< 1 Samuel 26 >

1 And Zipheis camen to Saul in to Gabaa, and seiden, Lo! Dauid is hidde in the hille of Achille, which is `euene ayens the wildirnesse.
Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya nati, “Davide akubisala ku phiri la Hakila, limene limayangʼanana ndi Yesimoni.”
2 And Saul roos, and yede doun in to deseert of Ziph, and with hym thre thousynde of men of the chosun of Israel, that he schulde seke Dauid in the desert of Ziph.
Choncho Sauli ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake 3,000 napita ku chipululu cha Zifi kukafunafuna Davide ku chipululuko.
3 And Saul settide tentis in Gabaa of Achille, that was euen ayens the wildirnesse in the weie. Sotheli Dauid dwellide in deseert. Forsothe Dauid siy that Saul hadde come aftir hym in to deseert;
Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,
4 and Dauid sente aspieris, and lernede moost certeynli, that Saul hadde come thidur.
iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.
5 And Dauid roos priueli, and cam to the place where Saul was. And whanne Dauid hadde seyn the place, wher ynne Saul slepte, and Abner, the sone of Ner, the prince of his chyualrye, and Saul slepynge in the tente, and the tother comyn puple bi his cumpas, Dauid seide to Achymelech,
Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.
6 Ethey, and to Abisai, sone of Saruye, the brother of Joab, `and seide, Who schal go doun with me to Saul in to `the castels? And Abisai seide, Y schal go doun with thee.
Ndipo Davide anafunsa Ahimeleki Mhiti ndi Abisai mwana wa Zeruya, mʼbale wa Yowabu kuti, “Ndani adzapita nane ku msasa kwa Sauli?” Abisai anayankha kuti, “Ine ndidzapita nanu.”
7 Therfor Dauid and Abisai camen to the puple in the nyyt, and thei founden Saul lyggynge and slepynge in `the tente, and a spere sette faste in the erthe at his heed; `forsothe thei founden Abner and the puple slepynge in his cumpas.
Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
8 And Abisay seide to Dauid, God hath closid to dai thin enemy in to thin hondis; now therfor Y schal peerse hym with a spere onys in the erthe, and `no nede schal be the secounde tyme.
Abisai anawuza Davide kuti, “Lero Mulungu wapereka mdani wanu mʼmanja mwanu. Tsopano ndiloleni ndimukhomere pansi ndi mkondo wangawu kamodzinʼkamodzi. Sindimulasa kawiri.”
9 And Dauid seide to Abysai, Sle thou not hym, for who schal holde forth his hond into the crist of the Lord, and schal be innocent?
Koma Davide anamuyankha Abisai kuti, “Usamuphe! Ndani adzapha wodzozedwa wa Yehova ndi kupezeka wosalakwa?
10 And Dauid seide, The Lord lyueth, for no but the Lord smyte hym, ether his dai come that he die, ether he go doun in to batel and perische;
Davide anati, Pali Yehova wamoyo, Yehova mwini ndiye adzamukanthe, mwina tsiku lake lomwalira lidzafika, kapena adzapita ku nkhondo nakaphedwa komweko.
11 the Lord be merciful to me, that Y holde not forth myn hond in to the crist of the Lord; now therfor take thou the spere, which is at his heed, and `take thou the cuppe of watir, and go we awei.
Koma Yehova andiletse kuti ndisapweteke wodzozedwa wa Yehova. Tsopano tingotenga mkondo umene uli ku mutu kwakewo ndi botolo la madzilo ndipo tizipita.”
12 Dauid took the spere, and the cuppe of watir, that was at the heed of Saul, and thei yeden forth, and no man was that siy, and vndirstood, and wakide, but alle men slepten; for the sleep of the Lord `hadde feld on hem.
Motero Davide anatenga mkondo ndi botolo lamadzi zimene zinali ku mutu kwa Sauli ndipo anachoka. Palibe amene anaona zimenezi kapena kudziwa, ndipo palibenso amene anadzuka. Onse anali mʼtulo, chifukwa Yehova anawagonetsa tulo tofa nato.
13 And whanne Dauid hadde passid euene ayens, and hadde stonde on the cop of the hil afer, and a greet space was bitwixe hem,
Pambuyo pake Davide anadutsa nakakwerera mbali ina ya phiri, ndi kuyimirira pamwamba pa phiri patali. Pakati pawo panali mpata waukulu.
14 Dauid criede to the puple, and to Abner, the sone of Ner, and seide, Abner, whether thou schalt not answere? And Abner answeride, and seide, Who art thou, that criest, and disesist the kyng?
