< Psalms 126 >

1 A Song of degrees. When the LORD turned again the captivity of Zion, we were like them that dream.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
2 Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with singing: then said they among the heathen, The LORD hath done great things for them.
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 The LORD hath done great things for us; for which we are glad.
Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Turn again our captivity, O LORD, as the streams in the south.
Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
5 They that sow in tears shall reap in joy.
Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 He that goeth forth and weepeth, bearing precious seed, shall doubtless return with rejoicing, bringing his sheaves with him.
Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

< Psalms 126 >