< Leviticus 18 >

1 The LORD said to Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Speak to the children of Israel, and say to them, ‘I am the LORD your God.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
3 You shall not do as they do in the land of Egypt, where you lived. You shall not do as they do in the land of Canaan, where I am bringing you. You shall not follow their statutes.
Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
4 You shall do my ordinances. You shall keep my statutes and walk in them. I am the LORD your God.
Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 You shall therefore keep my statutes and my ordinances, which if a man does, he shall live in them. I am the LORD.
Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
6 “‘None of you shall approach any close relatives, to uncover their nakedness: I am the LORD.
“‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
7 “‘You shall not uncover the nakedness of your father, nor the nakedness of your mother: she is your mother. You shall not uncover her nakedness.
“‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
8 “‘You shall not uncover the nakedness of your father’s wife. It is your father’s nakedness.
“‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
9 “‘You shall not uncover the nakedness of your sister, the daughter of your father, or the daughter of your mother, whether born at home or born abroad.
“‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
10 “‘You shall not uncover the nakedness of your son’s daughter, or of your daughter’s daughter, even their nakedness; for theirs is your own nakedness.
“‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
11 “‘You shall not uncover the nakedness of your father’s wife’s daughter, conceived by your father, since she is your sister.
“‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
12 “‘You shall not uncover the nakedness of your father’s sister. She is your father’s near kinswoman.
“‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
13 “‘You shall not uncover the nakedness of your mother’s sister, for she is your mother’s near kinswoman.
“‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
14 “‘You shall not uncover the nakedness of your father’s brother. You shall not approach his wife. She is your aunt.
“‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
15 “‘You shall not uncover the nakedness of your daughter-in-law. She is your son’s wife. You shall not uncover her nakedness.
“‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
16 “‘You shall not uncover the nakedness of your brother’s wife. It is your brother’s nakedness.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
17 “‘You shall not uncover the nakedness of a woman and her daughter. You shall not take her son’s daughter, or her daughter’s daughter, to uncover her nakedness. They are near kinswomen. It is wickedness.
“‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
18 “‘You shall not take a wife in addition to her sister, to be a rival, to uncover her nakedness, while her sister is still alive.
“‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
19 “‘You shall not approach a woman to uncover her nakedness, as long as she is impure by her uncleanness.
“‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
20 “‘You shall not lie carnally with your neighbor’s wife, and defile yourself with her.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
21 “‘You shall not give any of your children as a sacrifice to Molech. You shall not profane the name of your God. I am the LORD.
“‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
22 “‘You shall not lie with a man as with a woman. That is detestable.
“‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
23 “‘You shall not lie with any animal to defile yourself with it. No woman may give herself to an animal, to lie down with it: it is a perversion.
“‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
24 “‘Don’t defile yourselves in any of these things; for in all these the nations which I am casting out before you were defiled.
“‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
25 The land was defiled. Therefore I punished its iniquity, and the land vomited out her inhabitants.
Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
26 You therefore shall keep my statutes and my ordinances, and shall not do any of these abominations; neither the native-born, nor the stranger who lives as a foreigner among you
Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
27 (for the men of the land that were before you had done all these abominations, and the land became defiled),
pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
28 that the land not vomit you out also, when you defile it, as it vomited out the nation that was before you.
Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
29 “‘For whoever shall do any of these abominations, even the souls that do them shall be cut off from among their people.
“‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
30 Therefore you shall keep my requirements, that you do not practice any of these abominable customs which were practiced before you, and that you do not defile yourselves with them. I am the LORD your God.’”
Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”

< Leviticus 18 >