< Job 4 >

1 Then Eliphaz the Temanite answered,
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 “If someone ventures to talk with you, will you be grieved? But who can withhold himself from speaking?
“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
3 Behold, you have instructed many, you have strengthened the weak hands.
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
4 Your words have supported him who was falling, you have made the feeble knees firm.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
5 But now it has come to you, and you faint. It touches you, and you are troubled.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
6 Isn’t your piety your confidence? Isn’t the integrity of your ways your hope?
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
7 “Remember, now, who ever perished, being innocent? Or where were the upright cut off?
“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
8 According to what I have seen, those who plow iniquity and sow trouble, reap the same.
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
9 By the breath of God they perish. By the blast of his anger are they consumed.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 The roaring of the lion, and the voice of the fierce lion, the teeth of the young lions, are broken.
Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 The old lion perishes for lack of prey. The cubs of the lioness are scattered abroad.
Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
12 “Now a thing was secretly brought to me. My ear received a whisper of it.
“Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 In thoughts from the visions of the night, when deep sleep falls on men,
Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 fear came on me, and trembling, which made all my bones shake.
ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Then a spirit passed before my face. The hair of my flesh stood up.
Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 It stood still, but I couldn’t discern its appearance. A form was before my eyes. Silence, then I heard a voice, saying,
Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 ‘Shall mortal man be more just than God? Shall a man be more pure than his Maker?
‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Behold, he puts no trust in his servants. He charges his angels with error.
Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 How much more those who dwell in houses of clay, whose foundation is in the dust, who are crushed before the moth!
nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Between morning and evening they are destroyed. They perish forever without any regarding it.
Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Isn’t their tent cord plucked up within them? They die, and that without wisdom.’
Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

< Job 4 >