< Psalms 96 >

1 O sing to the LORD a new song: sing to the LORD, all the earth.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Sing to the LORD, bless his name; show forth his salvation from day to day.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Declare his glory among the heathen, his wonders among all people.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 For the LORD is great, and greatly to be praised: he is to be feared above all gods.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 For all the gods of the nations are idols: but the LORD made the heavens.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Honour and majesty are before him: strength and beauty are in his sanctuary.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Give to the LORD, O ye kindreds of the people, give to the LORD glory and strength.
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Give to the LORD the glory due to his name: bring an offering, and come into his courts.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 O worship the LORD in the beauty of holiness: fear before him, all the earth.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Say among the heathen that the LORD reigneth: the world also shall be established that it shall not be moved: he shall judge the people righteously.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Let the heavens rejoice, and let the earth be glad; let the sea roar, and all it containeth.
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Let the field be joyful, and all that is in it: then shall all the trees of the forest rejoice
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 Before the LORD: for he cometh, for he cometh to judge the earth: he shall judge the world with righteousness, and the people with his truth.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psalms 96 >