< Hosea 5 >

1 Hear ye this, O priests; and hearken, ye house of Israel; and give ye ear, O house of the king; for judgment is toward you, because ye have been a snare on Mizpah, and a net spread upon Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 And the revolters are gone deeply into slaughter, though I have been a rebuker of them all.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 I know Ephraim, and Israel is not hid from me: for now, O Ephraim, thou committest harlotry, and Israel is defiled.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 They will not frame their doings to turn to their God: for the spirit of harlotry is in the midst of them, and they have not known the LORD.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 And the pride of Israel doth testify to his face: therefore shall Israel and Ephraim fall in their iniquity; Judah also shall fall with them.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 They shall go with their flocks and with their herds to seek the LORD; but they shall not find him; he hath withdrawn himself from them.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 They have dealt treacherously against the LORD: for they have begotten strange children: now shall a month devour them with their portions.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Blow ye the horn in Gibeah, and the trumpet in Ramah: cry aloud at Bethaven, after thee, O Benjamin.
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Ephraim shall be desolate in the day of rebuke: among the tribes of Israel have I made known that which shall surely be.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 The princes of Judah were like them that remove a landmark: therefore I will pour out my wrath upon them like water.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Ephraim is oppressed and broken in judgment, because he willingly walked after the commandment.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 Therefore will I be to Ephraim as a moth, and to the house of Judah as rottenness.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 When Ephraim saw his sickness, and Judah saw his wound, then Ephraim went to the Assyrian, and sent to king Jareb: yet he could not heal you, nor cure you of your wound.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 For I will be to Ephraim as a lion, and as a young lion to the house of Judah: I, even I, will tear and go away; I will take away, and none shall rescue him.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 I will go and return to my place, till they acknowledge their offence, and seek my face: in their affliction they will seek me early.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

< Hosea 5 >