< 1 Chronicles 2 >

1 Forsothe the sones of Israel weren Ruben, Symeon, Leuy, Juda, Isachar, and Zabulon,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Joseph, Beniamyn, Neptalym, Gad, Aser.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 The sones of Juda weren Her, Onam, Sela; these thre weren borun to hym of Sue, a douyter of Canaan. Sotheli Her, the first gendrid sone of Juda, was yuel bifor the Lord, and he killide hym.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 Forsothe Thamar, wijf of the sone of Judas, childide to hym Phares, and Zaram; therfor alle the sones of Judas weren fyue.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 Sotheli the sones of Phares weren Esrom, and Chamul.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 And the sones of Zare weren Zamry, and Ethen, and Eman, and Calchab, and Dardan; fyue togidere.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 The sone of Charmy was Achar, that disturblide Israel, and synnede in the theft of thing halewid to the Lord.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 The sone of Ethan was Azarie.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 Sotheli the sones of Esrom, that weren borun to hym, weren Jeramael, and Aram, and Calubi.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 Forsothe Aram gendryde Amynadab. Sotheli Amynadab gendride Naason, the prince of the sones of Juda.
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 And Naason gendride Salmon; of which Salmon Booz was borun.
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 Sotheli Booz gendride Obeth; which hym silf gendride Ysay.
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 Forsothe Ysai gendride the firste gendride sone, Elyab, the secounde, Amynadab; the thridde, Samaa;
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 the fourthe, Nathanael;
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 the fyuethe, Sadai; the sixte, Asom;
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 the seuenthe, Dauyd; whose sistris weren Saruya, and Abigail. The sones of Saruye weren thre, Abisai, Joab, and Asahel.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 Forsothe Abigail childide Amasa, whos fadir was Gether Hismaelite.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 Sotheli Caleph, sone of Esrom, took a wijf, Azuba bi name, of whom he gendride Jerioth; and hise sones weren Jesar, and Sobab, and Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 And whanne Azuba was deed, Caleph took a wijf Effrata, whiche childide Hur to hym.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 Forsothe Hur gendride Hury; Hury gendride Beseleel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 After these thingis Esrom entride to the douytir of Machir, fadir of Galaad, and he took hir, whanne he was of sixti yeer; and sche childide Segub to hym.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 But also Segub gendride Jair; and he hadde in possessioun thre and twenti citees in the lond of Galaad;
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 and he took Gessur, and Aran, the citees of Jair, and Chanath, and the townes therof of seuenti citees. Alle these weren the sones of Machir, fadir of Galaad.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 Sotheli whanne Esrom was deed, Caleph entride in to Effrata. And Esrom hadde a wijf Abia, which childide to hym Assir, fadir of Thecue.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 Forsothe sones weren borun of Jezrameel, the firste gendrid of Esrom; Ram, the first gendrid of hym, and Aran, and Ason, and Achia.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 Also Jezrameel weddide anothir wijf, Athara bi name, that was the modir of Onam.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 But and the sones of Ram, the firste gendrid of Jezrameel, weren Mohas, and Jamyn, and Achaz.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 Forsothe Onam gendride sones, Semey, and Juda. Sotheli the sones of Semei weren Nadab, and Abisur;
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 forsothe the name of the wijf of Abisur was Abigail, that childide to hym Haaobban, and Molid.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 Sotheli the sones of Nadab weren Saled and Apphaym; forsothe Saled diede without children.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 Sotheli the sone of Apphaym was Jesi, which Jesi gendride Sesan; sotheli Sesan gendride Oholi.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 Forsothe the sones of Jada, brother of Semei, weren Jether and Jonathan; but Jether diede with out sones; treuli Jonathan gendride Phalech,
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 and Ziza. These ben the sones of Jerameel.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 Forsothe Sesan hadde not sones, but douytris, and a seruaunt of Egipt, Jeraa bi name;
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 and he yaf his douyter to wijf to Jeraa, whiche childide Ethei to hym.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 Forsothe Ethei gendride Nathan, and Nathan gendride Zadab.
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 Also Zadab gendride Ophial, and Ophial gendride Obed.
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 Obed gendride Yeu, Yeu gendride Azarie,
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 Azarie gendride Helles, Helles gendride Elasa,
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 Elasa gendride Sesamoy, Sesamoy gendride Sellum,
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 Sellum gendride Jecamya, Jecamia gendride Elisama.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 Forsothe the sones of Caleph, brothir of Jerameel, weren Mosa, the firste gendrid sone of hym; thilke is the fadir of Ziph; and the sones of Maresa, the fadir of Hebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 Certis the sones of Ebron weren Chore, and Raphu, Recem, and Samma.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 Forsothe Samma gendride Raam, the fadir of Jerechaam; and Recem gendride Semei.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 The sone of Semei was Maon; and Maon was the fadir of Bethsur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 Sotheli Epha, the secundarie wijf of Caleph, childide Aram, and Musa, and Theser; forsothe Aram gendride Jezen.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 The sones of Jadai weren Regon, and Jethon, and Zesum, Phalez, and Epha, and Saaph.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Matha, the secoundarie wijf of Caleph, childide Zaber, and Tharana.
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 Forsothe Saaph, the fadir of Madmenas, gendride Sue, the fadir of Magbena, and the fader of Gabaa; sotheli the douyter of Caleph was Axa.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 These weren the sones of Caleph. The sones of Hur, the firste gendrid sone of Effrata, weren Sobal, the fader of Cariathiarim;
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma, the fader of Bethleem; Ariph, the fader of Bethgader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 Sotheli the sones of Sobal, fader of Cariatiarim, that siy the myddil of restingis,
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 and was of the kynrede of Caryathiarym, weren Jethrey, and Aphutei, and Samathei, and Maserathei. Of these weren borun Sarytis, and Eschaolitis.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 The sones of Salma, fadir of Bethleem, and of Netophati, weren the corouns of the hows of Joab, and the half of restyng of Sarai.
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 And the kynredis of scryuens, dwellynge in Jabes, syngynge, and sownynge, and dwellynge in tabernaclis. These ben Cyneis, that camen of the heete of the fadir of the hows of Rechab.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Chronicles 2 >