< 2 Chronicles 28 >

1 Achaz was of twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede sixtene yeer in Jerusalem; he dide not riytfulnesse in the siyt of the Lord, as Dauid, his fadir, dide;
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 but he yede in the weies of the kyngis of Israel. Ferthermore and he yetyde ymagis to Baalym.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 He it is that brente encense in the valey of Beennon, and purgide hise sones bi fier bi the custom of hethene men, whiche the Lord killide in the comyng of the sones of Israel.
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 Also he made sacrifice, and brente encense in hiy places, and in hillis, and vndur ech tree ful of bowis.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 And `his Lord God bitook hym in the hond of the kyng of Sirie, which smoot Achaz, and took a greet preie of his empire, and brouyten in to Damask. Also Achaz was bitakun to the hondis of the kyng of Israel, and was smytun with a greet wounde.
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 And Facee, the sone of Romelie, killide of Juda sixe scoore thousynde in o dai, alle the men werriours; for thei hadden forsake the Lord God of her fadris.
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 In the same tyme Zechry, a myyti man of Effraym, killide Maasie, the sone of Rogloth, the kyng; and `he killide Ezrica, the duyk of his hows, and Elcana, the secounde fro the kyng.
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 And the sones of Israel token of her britheren two hundrid thousynde of wymmen and of children and of damysels, and prey with out noumbre; and baren it in to Samarie.
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 In that tempest a profete of the Lord, Obed bi name, was there, which yede out ayens the oost comynge in to Samarie, and seide to hem, Lo! the Lord God of youre fadris was wrooth ayens Juda, and bitook hem in youre hondis; and ye han slayn hem crueli, so that youre cruelte stretchide forth in to heuene.
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 Ferthermore ye wolen make suget to you the sones of Juda and of Jerusalem in to seruauntis and handmaidis; which thing is not nedeful to be doon; for ye han synned on this thing to `youre Lord God.
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 But here ye my councel, and lede ayen the prisounneris, whyche ye han brouyt of youre britheren; for greet veniaunce of the Lord neiyith to you.
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 Therfor men of the princes of the sones of Effraym, Azarie, the sone of Johannan, Barachie, the sone of Mosollamoth, Jesechie, the sone of Sellum, and Amasie, the sone of Adali, stoden ayens hem that camen fro the batel;
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 and seiden to hem, Ye schulen not brynge in hidur the prisoneris, lest we doen synne ayens the Lord; whi wolen ye `ley to on youre synnes, and heepe elde trespassis? For it is greet synne; the ire of the strong veniaunce of the Lord neiyeth on Israel.
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 And the men werriouris leften the prey, and alle thingis whiche thei hadden take, bifor the princes and al the multitude.
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 And the men stoden, whiche we remembriden bifore, and thei token the prisounneris, and clothiden of the spuylis alle that weren nakid; and whanne thei hadden clothid hem, and hadden schod, and hadden refreschid with mete and drynke, and hadden anoyntid for trauel, and hadden youe cure, `ether medecyn, to hem; `thei puttiden hem on horsis, whiche euere `myyten not go, and weren feble `of bodi, and brouyten to Jerico, a citee of palmes, to `the britheren of hem; and thei turneden ayen in to Samarie.
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 In that tyme kyng Achaz sente to the kyng of Assiriens, and axide help.
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 And Ydumeis camen, and killiden many men of Juda, and token greet prey.
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 Also Filisteis weren spred abrood bi citees of the feeldis, and at the south of Juda; and thei token Bethsames, and Hailon, and Gaderoth, and Socoth, and Thannan, and Zamro, with her villagis; and dwelliden in tho.
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 For the Lord made low Juda for Achaz, the kyng of Juda; for he hadde maad him nakid of help, and hadde dispisid the Lord.
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 And the Lord brouyte ayens him Teglat Phalasar, kyng of Assiriens, that turmentide hym, and waastide hym, while no man ayenstood.
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 Therfor Achaz, after that he hadde spuylid the hows of the Lord, and the hows of the kyng and of princes, yaf yiftis to the kyng of Assiriens, and netheles it profitide `no thing to hym.
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 Ferthermore also in the tyme of his angwisch he encreesside dispit ayens God; thilke kyng Achaz bi
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 hym silf offride sacrifices to the goddis of Damask, hise smyteris, and seide, The goddis of the kyngis of Sirie helpen hem, whiche goddis Y schal plese bi sacrifices, and thei schulen help me; whanne ayenward thei weren fallyng to hym, and to al Israel.
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 Therfor aftir that Achaz hadde take awei, and broke alle the vessels of the hows of God, he closide the yatis of Goddis temple, and made auteris to hym silf in alle the corneris of Jerusalem.
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 And in alle citees of Juda he bildide auteris to brenne encence, and he stiride the Lord God of hise fadris to wrathfulnesse.
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 Sotheli the residue of hise wordis and of alle hise werkis, the formere and the laste, ben writun in the book of kyngis of Juda and of Israel.
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 And Achaz slepte with hise fadris, and thei birieden hym in the citee of Jerusalem; for thei resseyueden not hym in the sepulcris of the kyngis of Israel; and Ezechie, his sone, regnede for hym.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 28 >