< 2 Chronicles 23 >

1 Forsothe in the seuenthe yeer Joiada was coumfortid, and took centuriouns, that is, Azarie, sone of Jeroboam, and Ismael, the sone of Johannam, and Azarie, the sone of Obeth, and Maasie, the sone of Adaie, and Elisaphat, the sone of Zechri; and he made with hem a counsel and a boond of pees.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 Which cumpassiden Juda, and gaderiden togidere dekenes of alle the citees of Juda, and the princes of the meynees of Israel, and camen in to Jerusalem.
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 Therfor al the multitude made couenaunt in the hows of the Lord with the kyng. And Joiada seide to hem, Lo! the sone of the kyng schal regne, as the Lord spak on the sones of Dauid.
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 Therfor this is the word, which ye schulen do.
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 The thridde part of you that ben comun to the sabat, of preestis, and of dekenes, and of porterys, schal be in the yatis; sotheli the thridde part schal be at the hows of the kyng; and the thridde part schal be at the yate, which is clepid of the foundement. Forsothe al the tother comyn puple be in the large places of the hows of the Lord;
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 and noon other man entre in to the hows of the Lord, no but preestis, and thei that mynystren of the dekenes; oneli entre thei, that ben halewid, and al the tother comyn puple kepe the kepyngis of the Lord.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 Forsothe the dekenes cumpasse the kyng, and ech man haue hise armuris; and if ony othere man entrith in to the temple, be he slayn; and be thei with the kyng entrynge and goynge out.
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 Therfor the dekenes and al Juda diden bi alle thingis, which Joiada, the bischop, hadde comaundid; and alle token the men, that weren with hem, and camen bi the ordre of sabat with hem, that hadden `fillid now the sabat, and schulen go out.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 For Joiada, the bischop, suffride not the cumpenyes to go awei, that weren wont to come oon after `the tother bi ech wouke. And Joiada, the preest, yaf to the centuriouns speris, and scheeldis, and bokeleris of kyng Dauid, whiche he hadde halewid in to the hows of the Lord.
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 And he ordeynede al the puple, of hem `that helden swerdis, at the riyt side of the temple `til to the left side of the temple, bifor the auter and the temple, bi cumpas of the king.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 And thei ledden out the sone of the kyng, and settiden a diademe on hym; and thei yauen to hym in his hond the lawe to be holdun, and thei maden hym kyng. And Joiada, the bischop, and his sones anoyntiden hym; and thei preiden hertli, and seiden, The kyng lyue!
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 And whanne Athalia hadde herd this thing, that is, the vois of men rennynge and preisynge the kyng, sche entride to the puple, in to the temple of the Lord.
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 And whanne sche hadde seyn the kyng stondynge on the grees in the entryng, and the princes and cumpenyes of knyytis aboute hym, and al the puple of the lond ioiynge, and sownynge with trumpis, and syngynge togidere with orguns of dyuerse kynde, and the vois of men preisynge, sche to-rente hir clothis, and seide, Tresouns! tresouns!
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Sotheli Joiada, the bischop, yede out to the centuriouns, and princes of the oost, and seide to hem, Lede ye hir with out the `purseyntis, ethir closyngis, of the temple, and be sche slayn with outforth bi swerd; and the preest comaundide, that sche schulde not be slayn in the hows of the Lord.
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 And thei settiden hondis on hir nol; and whanne she hadde entrid in to the yate of the horsis, of the kyngis hows, thei killiden hir there.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Forsothe Joiada couenauntide a boond of pees bitwixe him silf and al the puple and the kyng, that it schulde be the puple of the Lord.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Therfor al the puple entride in to the hows of Baal, and distrieden it, and braken the auteris and symylacris therof; but thei killiden bifor the auteris Mathan, the preest of Baal.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Forsothe Joiada ordeynede souereyns in the hows of the Lord, that vndur the hondis of preestis, and of dekenes, whiche Dauid departide in the hows of the Lord, thei schulden offre brent sacrifices to the Lord, as it is writun in the book of Moises, in ioie and songis, by the ordynaunce of Dauid.
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 Also he ordeynede porteris in the yatis of the hows of the Lord, that an vnclene man in ony thing schulde not entre in to it.
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 And he took the centuriouns, and strongeste men, and princes of the puple, and al the comyn puple of the lond. And thei maden the kyng to go doun fro the hows of the Lord, and to entre bi the myddis of the hiyere yate in to the hows of the kyng; and thei settiden hym in the kyngis trone.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 And al the puple of the lond was glad, and the citee restide; forsothe Athalia was slayn bi swerd.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.

< 2 Chronicles 23 >