< Ephesians 1 >

1 Paul, an emissary of Messiah Yeshua through the will of God, to the holy ones who are at Ephesus, and the faithful in Messiah Yeshua:
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
2 Grace to you and peace from God our Father and the Lord Yeshua the Messiah.
Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
3 Blessed be the God and Father of our Lord Yeshua the Messiah, who has blessed us with every spiritual blessing in the heavenly places in Messiah,
Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
4 even as he chose us in him before the foundation of the world, that we would be holy and without defect before him in love,
Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
5 having predestined us for adoption as children through Yeshua the Messiah to himself, according to the good pleasure of his desire,
Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
6 to the praise of the glory of his grace, by which he freely gave us favour in the Beloved.
Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
7 In him we have our redemption through his blood, the forgiveness of our trespasses, according to the riches of his grace
Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
8 which he made to abound towards us in all wisdom and prudence,
chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
9 making known to us the mystery of his will, according to his good pleasure which he purposed in him
Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
10 to an administration of the fullness of the times, to sum up all things in Messiah, the things in the heavens and the things on the earth, in him.
Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
11 We were also assigned an inheritance in him, having been foreordained according to the purpose of him who does all things after the counsel of his will,
Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
12 to the end that we should be to the praise of his glory, we who had before hoped in Messiah.
nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
13 In him you also, having heard the word of the truth, the Good News of your salvation—in whom, having also believed, you were sealed with the promised Holy Spirit,
Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
14 who is a pledge of our inheritance, to the redemption of God’s own possession, to the praise of his glory.
Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
15 For this cause I also, having heard of the faith in the Lord Yeshua which is amongst you and the love which you have towards all the holy ones,
Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
16 don’t cease to give thanks for you, making mention of you in my prayers,
ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
17 that the God of our Lord Yeshua the Messiah, the Father of glory, may give to you a spirit of wisdom and revelation in the knowledge of him,
Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
18 having the eyes of your hearts enlightened, that you may know what is the hope of his calling, and what are the riches of the glory of his inheritance in the holy ones,
Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
19 and what is the exceeding greatness of his power towards us who believe, according to that working of the strength of his might
Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
20 which he worked in Messiah when he raised him from the dead and made him to sit at his right hand in the heavenly places,
imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
21 far above all rule, authority, power, dominion, and every name that is named, not only in this age, but also in that which is to come. (aiōn g165)
Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn g165)
22 He put all things in subjection under his feet, and gave him to be head over all things for the assembly,
Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
23 which is his body, the fullness of him who fills all in all.
umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

< Ephesians 1 >