Davide anayitana gulu lankhondo ndi Abineri mwana wa Neri nawafunsa kuti, “Kodi sundiyankha ine Abineri?” Abineri anayankha kuti, “Ndiwe yani amene ukuyitana mfumu?”
15 And Dauith seide to Abner, Whether thou art not a man, and what other man is lijk thee in Israel? whi therfor `kepist thou not thi lord the kyng? `For o man of the cumpanye entride, that he schulde sle thi lord the kyng;
Davide anamufunsa Abineri kuti, “Kodi sindiwe mwamuna? Ndipo wofanana nawe ndani mu Israeli? Nʼchifukwa chiyani sunateteze mbuye wako mfumu? Munthu wina anabwera kumeneko.
16 this that thou hast doon, is not good; the Lord lyueth, for ye ben sones of deeth, that kepten not youre lord, the crist of the Lord. Now therfor se thou, where is the spere of the kyng, and where is the cuppe of watir, that weren at his heed.
Chimene wachita iwe si chabwino. Pali Yehova wamoyo iwe ndi asilikali ako muyenera kufa chifukwa simunateteze mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Tayangʼanayangʼana. Uli kuti mkondo wa mfumu ndi botolo lamadzi zimene zinali kumutu kwa mfumu?”
17 Forsothe Saul knew the vois of Dauid, and seide, Whether this vois is thin, my sone Dauid? And Dauid seide, My lord the kyng, it is my vois.
Sauli anazindikira mawu a Davide ndipo anafunsa kuti, “Kodi amenewa ndi mawu ako Davide mwana wanga?” Davide anayankha, “Inde ndi anga, mbuye wanga mfumu.
18 And Dauid seide, For what cause pursueth my lord his seruaunt? What haue Y do, ether what yuel is in myn hond? Now therfor,
Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukundilonda ine mtumiki wanu? Kodi ine ndachita chiyani ndipo ndapezeka ndi cholakwa chotani?
19 my lord the kyng, Y preye, here the wordis of thi seruaunt; if the Lord stirith thee ayens me, the sacrifice be smellid; forsothe if sones of men stiren thee, thei ben cursid in the siyt of the Lord, whiche han cast me out `to dai, that Y dwelle not in the erytage of the Lord, and seien, Go thou, serue thou alien goddis.
Tsopano mbuye wanga mfumu tamverani mawu a mtumiki wanu. Ngati ndi Yehova wautsa mtima wanu kuti mundiwukire, ndiye alandire chipepeso. Koma ngati ndi anthu amene achita zimene, ndiye Yehova awatemberere popeza andipirikitsa lero kundichotsa mʼdziko la Yehova, namati, ‘Pita kapembedze milungu ina.’
20 And now my blood be not sched out in the erthe bifor the Lord; for the kyng of Israel yede out, that he seke a quike fle, as a partrich is pursuede in hillis.
Tsopano musalole kuti magazi anga akhetsedwe kutali ndi Yehova pakuti mfumu ya Israeli yatuluka kudzafunafuna ine nsabwe, monga mmene munthu asakira nkhwali ku mapiri.”
21 And Saul seide, Y synnede; turne ayen, my sone Dauid, for Y schal no more do yuel to thee, for my lijf was precious to day in thin iyen; for it semeth, that Y dide folili, and Y vnknew ful many thingis.
Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
22 And Dauid answeride and seide, Lo! the spere of the kyng, oon of the `children of the kyng passe, and take it; forsothe the Lord schal yelde to ech man bi his riytfulnesse and feith;
Davide anayankha kuti, “Nawu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi wa anyamata anu abwere adzatenge.
23 for the Lord bitook thee to dai in to myn hond, and Y nolde holde forth myn hond in to the crist of the Lord;
Yehova amadalitsa munthu aliyense wolungama ndi wokhulupirika. Yehova anakuperekani lero mʼmanja mwanga, koma ine sindinakhudze wodzozedwa wa Yehova.
24 and as thi lijf is magnified to dai in myn iyen, so my lijf be magnyfied in the iyen of the Lord, and delyuere he me fro al angwisch.
Monga momwe ine lero ndachitira kuwuyesa moyo wanu ngati wamtengowapatali, momwemonso Yehova awuyese moyo wanga wamtengowapatali ndipo andipulumutse mʼmavuto anga onse.”
25 Therfor Saul seide to Dauid, Blessid be thou, my sone Dauid; and sotheli thou doynge schalt do, and thou myyti schalt be myyti. Therfor Dauid yede in to his weie, and Saul turnede ayen in to his place.
Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.

< 1 Samuel 26 >