fro tho, nether to the riyt side nether to the lefte side, nether suest alien goddis, nethir worschipist hem.
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 That if thou nylt here the vois of thi Lord God, that thou kepe and do alle hise heestis, and cerymonyes, whiche Y comaunde to thee to day, alle these cursyngis schulen come on thee, and schulen take thee.
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 Thou schalt be cursid in citee, cursid in feeld.
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 Cursid `schal be thi berne, and cursid schulen be thi relifs.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 Cursid schal be the fruit of thi wombe, and the fruyt of thi lond; `cursid schulen be the drooues of thin oxun, and the flockis of thi scheep.
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 Thou schalt be cursid goynge in, and `thou schalt be cursid goynge out.
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 The Lord schal sende on thee hungur, and thurst, and blamyng in to alle thi werkis whiche thou schalt do, til he al to-breke thee, and leese swiftli, for thi werste fyndyngis, in whiche thou hast forsake me.
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 The Lord ioyne pestilence to thee, til he waaste thee fro the lond, to which thou schalt entre to welde.
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 The Lord smyte thee with nedynesse, feuyr, and coold, brennynge, and heete, and with corrupt eir, and rust; and pursue thee til thou perische.
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 Heuene which is aboue thee be brasun; and the erthe which thou tredist be yrun.
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 The Lord yyue dust for reyn to thi lond, and aysche come doun fro heuene on thee, til thou be al to-brokun.
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 The Lord yyue thee fallynge bifor thin enemyes; bi o weie go thou ayens hem, and bi seuene weies fle thou, and be thou scaterid bi alle the rewmes of erthe;
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 and thi deed bodi be in to mete to alle volatils of heuene, and to beestis of erthe, and noon be that dryue hem awai.
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 The Lord smyte thee with the botche of Egipt, and `the Lord smyte the part of bodi wherbi `ordures ben voyded; also `the Lord smyte thee with scabbe, and yicchyng, so that thou mayst not be curid.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 The Lord smyte thee with madnesse, and blyndnesse, and woodnesse of thouyt;
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 and grope thou in mydday, as a blynd man is wont to grope in derknessis; and dresse he not thi weies; in al tyme suffre thou fals chaleng, and be thou oppressid bi violence, nethir haue thou ony that schal delyuere thee.
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 Take thou a wijf, and anothir man sleepe with hir; bilde thou an hows, and dwelle thou not ther ynne; plaunte thou a vyner, and gadere thou not grapis therof.
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 Thin oxe be offrid bifor thee, and ete thou not therof; thin asse be rauyschid in thi siyt, and be not yoldun to thee; thi scheep be youun to thin enemyes, and noon be that helpe thee.
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 Thi sones and thi douytris be youun to another puple, `while thin iyen seen, and failen at the siyt of hem al day; and no strengthe be in thin hond.
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 A puple whom thou knowist not ete the fruytis of thi lond, and alle thi trauels; and euere be thou suffrynge fals calengis, and be thou oppressid in alle daies,
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 and wondrynge at the ferdfulnesse of tho thingis whiche thin iyen schulen se.
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 The Lord smyte thee with the worste botche in the knees, and in the hyndere partes of the leg; and thou mow not be heelid fro the sole of the foot `til to the top.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 And the Lord schal lede thee, and thi kyng, whom thou schalt ordeyne on thee, in to a folc which thou knowist not, thou, and thi fadris; and thou schalt serue there to alien goddis, to a tre, and stoon.
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 And thou schalt be lost in to prouerbe, and fable to alle puplis, to whiche the Lord schal brynge thee yn.
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 Thou schalt caste myche seed in to the erthe, and thou schalt gadere litil; for locustis schulen deuoure alle thingis.
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 Thou schalt plaunte, and schalt digge a vyner, and thou schalt not drynke wyn, nether thou schalt gadere therof ony thing; for it schal be wastid with wormes.
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 Thou schalt haue olyue trees in alle thi termes, and thou schalt not be anoyntid with oile; for tho schulen falle doun, and schulen perische.
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 Thou schalt gendre sones and douytris, and thou schalt not vse hem; for thei schulen be led in to caitifte.
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 Rust schal waaste alle thi trees and fruytis of thi lond.
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 A comelyng, that dwellith with thee in the lond, schal stie on thee, and he schal be the hiyere; forsothe thou schalt go doun, and schalt be the lowere.
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 He schal leene to thee, and thou schalt not leene to hym; he schal be in to the heed, and thou schalt be in to the tail.
