< Job 8 >

1 Then Bildad the Shuhite answered,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “How long will you speak these things? Shall the words of your mouth be a mighty wind?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Does God pervert justice? Or does the Almighty pervert righteousness?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 If your children have sinned against him, he has delivered them into the hand of their disobedience.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 If you want to seek God diligently, make your supplication to the Almighty.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 If you were pure and upright, surely now he would awaken for you, and make the habitation of your righteousness prosperous.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Though your beginning was small, yet your latter end would greatly increase.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 “Please inquire of past generations. Find out about the learning of their fathers.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (For we are but of yesterday, and know nothing, because our days on earth are a shadow.)
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Shall they not teach you, tell you, and utter words out of their heart?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 “Can the papyrus grow up without mire? Can the rushes grow without water?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 While it is yet in its greenness, not cut down, it withers before any other reed.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 So are the paths of all who forget God. The hope of the godless man will perish,
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 whose confidence will break apart, whose trust is a spider’s web.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He will lean on his house, but it will not stand. He will cling to it, but it will not endure.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 He is green before the sun. His shoots go out along his garden.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 His roots are wrapped around the rock pile. He sees the place of stones.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 If he is destroyed from his place, then it will deny him, saying, ‘I have not seen you.’
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Behold, this is the joy of his way. Out of the earth, others will spring.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 “Behold, God will not cast away a blameless man, neither will he uphold the evildoers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 He will still fill your mouth with laughter, your lips with shouting.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Those who hate you will be clothed with shame. The tent of the wicked will be no more.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >