< Exodus 21 >

1 Now these are the judgments which thou shalt set before them.
“Uwawuze Aisraeli malamulo awa:
2 If thou shalt buy an Hebrew servant, six years he shall serve: and in the seventh he shall depart free for nothing.
“Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.
3 If he came in by himself, he shall depart by himself: if he was married, then his wife shall depart with him.
Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.
4 If his master hath given him a wife, and she hath borne him sons or daughters; the wife and her children shall be her master’s, and he shall depart by himself.
Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.
5 And if the servant shall plainly say, I love my master, my wife, and my children; I will not depart free:
“Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’
6 Then his master shall bring him to the judges; he shall also bring him to the door, or to the door post; and his master shall bore his ear through with an awl; and he shall serve him for ever.
mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.
7 And if a man shall sell his daughter to be a female slave, she shall not depart as the male slaves do.
“Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.
8 If she shall not please her master, who hath betrothed her to himself, then shall he let her be redeemed: to sell her to a strange nation he shall have no power, seeing he hath dealt deceitfully with her.
Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye.
9 And if he hath betrothed her to his son, he shall deal with her after the manner of daughters.
Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi.
10 If he shall take him another wife; her food, her raiment, and her duty of marriage, shall he not diminish.
Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake.
11 And if he shall not perform these three things for her, then shall she depart free without money.
Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.
12 He that smiteth a man, so that he die, shall be surely put to death.
“Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa.
13 And if a man shall not lie in wait, but God shall deliver him into his hand; then I will appoint thee a place where he shall flee.
Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani.
14 But if a man shall come presumptuously upon his neighbour, to slay him with guile; thou shalt take him from my altar, that he may die.
Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.
15 And he that smiteth his father, or his mother, shall be surely put to death.
“Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.
16 And he that stealeth a man, and selleth him, or if he shall be found in his hand, he shall surely be put to death.
“Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.
17 And he that curseth his father, or his mother, shall surely be put to death.
“Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.
18 And if men contend together, and one shall smite another with a stone, or with his fist, and he shall not die, but keepeth to his bed:
“Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi,
19 If he shall rise again, and walk abroad upon his staff, then shall he that smote him be clear: only he shall pay for the loss of his time, and shall cause him to be thoroughly healed.
kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.
20 And if a man shall smite his male or female servant, with a rod, and he shall die under his hand; he shall be surely punished.
“Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa.
21 However, if he shall continue a day or two, he shall not be punished: for he is his money.
Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.
22 If men shall contend, and hurt a woman with child, so that her fruit shall depart from her, and yet no harm follow: he shall be surely punished, according as the woman’s husband will lay upon him; and he shall pay as the judges determine.
“Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza.
23 And if any harm shall follow, then thou shalt give life for life,
Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo,
24 Eye for eye, tooth for tooth, hand for hand, foot for foot,
diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi.
25 Burning for burning, wound for wound, stripe for stripe.
Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.
26 And if a man shall smite the eye of his male servant, or the eye of his female servant, that it shall perish; he shall let him go free for his eye’s sake.
“Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake.
27 And if he shall smite out his male servant’s tooth, or his female servant’s tooth; he shall let him go free for his tooth’s sake.
Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.
28 If an ox shall gore a man or a woman, that they die: then the ox shall be surely stoned, and his flesh shall not be eaten; but the owner of the ox shall be clear.
“Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu.
29 But if the ox was accustomed to push with his horn in time past, and it hath been testified to his owner, and he hath not restrained him, but that he hath killed a man or a woman; the ox shall be stoned, and his owner also shall be put to death.
Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso.
30 If there shall be laid on him a sum of money, then he shall give for the ransom of his life whatever is laid upon him.
Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.
31 Whether he hath gored a son, or hath gored a daughter, according to this judgment shall it be done to him.
Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi.
32 If the ox shall push a male or female servant; he shall give to their master thirty shekels of silver, and the ox shall be stoned.
Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.
33 And if a man shall open a pit, or if a man shall dig a pit, and not cover it, and an ox or a donkey shall fall into it;
“Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo,
34 The owner of the pit shall make payment, and give money to the owner of them; and the dead beast shall be his.
mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.
35 And if one man’s ox shall hurt another’s, that he shall die; then they shall sell the live ox, and divide the money of it; and the dead ox also they shall divide.
“Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija.
36 Or if it shall be known that the ox was accustomed to push in time past, and his owner hath not restrained him; he shall surely pay ox for ox; and the dead shall be his own.
Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”

< Exodus 21 >