< Luke 20 >

1 And it came to pass, [that] on one of those days, as he was teaching the people in the temple, and preaching the gospel, the chief priests and the scribes came upon [him], with the elders,
Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
2 And spoke to him, saying, Tell us, By what authority doest thou these things? or who is he that gave thee this authority?
Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
3 And he answered and said to them, I will also ask you one thing; and answer me:
Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
4 The baptism of John, was it from heaven, or from men?
‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
5 And they reasoned with themselves, saying, If we shall say, From heaven; he will say, Why then believed ye him not?
Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
6 But if we say, From men; all the people will stone us: for they are persuaded that John was a prophet.
Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
7 And they answered, that they could not tell whence [it was].
Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
8 And Jesus said to them, Neither do I tell you by what authority I do these things.
Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
9 Then he began to speak to the people this parable; A certain man planted a vineyard, and let it to husbandmen, and went into a far country for a long time.
Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
10 And at the season he sent a servant to the husbandmen, that they should give him of the fruit of the vineyard: but the husbandmen beat him, and sent [him] away empty.
Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
11 And again he sent another servant: and they beat him also, and treated [him] shamefully, and sent [him] away empty.
Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
12 And again he sent the third: and they wounded him also, and cast [him] out.
Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
13 Then said the lord of the vineyard, What shall I do? I will send my beloved son: it may be when they see him they will reverence him.
“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
14 But when the husbandmen saw him, they reasoned among themselves, saying, This is the heir; come, let us kill him, that the inheritance may be ours.
“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
15 So they cast him out of the vineyard, and killed [him]. What therefore will the lord of the vineyard do to them?
Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
16 He will come and destroy these husbandmen, and will give the vineyard to others. And when they heard [it], they said, may that never be.
Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
17 And he beheld them, and said, What is this then that is written, The stone which the builders rejected, the same is become the head of the corner?
Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
18 Whoever shall fall upon that stone, shall be broken: but on whomsoever it shall fall, it will grind him to powder.
Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
19 And the chief priests and the scribes the same hour sought to lay hands on him; and they feared the people: for they perceived that he had spoken this parable against them.
Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
20 And they watched [him], and sent forth spies, who should feign themselves just men, that they might take hold of his words, that so they might deliver him to the power and authority of the governor.
Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
21 And they asked him, saying, Master, we know that thou sayest and teachest rightly, neither acceptest thou the person [of any], but teachest the way of God truly:
Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
22 Is it lawful for us to give tribute to Cesar, or not?
Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
23 But he perceived their craftiness, and said to them, Why tempt ye me?
Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
24 Show me a penny. Whose image and superscription hath it? They answered and said, Cesar's.
“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
25 And he said to them, Render therefore to Cesar the things which are Cesar's, and to God the things which are God's.
Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
26 And they could not take hold of his words before the people: and they marveled at his answer, and held their peace.
Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
27 Then came to [him] certain of the Sadducees (who deny that there is any resurrection) and they asked him,
Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
28 Saying, Master, Moses wrote to us, If any man's brother should die, having a wife, and he should die without children, that his brother should take his wife, and raise up seed to his brother.
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
29 There were therefore seven brothers: and the first took a wife, and died without children.
Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
30 And the second took her for a wife, and he died childless.
Wachiwiri
31 And the third took her; and in like manner the seven also: And they left no children, and died.
ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
32 Last of all the woman died also.
Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
33 Therefore in the resurrection, whose wife of them is she? for seven had her to wife.
Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
34 And Jesus answering, said to them, The children of this world marry, and are given in marriage: (aiōn g165)
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
35 But they who shall be accounted worthy to obtain that world, and the resurrection from the dead, neither marry, nor are given in marriage. (aiōn g165)
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
36 Neither can they die any more: for they are equal to the angels; and are the children of God, being the children of the resurrection.
Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
37 Now that the dead are raised, even Moses showed at the bush, when he calleth the Lord the God of Abraham, and the God of Isaac, and the God of Jacob.
Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
38 For he is not a God of the dead, but of the living: for all live to him.
Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
39 Then certain of the scribes answering, said, Master, thou hast well said.
Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
40 And after that, they durst not ask him any question at all.
Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
41 And he said to them, How say they that Christ is David's son?
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
42 And David himself saith in the book of Psalms, The LORD said to my Lord, Sit thou on my right hand,
Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
43 Till I make thy enemies thy footstool.
mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
44 David therefore calleth him Lord, how is he then his son?
Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
45 Then in the audience of all the people, he said to his disciples,
Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
46 Beware of the scribes, who desire to walk in long robes, and love greetings in the markets, and the highest seats in the synagogues, and the chief rooms at feasts;
“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
47 Who devour widows' houses, and for a show make long prayers: the same shall receive greater damnation.
Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

< Luke 20 >