< 2 Corinthians 1 >

1 Poul, apostle of Jhesu Crist, bi the wille of God, and Tymothe, brothir, to the chirche of God that is at Corinthi, with alle seyntis that ben in al Acaie, grace to you,
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo, Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.
2 and pees of God oure fadir and of the Lord Jhesu Crist.
Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
3 Blessid be God and the fadir of oure Lord Jhesu Crist, fadir of mercies, and God of al coumfort,
Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse.
4 which coumfortith vs in al oure tribulacioun, that also we moun coumforte hem, that ben in al diseese, bi the monestyng bi which also we ben monestid of God.
Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu.
5 For as the passiouns of Crist ben plenteuouse in vs, so also bi Crist oure coumfort is plenteuouse.
Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri.
6 And whether we ben in tribulacioun, for youre tribulacioun and heelthe, ethir we ben coumfortid, for youre coumfort, ethir we ben monestid, for youre monestyng and heelthe. Which worchith in you the suffring of the same passiouns, whiche `we also suffren,
Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife.
7 that oure hope be sad for you; witynge for as ye ben felowis of passiouns, so ye schulen ben also of coumfort.
Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.
8 For, britheren, we wolen that ye wite of oure tribulacioun, that was don in Asie; for ouer maner we weren greued ouer myyt, so that it anoiede vs, yhe, to lyue.
Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo.
9 But we in vs silf hadden answere of deth, that we truste not in vs, but in God that reisith deed men.
Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa.
10 Which delyuerede vs, and delyuerith fro so grete perelis, in to whom we hopen, also yit he schal delyuere,
Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe.
11 while also ye helpen in preier for vs; that of the persones of many faces of that yyuyng that is in vs, thankyngis ben don for vs bi many men to God.
Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.
12 For oure glorie is this, the witnessyng of oure conscience, that in symplenesse and clennesse of God, and not in fleischli wisdom, but in the grace of God, we lyueden in this world, but more plenteuousli to you.
Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu.
13 And we writen not othere thingis to you, than tho that ye han red and knowe, and Y hope that in to the ende ye schulen knowe,
Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa.
14 as also ye han knowe vs a parti; for we ben youre glorie, as also ye ben oure in the dai of oure Lord Jhesu Crist.
Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.
15 And in this tristyng Y wolde first come to you, that ye schulden haue the secounde grace,
Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri.
16 and passe bi you in to Macedonye, and eft fro Macedonye come to you, and of you be led in to Judee.
Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya.
17 But whanne Y wolde this thing, whether Y vside vnstidfastnesse, ether tho thingis that Y thenke, Y thenke aftir the fleisch, that at me be, it is and it is not?
Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”
18 But God is trewe, for oure word that was at you is and is not, is not ther ynne, but is is in it.
Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.”
19 For whi Jhesus Crist, the sone of God, which is prechid among you bi vs, bi me, and Syluan, and Tymothe, ther was not in hym is and is not, but is was in hym.
Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.”
20 For whi hou many euer ben biheestis of God, in thilke is, `that is, ben fillid. And therfor and bi hym we seien amen to God, to oure glorie.
Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu.
21 Sotheli it is God that confermeth vs with you in Crist, and the which God anoyntide vs,
Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife,
22 and which markide vs, and yaf ernes of the spirit in oure hertis.
nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.
23 For Y clepide God to witnesse ayens my soule, that Y sparynge you cam not ouer to Corynthe;
Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni.
24 not that we ben lordis of youre feith, but we ben helperis of youre ioye; for thorouy bileue ye stonden.
Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.

< 2 Corinthians 1 >