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 And alle these cursyngis schulen come on thee, and schulen pursue, and schulen take thee, til thou perische; for thou herdist not the vois of thi Lord God, nether kepist hise comaundementis and cerymonyes, whiche he comaundide to thee.
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 And signes, and grete wondris schulen be in thee, and in thi seed, til in to withouten ende;
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 for thou seruedist not thi Lord God in the ioye and gladnesse of herte, for the abundaunce of alle thingis.
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 Thou schalt serue thin enemye, whom God schal sende to thee in hungur, and thirst, and nakidnesse, and in pouert of alle thingis; and he schal putte an yrun yok on thi nol, til he al to-breke thee.
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 The Lord schal brynge on thee a folk fro fer place, and fro the laste endis of erthe, in to the licnesse of an egle fleynge with bire, of which folc thou maist not vnderstonde the langage;
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 a folk moost greedi axere, that schal not yyue reuerence to an elde man, nethir haue mercy on a litil child.
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 And schal deuoure the fruyt of thi beestis, and the fruytis of thi lond, til thou perischist, and schal not leeue to thee wheete, wyn, and oile, droues of oxun, and flockis of scheep,
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 til he leese thee, and al to-breke in alle thi citees, and til thi sadde and hiye wallis be distried, in whiche thou haddist trust in al thi lond. Thou schalt be bisegid withynne thi yatis in al thi lond, which thi Lord God schal yyue to thee.
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 And thou schalt ete the fruyt of thi wombe, and the fleischis of thi sones, and of thi douytris, whiche thi Lord God schal yyue to thee, in the angwisch and distriyng, bi which thin enemye schal oppresse thee.
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 A man delicat of lijf, and `ful letcherouse, schal haue enuye to his brother, and wijf that liggith in his bosum,
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 lest he yyue to hem of the fleischis of hise sones whiche he schal ete; for he hath noon other thing in biseging and pouert, bi which thin enemyes schulen waaste thee with ynne alle thi yatis.
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 A tendur womman and delicat, that myyte not go on the erthe, nether set a step of foot, for most softnesse and tendirnesse, schal haue enuye to hir hosebonde that liggith in hir bosum, on the fleischis of sone and douyter,
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 and on the filthe of skynnes, wherynne the child is wlappid in the wombe, that gon out of the myddis of hir `scharis, ethir hipe bonys, and on fre children that ben borun in the same our. Thei schulen ete `tho children priueli, for the scarsete of alle thingis in bisegyng and distriyng, bi which thin enemy schal oppresse thee with ynne thi yatis.
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 No but thou schalt kepe and do alle the wordis of this lawe, that ben writun in this volym, `ether book, and schalt drede his gloriouse name and ferdful, that is thi Lord God,
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 the Lord schal encreese thi woundis, and the woundis of thi seed; grete woundis and contynuel, sikenessis worste and euerlestinge.
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 And he schal turne in to thee alle the turmentyngis of Egipt, whiche thou dreddist, and tho schulen cleue to thee.
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 Ferthermore the Lord schal brynge on thee also alle the sorewis and woundis, that ben not writun in the volym of this lawe, til he al to-breke thee.
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 And ye schulen dwelle fewe in noumbre, that weren bifore as the sterris of heuene for multitude, for thou herdist not the vois of thi Lord God.
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 And as the Lord was glad bifore on you, and dide wel to you, and multipliede you; so he schal be glad, `and schal leese, and distrie you, that ye be takun awei fro the lond, to which thou schalt entre to welde.
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 The Lord schal leese thee in to alle puplis, fro the hiynesse of erthe `til to the termes therof; and thou schalt serue there to alien goddis, whiche thou knowist not, and thi fadris `knowen not, to trees and stoonys.
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 Also thou schalt not reste in tho folkis, nether rest schal be to the step of thi foot. For the Lord schal yyue to thee there a ferdful herte, and iyen failynge, and lijf waastyd with morenyng.
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 And thi lijf schal be as hangynge bifore thee; thou schalt drede in nyyt and dai, and thou schal not bileue to thi lijf.
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 In the morewtid thou schalt seie, Who schal yyue the euentid to me? and in the euentid `thou schalt seie, Who schal yyue the morewtid to me? for the drede of thin herte, bi which thou schalt be maad aferd, and for tho thingis whiche thou schalt see with thin iyen.
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 The Lord schal lede thee ayen bi schipis in to Egipt, by the weie of which he seide to thee, that thou schuldist no more se it. There thou schalt be seeld to thin enemyes, in to seruauntis and `hand maidis; and noon schal be that schal delyuere thee.
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

< Deuteronomy 28 >