< 2 Chronicles 27 >

1 Joathan was of fyue and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede sixtene yeer in Jerusalem; the name of his modir was Jerusa, the douyter of Sadoch.
Yotamu anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Dzina la amayi ake linali Yerusa mwana wa Zadoki.
2 He dide that, that was riytful bifor the Lord, bi alle thingis whiche Ozie, his fadir, hadde do; outakun that he entride not in to the temple of the Lord, and the puple trespasside yit.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga anachitira Uziya abambo ake, kupatula kuti iyeyo sanalowe mʼNyumba ya Yehova. Komabe anthu anapitirira kuchita zoyipa.
3 He bildide the hiy yate of the hous of the Lord, and he bildide manye thingis in the wal of Ophel;
Yotamu anamanganso chipata chakumtunda cha Nyumba ya Yehova ndipo anagwira ntchito yayikulu yomanga khoma la ku phiri la Ofeli.
4 also he bildide citees in the hillis of Juda, and he bildide castels and touris in forestis.
Iye anamanga mizinda mʼmapiri a ku Yuda ndipo anamanganso malinga ndi nsanja mʼmadera a ku nkhalango.
5 He fauyt ayens the kyng of the sones of Amon, and ouercam hym; and the sones of Amon yauen to hym in that tyme an hundrid talentis of siluer, and ten thousynde choris of barli, and so many of wheete; the sones of Amon yauen these thingis to hym in the secounde and in the thridde yeer.
Yotamu anachita nkhondo ndi mfumu ya Aamoni ndipo anawagonjetsa. Chaka chimenecho Aamoni anapereka makilogalamu 3,400, matani 1,000 a tirigu ndiponso matani 1,000 a barele. Aamoni anabweretsa zinthu zomwezi chaka chachiwiri ndi chachitatu.
6 And Joathan was maad strong, for he hadde dressid hise weies bifor `his Lord God.
Yotamu anakula mphamvu chifukwa anayenda molungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
7 Forsothe the residue of wordis of Joathan, and alle hise batels, and werkis, ben writun in the book of kyngis of Israel and of Juda.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Yotamu, kuphatikizapo nkhondo zake zonse ndi zinthu zina zimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
8 He was of fyue and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede sixtene yeer in Jerusalem.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16.
9 And Joathan slepte with hise fadris, and thei birieden hym in the citee of Dauid; and Achaz, his sone, regnede for him.
Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 27 >