< 1 Samuel 23 >

1 And thei telden to Dauid, and seiden, Lo! Filisteis fiyten ayens Seila, and rauyschen the corn floris.
Davide atawuzidwa kuti “Onani, Afilisti akuthira nkhondo mzinda wa Keila ndi kulanda zokolola zawo za mʼnkhokwe,”
2 Therfor Dauid councelide the Lord, and seide, Whether Y schal go, and smyte Filisteis? And the Lord seide to Dauid, Go thou, and thou schalt smyte Filisteis, and thou schalt saue Seila.
anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ndikamenyane nawo Afilistiwa?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, kamenyane nawo Afilisti ndi kupulumutsa mzinda wa Keila.”
3 And men, that weren with Dauid, seiden to him, Lo! we ben heere in Judee, and dredden; hou myche more, if we schulen go in to Seila ayens the cumpanyes of Filisteis.
Koma anthu amene anali ndi Davide anati, “Ngati tikuchita mantha ku Yuda konkuno, nanji kupita ku Keila kukamenyana ndi ankhondo a Afilisti!”
4 Therfor eft Dauid councelide the Lord; which answeride, and seide to Dauid, Rise thou, and go `in to Seila; for Y schal bitake Filisteis in thin hond.
Davide anafunsanso Yehova, ndipo Yehova anamuyankha kuti, “Pita ku Keila pakuti ndapereka Afilisti mʼdzanja lako.”
5 Therfor Dauid yede, and hise men, in to Seila, and fauyt ayens Filisteis; and he droof awey her werk beestis, and smoot hem with greet wounde; and Dauid sauyde the dwelleris of Seila.
Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Keila kukamenyana ndi Afilisti. Anapha Afilisti ambiri ndi kutenga ziweto zawo. Choncho anapulumutsa anthu a ku Keila.
6 Forsothe in that tyme, `wher ynne Abiathar, sone of Achymelech, fledde to Dauid in to Seile, he cam doun, and hadde with hym `ephoth, that is, the cloth of the hiyeste preest.
(Pamene Abiatara mwana wa Ahimeleki anathawira kwa Davide anabwera ndi efodi mʼmanja mwake).
7 Forsothe it was teld to Saul, that Dauid hadde come in to Seila; and Saul seide, The Lord hath take hym in to myn hondis, and he `is closid, and entride in to a citee, in which ben yatis and lockis.
Sauli atamva kuti Davide wapita ku Keila anati, “Mulungu wamupereka kwa ine, pakuti Davide wadzitsekera yekha mʼndende polowa mu mzinda umene uli ndi zipata ndi zotsekera zake.”
8 And Saul comaundide to al the puple, that it schulde go doun to batel in to Seila, and bisege Dauid and hise men.
Choncho Sauli anasonkhanitsa ankhondo ake nawatuma ku Keila kuti akamuzungulire Davide ndi anthu ake.
9 And whanne Dauid perceyuede, that Saul made redi yuel priueli to hym, he seide to Abiathar, preest, Brynge hidur ephoth.
Davide atadziwa kuti Sauli akufuna kumuchita chiwembu, anawuza Abiatara wansembe uja kuti, “Bwera nayo efodiyo.”
10 And Dauid seide, Lord God of Israel, thi seruaunt `herde fame, that Saul disposith to come to Seila, that he distrie the citee for me;
Tsono Davide anayankhula ndi Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, ine mtumiki wanu ndamva ndithu kuti Sauli akufuna kubwera ku Keila ndi kudzawononga mzindawu chifukwa cha ine.
11 if the men of Seila schulen bitake me in to hise hondis, and if Saul schal come doun, as thi seruaunt herde, thou Lord God of Israel schewe to thi seruaunt? And the Lord seide, He schal come doun.
Kodi anthu a Keila adzandipereka mʼmanja mwa Sauli? Kodi Sauli abweradi monga ndamvera ine mtumiki wanu? Inu Yehova Mulungu wa Israeli, chonde, ndiwuzeni ine mtumiki wanu.” Ndipo Yehova anati, “Sauli abweradi.”
12 And Dauid seide eft, Whether the men of Seila schulen bitake me, and the men that ben with me, in to the hondis of Saul? And the Lord seide, Thei schulen bitake, `that is, if thou dwellist in the citee, and Saul come thidur.
Davide anafunsanso, “Kodi anthu a ku Keila adzapereka ine ndi anthu angawa kwa Sauli?” Ndipo Yehova anayankha, “Iwo adzakuperekanidi.”
13 Therfor Dauid roos, and hise men, as sixe hundrid; and thei yeden out of Seila, and wandriden vncerteyn hidur and thidur. And it was telde to Saul, that Dauid hadde fledde fro Seila, and was saued; wherfor Saul dissymylide to go out.
Choncho Davide ndi anthu ake, omwe analipo 600, anachoka ku Keila namayenda mothawathawa. Sauli atamva kuti Davide wathawa ku Keila, sanatumizeko ankhondo ake aja.
14 Forsothe Dauid dwellide in the deseert, in strongeste places, and he dwellide in the hil of wildirnesse of Ziph, in a derk hil; netheles Saul souyte hym in alle daies, and the Lord bitook not hym in to the hondis of Saul.
Davide ankakhala mʼmapanga mʼdziko lamapiri ku chipululu cha Zifi. Sauli ankamufufuza tsiku ndi tsiku, koma Mulungu sanapereke Davide mʼmanja mwake.
15 And Dauid siy, that Saul yede out, that he schulde seke his lijf. Forsothe Dauid was in the deseert of Ziph, in a wode.
