< 1 John 1 >

1 That which was from the beginning, which we have listened to, which we have seen with our own eyes, and our own hands have handled concerning the Word of Life--
Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
2 the Life was manifested, and we have seen and bear witness, and we declare unto you the Life of the Ages which was with the Father and was manifested to us-- (aiōnios g166)
Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios g166)
3 that which we have seen and listened to we now announce to you also, in order that you also may have fellowship in it with us, and this fellowship with us is fellowship with the Father and with His Son Jesus Christ.
Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
4 And we write these things in order that our joy may be made complete.
Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
5 This is the Message which we have heard from the Lord Jesus and now deliver to you--God is Light, and in Him there is no darkness.
Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
6 If, while we are living in darkness, we profess to have fellowship with Him, we speak falsely and are not adhering to the truth.
Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
7 But if we live in the light as He is in the light, we have fellowship with one another, and the blood of Jesus, His Son, cleanses us from all sin.
Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
8 If we claim to be already free from sin, we lead ourselves astray and the truth has no place in our hearts.
Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
9 If we confess our sins, He is so faithful and just that He forgives us our sins and cleanses us from all unrighteousness.
Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
10 If we deny that we have sinned, we make Him a liar, and His Message has no place in our hearts.
Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.

< 1 John 1 >