< 1 Chronicles 24 >

1 Forsothe to the sones of Aaron these porciouns schulen be; the sones of Aaron weren Nadab, and Abyud, Eleazar, and Ythamar;
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 but Nadab and Abyud weren deed with out fre children bifor her fadir, and Eleazar and Ythamar weren set in presthod.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 And Dauith departide hem, that is, Sadoch, of the sones of Eleazar, and Achymelech, of the sones of Ithamar, by her whiles and seruyce;
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 and the sones of Eleazar weren founden many mo in the men princes, than the sones of Ythamar. Forsothe he departide to hem, that is, to the sones of Eleazar, sixtene prynces bi meynees; and to the sones of Ythamar eiyte prynces bi her meynees and howsis.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Sotheli he departide euer eithir meynees among hem silf bi lottis; for there weren princes of the seyntuarye, and princes of the hows of God, as wel of the sones of Eleazar as of the sones of Ithamar.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 And Semeye, the sone of Nathanael, a scribe of the lynage of Leuy, discriuede hem bifore the king and pryncis, and bifor Sadoch, the preest, and Achymelech, the sone of Abiathar, and to the prynces of meynees of the preestis and of the dekenes; he discriuyde oon hows of Eleazar, that was souereyn to othere, and `the tother hows of Ithamar, that hadde othere vndir hym.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Forsothe the firste lot yede out to Joiarib, the secounde to Jedeie,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 the thridde to Aharym, the fourthe to Seorym,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 the fyuethe to Melchie,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 the sixte to Maynan, the seuenthe to Accos,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 the eiythe to Abia, the nynthe to Hieusu, the tenthe to Sechema, the elleuenthe to Eliasib,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 the tweluethe to Jacyn,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 the thrittenthe to Opha, the fourtenthe to Isbaal,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 the fiftenthe to Abelga, the sixtenthe to Emmer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 the seuententhe to Ezir, the eiytenthe to Ahapses, the nyntenthe to Pheseye,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 the twentithe to Jezechel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 the oon and twentithe to Jachym, the two and twentithe to Gamul, the thre and twentithe to Dalayam,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 the foure and twentithe to Mazzian.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 These weren the whilis of hem bi her mynysteries, that thei entre in to the hows of God, and bi her custom vndur the hond of Aaron, her fadir, as the Lord God of Israel comaundide.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Forsothe Sebahel was prince of the sones of Leuy that weren resydue, of the sones of Amram; and the sone of Sebahel was Jedeie;
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 also Jesie was prince of the sones of Roobie.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Sotheli Salomoth was prince of Isaaris; and the sone of Salamoth was Janadiath;
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 and his firste sone was Jeriuans, `Amarie the secounde, Azihel the thridde, `Jethmoan the fourthe.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 The sone of Ozihel was Mycha; the sone of Mycha was Samyr;
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 the brother of Mycha was Jesia; and the sone of Jesia was Zacharie.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 The sones of Merary weren Mooli and Musi; the sone of Josyan was Bennon;
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 and the sone of Merarie was Ozian, and Soen, and Zaccur, and Hebri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Sotheli the sone of Mooli was Eleazar, that hadde not fre sones; forsothe the sone of Cys was Jeremyhel;
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 the sones of Musy weren Mooli,
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Eder, Jerymuth. These weren the sones of Leuy, bi the housis of her meynees.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Also and thei senten lottis ayens her britheren, the sones of Aaron, bifor Dauid the kyng, and bifor Sadoch, and Achymelech, and the princes of meynees of preestis and of dekenes; lot departide euenli alle, bothe the gretter and the lesse.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronicles 24 >