Davide anaona kuti Sauli akufunafuna kuti amuphe. Nthawiyi nʼkuti Davide ali mʼchipululu cha Zifi ku Horesi.
16 And Jonathas, the sone of Saul, roos, and yede to Dauid in to the wode, and coumfortide hise hondis in God.
Ndipo Yonatani mwana wa Sauli anapita kwa Davide ku Horesi ndipo anamulimbitsa mtima pomuwuza kuti Yehova ali naye.
17 And he seide to Dauid, Drede thou not; for the hond of Saul my fadir schal not fynde thee, and thou schalt regne on Israel, and Y schal be the secounde to thee; but also Saul my father woot this.
Iye anamuwuza kuti, “Usaope, abambo anga sadzakupha. Iwe udzakhala mfumu ya Israeli ndipo ine ndidzakhala wachiwiri wako. Ngakhale abambo anga Sauli akudziwa zimenezi.”
18 Therfor euer eithir smoot boond of pees bifor the Lord. And Dauid dwellide in the wode; forsothe Jonathas turnede ayen in to his hows.
Awiriwa anachita pangano pamaso pa Yehova. Ndipo Yonatani anabwerera kwawo, koma Davide anakhalabe ku Horesi.
19 Forsothe men of Ziph stieden to Saul in Gabaa, and seiden, Lo! whether not Dauid is hid at vs in the sikireste places of the wode, in the hille of Achille, which is at the riyt syde of deseert?
Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya ndipo anamuwuza kuti, “Davide akubisala kwathu, mʼmapanga a ku Horesi, mʼphiri la Hakila, kummwera kwa Yesimoni.
20 Now therfor come thou doun, as thi soule desiride, that thou schuldist come doun; forsothe it schal be oure, that we bitake hym in to the hondis of the kyng.
Tsopano inu, mubwere nthawi iliyonse imene mukufuna, ndipo ife tidzamupereka kwa mfumu.”
21 And Saul seide, Blessid be ye of the Lord, for ye sorewiden `for my stide.
Sauli anayankha kuti, “Yehova akudalitseni pakuti mwandichitira chifundo.
22 Therfor, Y preie, go ye, and make redi more diligentli, and do ye more curiousli ether intentifli, and biholde ye swiftly, where his foot is, ethir who siy hym there, where ye seiden; for he thenkith on me, that felli Y aspie hym.
Pitani mukatsimikizire. Mukaone kumene amakhala ndiponso mupeze munthu amene wamuona. Anthu amandiwuza kuti ndi wochenjera kwambiri.
23 Biholde ye, and se alle his hidyng places, in whiche he is hid, and turne ye ayen to me at a certeyn thing, that Y go with you; that if he closith hym silf yhe in to erthe, Y schal seke hym with alle the thousyndis of Juda.
Kafufuzeni ndithu malo onse kumene amabisalako, ndipo mubwerenso kuno mudzandiwuze chenicheni. Pambuyo pake ine ndidzapita nanu. Ngatidi ali mʼderalo ndidzamusaka pakati pa mabanja onse a Yuda.”
24 And thei risiden, and yeden in to Ziph bifor Saul. Forsothe Dauid and hise men weren in the deseert of Maon, in the feldi places, at the riyt half of Jesymyth.
Kotero iwo ananyamuka ndi kupita ku Zifi, koma Sauli asananyamuke. Nthawi imeneyi Davide ndi anthu ake anali ku chipululu cha Maoni, ku Araba kummwera kwa Yesimoni.
25 Therfor Saul yede and hise felowis to seke Dauid, and it was teld to Dauid; and anoon he yede doun to the stoon, and lyuyde in the deseert of Maon; and whanne Saul hadde herd this, he pursuede Dauid in the deseert of Maon.
Sauli ndi anthu ake anapita kukamufufuza Davide. Koma Davide atamva izi anathawa ndi kukabisala ku thanthwe la chipululu cha Maoni. Sauli atamva kuti Davide anathawira ku Maoni anamutsatira ku chipululu komweko.
26 And Saul yede and hise men at the side of the hil `on o part; forsothe Dauid and hise men weren in the side of the hil on the tother part; sotheli Dauid dispeiride, that he myyte ascape fro the face of Saul. And so Saul and hise men cumpassiden bi the maner of a coroun Dauid and hise men, that thei schulden take hem.
Sauli amayenda mbali ina ya phirilo, ndipo Davide ndi anthu ake nawonso anali mbali ina ya phirilo. Koma Davide ndi anthu ake anafulumira kumuthawa Sauli pamene Sauliyo ndi anthu ake ali pafupi kuwagwira.
27 And a messanger cam to Saul, and seide, Haste thou, and come, for Filisteis han spred hem silf on the lond.
Nthawi yomweyo munthu wina wamthenga anabwera kudzamuwuza Sauli kuti, “Bwerani msanga! Afilisti akuthira nkhondo dzikoli.”
28 Therfor Saul turnede ayen, and ceesside to pursue Dauid; and yede ayens the comyng of Filisteis. For this thing thei clepen that place the Stoon Departynge.
Choncho Sauli analeka kuthamangitsa Davide ndipo anapita kukamenyana ndi Afilisti. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Mwala wa Malekano.
29 Therfor Dauid stiede fro thennus, and dwellide in the sykireste places of Engaddi.
Ndipo Davide anachoka kumeneko ndi kukakhala ku mapanga a ku Eni Gedi.

< 1 Samuel 23 >