< Deuteronomy 16 >

1 Kepe thou the monethe of newe fruytis, and of the bigynnyng of somer, that thou make pask to thi Lord God; for in this monethe thi Lord God ledde thee out of Egipt in the nyyt.
Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.
2 And thou schalt offre pask to thi Lord God, of scheep and of oxun, in the place which thi Lord God chees, that his name dwelle there.
Mumuphere Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, chiweto chochokera pa nkhosa zanu kapena ngʼombe zanu kumalo kumene Yehova adzasankha kuti akhazikeko dzina lake.
3 Thou schalt not ete `ther ynne breed `diyt with sourdouy; in seuene daies thou schalt ete breed of affliccioun, with out sourdouy, for in drede thou yedist out of Egipt, that thou haue mynde of the dai of thi goyng out of Egipt, in alle the daies of thi lijf.
Musadyere pamodzi ndi buledi wopanga ndi yisiti, koma kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti, buledi wa masautso, chifukwa munachoka ku Igupto mwamsangamsanga kuti pa masiku onse a moyo wanu muzikumbukira nthawi imene munanyamukira ku Igupto.
4 No thing `diyt with sourdouy schal appere in alle thi termes by seuene daies, and of the fleischis of that that is offrid in the euentid, schal not dwelle in the firste dai in the morewtid.
Yisiti asapezeke kwa masiku asanu ndi awiri pa katundu wanu mʼdziko lanu lonse. Ndipo musasunge nyama imene mwapereka nsembe madzulo a tsiku loyamba mpaka mmawa.
5 Thou schalt not mow offre pask in ech of thi citees whiche thi Lord God schal yyue to thee,
Musamangopereka nsembe ya Paska mu mzinda wina uliwonse umene Yehova Mulungu wanu wakupatsani,
6 but in the place which thi Lord God chees, that his name dwelle there; thou schalt offre pask in the euentid, at the goyng doun of the sunne, whanne thou yedist out of Egipt.
koma ku malo wokhawo amene Iye adzawasankhe kukhazikitsako Dzina lake. Kumeneko ndiye muzikapereka nsembe ya Paska madzulo, pamene dzuwa likulowa, pa tsiku lokumbukira kutuluka mu Igupto.
7 And thou schalt sethe, and ete, in the place which thi Lord God hath chose, and thou schalt rise in the morewtid of the secunde dai, and thou schalt go in to thi tabernaclis.
Muyiwotche ndi kuyidya pa malo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. Kenaka mmawa mubwerere ku matenti anu.
8 Bi sixe daies thou schalt ete therf breed; and in the seuenthe dai, for it is the gaderyng of thi Lord God, thou schalt not do werk.
Kwa masiku asanu ndi limodzi muzidya buledi wopanda yisiti ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wa Yehova Mulungu wanu ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
9 Thou schalt noumbre to thee seuene woukis, fro that dai in which thou settidist a sikil in to the corn;
Muziwerenga masabata asanu ndi awiri kuyambira pamene mwatenga chikwakwa ndi kuyamba kumweta tirigu wachilili.
10 and thou schalt halewe the feeste dai of woukis to thi Lord God, a wilful offryng of thyn hond, which thou schalt offre by the blessing of thi Lord God.
Pamenepo muzichita Chikondwerero cha Masabata pamaso pa Yehova Mulungu wanu popereka chopereka chaufulu mofanana ndi madalitso amene Yehova Mulungu wakupatsani
11 And thou schalt ete bifore thi Lord God, thou, and thi sone, and thi douytir, and thi seruaunt, and thin handmayde, and the dekene which is with ynne thi yatis, and the comelynge, and the fadirles ethir modirles child, and the widue, that dwellen with you, in the place `which thi Lord God chees that his name dwelle there.
Ndipo inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi a mʼmizinda mwanu, alendo, ana ndi akazi amasiye okhala pakati panu, mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku malo amene adzawasankhe kukhazikitsako dzina lake.
12 And thou schalt haue mynde for thou were seruaunt in Egipt, and thou schalt kepe and do tho thingis that ben comaundid.
Kumbukirani kuti inunso munali akapolo ku Igupto, ndiye muzitsatira malangizo awa mosamalitsa.
13 And thou schalt halewe the solempnytee of tabernaclis bi seuene daies, whanne thou hast gaderid thi fruytis of the cornfloor, and pressour.
Mukatha kukolola tirigu wanu ndi kupsinya vinyo wanu, muzikhala ndi Chikondwerero cha Misasa kwa masiku asanu ndi awiri.
14 And thou schalt ete in thi feeste dai, thou, and thi sone, and douytir, and thi seruaunt, and handmayde, also the dekene, and comelyng, and the fadirles ether modirles child, and the widewe, that ben with ynne thi yatis, `schulen ete.
Musangalale pa chikondwerero chanu, inu, ana anu aamuna, aakazi, antchito anu aamuna, adzakazi, Alevi, alendo, ana ndi akazi amasiye amene ali mʼmizinda yanu.
15 Bi seuene daies thou schalt halewe feestis to thi Lord God, in the place which the Lord chees; and thi Lord God schal blesse thee, in alle thi fruytis, and in al the werk of thin hondis, and thou schalt be in gladnesse.
Kwa masiku asanu ndi awiri muzichita chikondwererochi kwa Yehova Mulungu wanu kumalo kumene Yehova adzasankhe. Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani inu pa zokolola zanu ndi pa ntchito za manja anu, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
16 In thre tymes bi the yeer al thi male kynde schal appere in the siyt of thi Lord, in the place which he chees, in the solempnyte of therf looues, and in the solempnyte of woukis, and in the solempnyte of tabernaclis. A man schal not appere voide bifor the Lord;
Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu katatu pa chaka ku malo amene Iye adzasankha. Pa Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti, pa Chikondwerero cha Masabata ndi pa Chikondwerero cha Misasa. Munthu aliyense asadzapite pamaso pa Yehova wopanda kanthu mʼmanja mwake.
17 but ech man schal offre vpe this that he hath, bi the blessyng of his Lord God, which he yaf to `that man.
Aliyense wa inu adzabweretse mphatso molingana ndi momwe Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
18 Thou schalt ordeyne `iugis, and maystris, in alle thi yatis whiche thi Lord God schal yyue to thee, bi ech of thi lynagis, that thei deme the puple bi iust doom,
Musankhe oweruza ndi akuluakulu a fuko lanu lililonse mu mzinda uliwonse umene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, ndipo adzaweruza anthuwa mwachilungamo.
19 and bowe not in `to the tother part for fauour, ethir yifte `ayens equete. Thou schalt not take persoone nether yiftis, for whi yiftis blynden the iyen of wise men, `and chaungen the wordis of iust men.
Musamakhotetse chiweruzo kapena kukondera. Musamalandire chiphuphu pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu a nzeru ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
20 Thou schalt pursue iustli that that is iust, that thou lyue and welde the lond which thi Lord God schal yyue to thee.
Tsatani chilungamo chokhachokha basi kuti mukhale ndi moyo ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
21 Thou schalt not plaunte a wode, and ech tre bi the auter of thi Lord God;
Musazike mtengo wina uliwonse wa mafano a Asera pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu,
22 nether thou schalt make to thee, and ordeyne an ymage; whiche thingis thi Lord God hatith.
ndipo musayimike mwala wachipembedzo pakuti Yehova Mulungu wanu amadana nazo zimenezi.

< Deuteronomy 16 >