< 1 Kings 4 >

1 So king Solomon was king over all Israel.
Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
2 And these were the princes which he had; Azariah the son of Zadok the priest,
Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
3 Elihoreph and Ahiah, the sons of Shisha, scribes; Jehoshaphat the son of Ahilud, the recorder.
Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
4 And Benaiah the son of Jehoiada was over the army: and Zadok and Abiathar were the priests:
Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
5 And Azariah the son of Nathan was over the officers: and Zabud the son of Nathan was principal officer, and the king’s friend:
Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
6 And Ahishar was over the household: and Adoniram the son of Abda was over the forced labour.
Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
7 And Solomon had twelve officers over all Israel, who provided food for the king and his household: each man his month in a year made provision.
Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
8 And these are their names: The son of Hur, in mount Ephraim:
Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
9 The son of Dekar, in Makaz, and in Shaalbim, and Bethshemesh, and Elonbethhanan:
Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
10 The son of Hesed, in Aruboth; to him pertained Sochoh, and all the land of Hepher:
Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
11 The son of Abinadab, in all the region of Dor; who had Taphath the daughter of Solomon for a wife:
Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
12 Baana the son of Ahilud; to him pertained Taanach and Megiddo, and all Bethshean, which is by Zartanah beneath Jezreel, from Bethshean to Abelmeholah, even to the place that is beyond Jokneam:
Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
13 The son of Geber, in Ramothgilead; to him pertained the towns of Jair the son of Manasseh, which are in Gilead; to him also pertained the region of Argob, which is in Bashan, sixty great cities with walls and brasen bars:
Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
14 Ahinadab the son of Iddo had Mahanaim:
Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
15 Ahimaaz was in Naphtali; he also took Basmath the daughter of Solomon for a wife:
Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
16 Baanah the son of Hushai was in Asher and in Aloth:
Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
17 Jehoshaphat the son of Paruah, in Issachar:
Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
18 Shimei the son of Elah, in Benjamin:
Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
19 Geber the son of Uri was in the country of Gilead, in the country of Sihon king of the Amorites, and of Og king of Bashan; and he was the only officer who was in the land.
Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
20 Judah and Israel were many, as the sand which is by the sea in multitude, eating and drinking, and making merry.
Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
21 And Solomon reigned over all kingdoms from the river to the land of the Philistines, and to the border of Egypt: they brought presents, and served Solomon all the days of his life.
Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
22 And Solomon’s provision for one day was thirty measures of fine flour, and sixty measures of meal,
Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
23 Ten fat oxen, and twenty oxen out of the pastures, and an hundred sheep, besides harts, and roebucks, and fallowdeer, and fatted fowls.
ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
24 For he had dominion over all the region on this side the river, from Tiphsah even to Azzah, over all the kings on this side of the river: and he had peace on all sides around him.
Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
25 And Judah and Israel dwelt safely, every man under his vine and under his fig tree, from Dan even to Beersheba, all the days of Solomon.
Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
26 And Solomon had forty thousand stalls of horses for his chariots, and twelve thousand horsemen.
Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
27 And those officers provided food for king Solomon, and for all that came to king Solomon’s table, every man in his month: they lacked nothing.
Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
28 Barley also and straw for the horses and dromedaries they brought to the place where the officers were, every man according to his charge.
Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
29 And God gave Solomon great wisdom and understanding, and largeness of heart, even as the sand that is on the sea shore.
Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
30 And Solomon’s wisdom excelled the wisdom of all the children of the east country, and all the wisdom of Egypt.
Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
31 For he was wiser than all men; than Ethan the Ezrahite, and Heman, and Chalcol, and Darda, the sons of Mahol: and his fame was in all the surrounding nations.
Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
32 And he spoke three thousand proverbs: and his songs were a thousand and five.
Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
33 And he spoke of trees, from the cedar tree that is in Lebanon even to the hyssop that springeth out of the wall: he spoke also of beasts, and of fowls, and of creeping things, and of fishes.
Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
34 And there came of all people to hear the wisdom of Solomon, from all kings of the earth, who had heard of his wisdom.
Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.

< 1 Kings 4 >