< Psalms 121 >

1 A Song of Ascents. I will lift up my eyes to the hills. Where does my help come from?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 My help comes from the LORD, who made heaven and earth.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 He will not allow your foot to be moved. He who keeps you will not slumber.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Behold, he who keeps Israel will neither slumber nor sleep.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 The LORD is your keeper. The LORD is your shade on your right hand.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 The sun will not harm you by day, nor the moon by night.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 The LORD will keep you from all evil. He will keep your soul.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 The LORD will keep your going out and your coming in, from this time forward, and forever more.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Psalms 121 >