< 1 Chronicles 18 >

1 Forsothe it was doon aftir these thingis, that Dauid smoot Filisteis, and made hem lowe, and took awey Geth and vilagis therof fro the hond of Filisteis;
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 and that he smoot Moab; and Moabitis weren maad seruauntis of Dauid, and brouyten yiftis to hym.
Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
3 In that tyme Dauid smoot also Adadezer, kyng of Soba, of the cuntrey of Emath, whanne he yede for to alarge his empire til to the flood Eufrates.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 Therfor Dauid took a thousynde foure horsid cartis of his, and seuene thousynde of horsmen, and twenti thousynde of foot men; and he hoxide alle the horsis of charis, outakun an hundrid foure horsid cartis, whiche he kepte to hym silf.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Forsothe also Sirus of Damask cam aboue, to yyue help to Adadezer, kyng of Soba, but Dauid smoot also of hise two and twenti thousynde of men;
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 and he settide kniytis in Damask, that Sirie also schulde serue hym, and brynge yiftis. And the Lord helpide hym in alle thingis to whiche he yede.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 And Dauid took goldun arowe caasis, whiche the seruauntis of Adadezer hadden, and he brouyte tho in to Jerusalem;
Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 also and of Thebath and of Chum, the citees of Adadezer, he took ful myche of bras, wherof Salomon made the brasun see, `that is, waischynge vessel, and pileris, and brasun vessels.
Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
9 And whanne Thou, kyng of Emath, hadde herd this thing, `that is, that Dauid hadde smyte al the oost of Adadezer, kyng of Soba,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
10 he sente Aduram, his sone, to Dauid the kyng, for to axe of hym pees, and for to thanke hym, for he hadde ouercome and hadde smyte Adadezer; for whi king Adadezer was aduersarie of Thou.
anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
11 But also kyng Dauid halewide to the Lord alle the vessels of gold, and of siluer, and of bras; and the siluer, and the gold, which the kyng hadde take of alle folkis, as wel of Idumee and Moab, and of the sones of Amon, as of Filisteis and Amalech.
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
12 Forsothe Abisai, the sone of Saruye, smoot Edom in the valei of salt pittis, `ten and eiyte thousynde.
Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
13 And he settide strong hold in Edom, that Ydumei schulde serue Dauid. And the Lord sauide Dauid in alle thingis, to whiche he yede.
Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
14 Therfor Dauid regnede on al Israel, and dide doom and riytwisnesse to al his puple.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
15 Forsothe Joab, the sone of Saruye, was `on the oost; and Josaphat, the sone of Ayluth, was chaunceler;
Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
16 forsothe Sadoch, the sone of Achitob, and Achymalech, the sone of Abyathar, weren preestis; and Susa was scribe;
Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
17 and Banaye, the sone of Joiada, was on the legiouns Cerethi and Phelethi; sotheli the sones of Dauid weren the firste at the hond of the kyng.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.

< 1 Chronicles 18 >