< Psalms 8 >

1 To the chief Musician upon Gittith, A Psalm of David. O LORD our Lord, how excellent is thy name in all the earth! who hast set thy glory above the heavens.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
2 Out of the mouth of babes and sucklings hast thou ordained strength because of thy enemies, that thou mightest still the enemy and the avenger.
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 When I consider thy heavens, the work of thy fingers, the moon and the stars, which thou hast ordained;
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
4 What is man, that thou art mindful of him? and the son of man, that thou visitest him?
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 For thou hast made him a little lower than the angels, and hast crowned him with glory and honour.
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 Thou hast made him to have dominion over the works of thy hands; thou hast put all things under his feet:
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 All sheep and oxen, yea, and the beasts of the field;
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
8 The fowl of the air, and the fish of the sea, and whatever passeth through the paths of the seas.
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 O LORD our Lord, how excellent is thy name in all the earth!
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< Psalms 8 >