< 1 Kings 19 >

1 Forsothe Achab telde to Jezabel alle thingis whiche Elie hadde do, and how he hadde slayn by swerd alle the prophetis of Baal.
Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
2 And Jezabel sente a messanger to Elie, and seide, Goddis do these thingis to me, and adde these thingis, no but to morewe in this our Y schal putte thi lijf as the lijf of oon of hem.
Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
3 Therfor Elie dredde, and roos, and yede whidur euer wille bar hym; and he cam in to Bersabe of Juda, and he lefte there his child;
Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
4 and yede in to deseert, the weie of o dai. And whanne he cam, and sat vndir o iunypere tre, he axide to his soule, that he schulde die; and he seide, Lord, it suffisith to me, take my soule; for Y am not betere than my fadris.
ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
5 And he castide forth hym silf, and slepte in the schadewe of the iunypere tree. And lo! the aungel of the Lord touchide hym, and seide to hym, Rise thou, and ete.
Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
6 He bihelde, and, lo! at his heed was a loof bakun vndur aischis, and a vessel of watir. Therfor he ete, and drank, and slepte eft.
Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
7 And the aungel of the Lord turnede ayen the secounde tyme, and touchide hym; and `the aungel seide to hym, Rise thou, and ete; for a greet weie is to thee.
Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
8 And whanne he hadde rise, he ete, and drank; and he yede in the strengthe of that mete bi fourti dayes and fourti nyytis, `til to Oreb, the hil of God.
Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
9 And whanne he hadde come thidur, he dwellide in a denne; and lo! the word of the Lord `was maad to him, and seide to hym, Elie, what doist thou here?
Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
10 And he answeride, Bi feruent loue Y louede feruentli, for the Lord God of oostis; for the sones of Israel forsoken the couenaunt of the Lord; thei destrieden thin auters, and killiden bi swerd thi prophetis; and Y am left aloone, and thei seken my lijf, that thei do it awei.
Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
11 And he seide to Elie, Go thou out, and stonde in the hil, bifor the Lord. And lo! the Lord passith, and a greet wynde, and strong, turnynge vpsodoun hillis, and al to brekinge stonys bifor the Lord; not in the wynde ys the Lord. And aftir the wynd is a stirynge; not in the stiryng is the Lord.
Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
12 And aftir the stiryng is fier; not in the fier is the Lord. And aftir the fier is the issyng of thinne wynd; there is the Lord.
Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
13 And whanne Elie hadde herd this, he hilide his face with a mentil, and he yede out, and stood in the dore of the denne. And a vois spak to hym, and seide, Elie, what doist thou here?
Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
14 And he answeride, Bi feruent loue Y louede feruentli, for the Lord God of oostis; for the sones of Israel forsoken thi couenaunt; thei distrieden thin auteris, and thei killiden bi swerd thi prophetis; and Y am left aloone, and thei seken my lijf, that thei do it awey.
Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
15 And the Lord seide to hym, Go, and turne ayen in to thi weie, bi the deseert, in to Damask; and whanne thou schalt come thidur, thou schalt anoynte Asahel kyng on Sirie;
Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
16 and thou schalt anoynte kyng on Israel Hieu, the sone of Namsi; sotheli thou schalt anoynte prophete for thee, Elise, sone of Saphat, which is of Abelmeula.
Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
17 And it schal be, who euer schal fle the swerd of Asahel, Hieu schal sle hym; and who euer schal fle the swerd of Hieu, Elise schal sle hym.
Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
18 And Y schal leeue to me in Israel seuene thousynde of men, of whiche the knees ben not bowid bifor Baal, and ech mouth that worschipide not hym, and kisside hond.
Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
19 Therfor Elie yede forth fro thennus, and foond Elise, sone of Saphat, erynge in twelue yockis of oxis; and he was oon in the twelue yockis of oxys, erynge. And whanne Elie hadde come to hym, Elie castide his mentil on hym.
Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
20 Which ran anoon after Elie, whanne the oxis weren left, and seide, Y preie thee, kysse Y my fadir and my modir, and so Y schal sue thee. And Elie seide to hym, Go thou, and turne ayen, for Y haue do to thee that that was myn.
Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
21 `Sotheli he turnede ayen fro Elie, and took tweine oxis, and killide hem; and with the plow of oxis he sethide the fleischis, and yaf to the puple, and thei eeten; and he roos, and yede, and suede Elie, and `mynystride to hym.
Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.

< 1 Kings 19 >