< 1 Kings 16 >

1 Forsothe the word of the Lord was maad to Hieu, sone of Anany, ayens Baasa, and seide,
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 For that that Y reiside thee fro dust, and settide thee duyk on Israel, my puple; sotheli thou yedist in the weie of Jeroboam, and madist my puple Israel to do synne, that thou schuldist terre me to ire, in the synnes of hem; lo!
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 Y schal kitte awey the hyndrere thingis of Baasa, and the hyndrere thingis of `his hows, and Y schal make thin hows as the hows of Jeroboam, sone of Nabath.
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 Doggis schulen ete that man of Baasa, that schal be deed in citee, and briddis of the eyr schulen ete that man of Baasa, that schal die in the feeld.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 Sotheli the residue of wordis of Baasa, and what euer thingis he dide, and hise batels, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kynges of Israel?
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 Therfor Baasa slepte with hise fadris, and he was biried in Thersa; and Hela, his sone, regnede for hym.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 Forsothe whanne the word of the Lord was maad in the hond of Hieu, sone of Anany, ayens Baasa, and ayens his hows, and ayens al yuel which he dide bifor the Lord, to terre hym to ire in the werkis of hise hondis, that he schulde be as the hows of Jeroboam, for this cause he killide hym, that is, Hieu, the prophete, the sone of Anany.
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 In the sixe and twentithe yeer of Aza, kyng of Juda, Hela, the sone of Baasa, regnyde on Israel, in Thersa, twei yeer.
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 And Zamry, `his seruaunt, duyk of the half part of knyytis, rebellide ayens hym; sotheli Hela was in Thersa, and drank, and was drunkun in the hows of Arsa, prefect of Thersa.
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 Therfor Zamri felde in, and smoot, and killide hym, in the seuene and twentithe yeer of Asa, kyng of Juda; and regnede for hym.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 And whanne he hadde regned, and hadde setun on his trone, he smoot al the hows of Baasa, and he lefte not therof a pissere to the wal, and hise kynnesmen, and frendis.
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 And Zamri dide awey al the hows of Baasa, bi the word of the Lord, which he spak to Baasa, in the hond of Hieu, the prophete, for alle the synnes of Baasa,
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 and for the synnes of Hela, his sone, whiche synneden, and maden Israel to do synne, and wraththiden the Lord God of Israel in her vanytees.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Sotheli the residue of the wordis of Hela, and alle thingis whiche he dide, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Israel?
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 In the seuene and twentithe yeer of Aza, kyng of Juda, Zamri regnede seuene daies in Tharsa; forsothe the oost bisegide Gebethon, the citee of Philisteis.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 And whanne it hadde herd, that Zamri hadde rebellid, and hadde slayn the kyng, al Israel made Amry kyng to hem, that was prince of the chyualrye, on Israel, in that dai, in `the castels.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 Therfor Amry stiede, and al Israel with hym, fro Gebethon, and bisegide Thersa.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 Sothely Zamri siy, that the citee schulde be ouercomun, and he entride in to the palis, and brente hym silf with the kyngis hows;
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 and he was deed in hise synnes whiche he synnede, doynge yuel bifor the Lord, and goynge in the weie of Jeroboam, and in hise synnes, bi whiche he made Israel to do synne.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 Sotheli the residue of wordis of Zamri, and of his tresouns, and tyrauntrie, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Israel?
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 Thanne the puple of Israel was departid in to twei partis; the half part of the puple suede Thebny, sone of Geneth, to make hym kyng, and the half part suede Amry.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 Sotheli the puple that was with Amry, hadde maystry ouer the puple that suede Thebny, the sone of Geneth; and Thebny was deed, and Amri regnede.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 In the oon and thrittithe yeer of Aza, kyng of Juda, Amri regnede on Israel, twelue yeer; in Thersa he regnede sixe yeer.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 And he bouyte of Soomeer, for twei talentis of siluer, the hil of Samarie, and `bildide that hil; and he clepide the name of the citee, which he hadde bildid, bi the name of Soomer, lord of the hil of Samarie.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 Forsothe Amry dide yuel in the siyt of the Lord, and wrouyte weiwardli, ouer alle men that weren bifor hym.
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 And he yede in al the weie of Jeroboam, sone of Nabath, and in hise synnes, bi whiche he made Israel to do synne, that he schulde terre to ire, in his vanytees, the Lord God of Israel.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Forsothe the residue of wordis of Amry, and hise batels, which he dide, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Israel?
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 And Amry slepte with hise fadris, and was biried in Samarie; and Achab, his sone, regnede for hym.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Forsothe Achab, the sone of Amry, regnede on Israel, in the `eiyte and thrittithe yeer of Asa, kyng of Juda; and Achab, sone of Amry, regnede on Israel, in Samarie, two and twenti yeer.
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 And Achab, sone of Amry, dide yuel in the siyte of the Lord, ouer alle men that weren bifor hym;
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 and it suffiside not to hym that he yede in the synnes of Jeroboam, sone of Nabath, ferthermore and he weddide a wijf, Jezabel, the douyter of Methaal, kyng of Sydoneis; and he yede, and seruyde Baal, and worschipide hym.
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 And he settide an auter to Baal in the temple of Baal, which he hadde bildid in Samarie, and he plauntide a wode;
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 and Achab addide in his werk, and terride to ire the Lord God of Israel, more thanne alle kyngis of Israel that weren bifor hym.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 Forsothe in hise daies Ahiel of Bethel bildide Jerico; in Abiram, his firste sone, he foundide it, in Segub, his laste sone, he settide yatis therof, bi the word of the Lord, which he hadde spoke in the hond of Josue, sone of Nun.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.

< 1 Kings 16 >