< Numbers 7 >

1 And it came to pass on the day that Moses had fully set up the tabernacle, and had anointed it, and sanctified it, and all its instruments, both the altar and all its vessels, and had anointed them, and sanctified them;
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 That the princes of Israel, heads of the house of their fathers, who were the princes of the tribes, and were over them that were numbered, offered:
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 And they brought their offering before the LORD, six covered wagons, and twelve oxen; a wagon for two of the princes, and for each one an ox: and they brought them before the tabernacle.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 And the LORD spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
5 Take it of them, that they may be to perform the service of the tabernacle of the congregation; and thou shalt give them to the Levites, to every man according to his service.
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 And Moses took the wagons and the oxen, and gave them to the Levites.
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 Two wagons and four oxen he gave to the sons of Gershon, according to their service:
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 And four wagons and eight oxen he gave to the sons of Merari, according to their service, under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 But to the sons of Kohath he gave none: because the service of the sanctuary belonging to them was that they should bear upon their shoulders.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 And the princes offered for dedicating the altar in the day that it was anointed, even the princes offered their offering before the altar.
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 And the LORD said to Moses, They shall offer their offering, each prince on his day, for the dedicating of the altar.
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 And he that offered his offering the first day was Nahshon the son of Amminadab, of the tribe of Judah:
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 And his offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them were full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 One spoon of ten shekels of gold, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Nahshon the son of Amminadab.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 On the second day Nethaneel the son of Zuar, prince of Issachar, offered:
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 He offered for his offering one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 One spoon of gold of ten shekels, full of incense:
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Nethaneel the son of Zuar.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 On the third day Eliab the son of Helon, prince of the children of Zebulun, offered:
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Eliab the son of Helon.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 On the fourth day Elizur the son of Shedeur, prince of the children of Reuben, offered:
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 His offering was one silver platter of the weight of an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Elizur the son of Shedeur.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 On the fifth day Shelumiel the son of Zurishaddai, prince of the children of Simeon, offered:
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Shelumiel the son of Zurishaddai.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 On the sixth day Eliasaph the son of Deuel, prince of the children of Gad, offered:
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 His offering was one silver platter of the weight of an hundred and thirty shekels, a silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Eliasaph the son of Deuel.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 On the seventh day Elishama the son of Ammihud, prince of the children of Ephraim, offered:
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Elishama the son of Ammihud.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 On the eighth day offered Gamaliel the son of Pedahzur, prince of the children of Manasseh:
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 His offering was one silver platter of the weight of an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Gamaliel the son of Pedahzur.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 On the ninth day Abidan the son of Gideoni, prince of the children of Benjamin, offered:
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Abidan the son of Gideoni.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 On the tenth day Ahiezer the son of Ammishaddai, prince of the children of Dan, offered:
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Ahiezer the son of Ammishaddai.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 On the eleventh day Pagiel the son of Ocran, prince of the children of Asher, offered:
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Pagiel the son of Ocran.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 On the twelfth day Ahira the son of Enan, prince of the children of Naphtali, offered:
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 His offering was one silver platter, the weight of which was an hundred and thirty shekels, one silver bowl of seventy shekels, after the shekel of the sanctuary; both of them full of fine flour mixed with oil for a meat offering:
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 One golden spoon of ten shekels, full of incense:
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 One young bull, one ram, one lamb of the first year, for a burnt offering:
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 One kid of the goats for a sin offering:
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 And for a sacrifice of peace offerings, two oxen, five rams, five male goats, five lambs of the first year: this was the offering of Ahira the son of Enan.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 This was the dedication of the altar, in the day when it was anointed, by the princes of Israel: twelve platters of silver, twelve silver bowls, twelve spoons of gold:
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 Each platter of silver weighing an hundred and thirty shekels, each bowl seventy: all the silver vessels weighed two thousand and four hundred shekels, after the shekel of the sanctuary:
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 The golden spoons were twelve, full of incense, weighing ten shekels apiece, after the shekel of the sanctuary: all the gold of the spoons was an hundred and twenty shekels.
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 All the oxen for the burnt offering were twelve bulls, the rams twelve, the lambs of the first year twelve, with their meat offering: and the kids of the goats for sin offering twelve.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 And all the oxen for the sacrifice of the peace offerings were twenty and four bulls, the rams sixty, the male goats sixty, the lambs of the first year sixty. This was the dedication of the altar, after it was anointed.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 And when Moses had entered into the tabernacle of the congregation to speak with him, then he heard the voice of one speaking to him from off the mercy seat that was upon the ark of testimony, from between the two cherubim: and he spoke to him.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

< Numbers 7 >