< 1 Samuel 30 >

1 And whanne Dauid and hise men hadden come `in to Sichelech in the thridde dai, men of Amalech hadden maad asauyt on the south part in Sichelech; and thei smytiden Sichelech, and brenten it bi fier.
Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
2 And thei ledden the wymmen prisoneris fro thennus, fro the leeste `til to the grete; and thei hadden not slayn ony, but thei ledden with hem, and yeden in her weie.
Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
3 Therfor whanne Dauid and hise men hadde come to the citee, and hadden founde it brent bi fier, and that her wyues, and her sones, and douytris weren led prisoneris,
Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
4 Dauid and the puple that was with hym reisiden her voices, and weiliden, til teeris failiden in hem.
Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
5 Forsothe also twei wyues of Dauid weren led prisoneris, Achynoem of Jezrael, and Abigail, the wijf of Nabal of Carmele.
Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
6 And Dauid was ful sori; forsothe al the puple wold stone hym, for the soule of ech man was bittir on her sones and douytris. Forsothe Dauid was coumfortid in his Lord God.
Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
7 And he seide to Abiathar, preest, the sone of Achymelech, Bringe thou ephoth to me. And Abiathar brouyte ephoth to Dauid; and Dauid councelide the Lord,
Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
8 and seide, Schal Y pursue, ether nay, `these theues? and schal Y take hem? And the Lord seide to hym, Pursue thou; for with out doute thou schalt take hem, and thou schalt take awey the prey.
Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
9 Therfor Dauid yede, he and sixe hundrid men that weren with hym, and thei camen `til to the stronde of Besor; and sotheli the wery men abididen.
Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
10 Forsothe Dauid pursuede, he and foure hundrid men; for twei hundrid abididen, that weren weeri, and myyten not passe the stronde of Besor.
Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
11 And thei founden a man of Egipte in the feeld, and thei brouyten hym to Dauid; and thei yauen `breed to hym, that he schulde ete, and `schulde drynke watir;
Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
12 but also thei yauen to hym a gobet of a bundel of drye figis, and twei byndyngis of dried grapis. And whanne he hadde ete tho, his spirit turnede ayen, and he was coumfortid; for he hadde not ete breed, nether hadde drunk watir in thre daies and thre nyytis.
Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
13 Therfor Dauid seide to hym, Whos man art thou, ethir fro whennus and whidur goist thou? And he seide, Y am a child of Egipt, the seruaunt of a man of Amalech; forsothe my lord forsook me, for Y bigan to be sijk the thridde dai ago.
Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
14 Sotheli we braken out to the south coost of Cerethi, and ayens Juda, and to the south of Caleb, and we brenten Sichelech bi fier.
Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
15 And Dauid seide to hym, Maist thou lede me to this cumpeny? Which seide, Swere thou to me bi God, that thou schalt not sle me, and schalt not bitake me in to the hondis of my lord; and Y schal lede thee to this cumpeny. And Dauid swoor to hym.
Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
16 And whanne the child hadde ledde hym, lo! thei saten at the mete, on the face of al the erthe, etynge and drynkynge, and as halewynge a feeste, for al the prey and spuylis whiche thei hadden take of the lond of Filisteis, and of the lond of Juda.
Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
17 And Dauid smoot hem fro euentid `til to euentid of the tothir dai, and not ony of hem escapide, no but foure hundrid yonge men, that stieden on camels, and fledden.
Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
18 Forsothe Dauid delyuerede alle thingis whiche the men of Amalech token, and he delyuerede hise twei wyues;
Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
19 nether ony of hem failide fro litil `til to greet, as wel of sones as of douytris, and of spuylis; and what euer thingis thei hadden rauyschid, Dauid ledde ayen alle thingis;
Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
20 and he took alle flockis and grete beestis, and droof bifor his face. And thei seiden, This is the prey of Dauid.
Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
21 Forsothe Dauid cam to twei hundrid men, that weren weeri, and abididen, and myyten not sue Dauid; and he hadde comaundid hem to sitte in the stronde of Besor; whiche yeden out ayens Dauid, and the puple that was with hym. Forsothe Dauid neiyede to the puple, and grette it pesibli.
Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
22 And o man, the werste and vniust of the men that weren with Dauid, answeride, and seide, For thei camen not with vs, we schulen not yyue to hem ony thing of the prey, which we rauyschiden, but his wijf and children `suffice to ech man; and whanne thei han take hem, go thei awei.
Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
23 Forsothe Dauid seide, My britheren, ye schulen not do so of these thingis, whiche the Lord yaf to vs, and kepte vs, and yaf the theues, that braken out ayens vs, in to oure hondis;
Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
24 nether ony man schal here vs on this word. For euene part schal be of him that goith doun to batel, and of hym that dwellith at the fardelis; and in lijk maner thei schulen departe.
Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
25 And this was maad a constitucioun and doom fro that dai and afterward, and as a lawe in Israel til in to this dai.
Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
26 Therfor Dauid cam in to Sichelech, and sente yiftis of the prey to the eldere men of Juda, hise neiyboris, and seide, Take ye blessyng of the prey of enemyes of the Lord;
Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
27 to hem that weren in Bethel, and that weren in Ramoth, at the south,
Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
28 and that weren in Jether, and that weren in Aroer, and that weren in Sephamoth, and that weren in Escama, and that weren in Rethala,
Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
29 and that weren in the citees of Jeramel, and that weren in the citees of Ceny,
Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
30 and that weren in Arama, and that weren in Lautuasam, and that weren in Athec,
a ku Horima, Borasani, Ataki,
31 and that weren in Ebron, and to othere men, that weren in these places, in whiche Dauid dwellide and hise men.
Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.

< 1 Samuel 30 >