< Job 8 >

1 Then Bildad the Shuhite answered and said,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “How long will you say these things? How long will the words of your mouth be a mighty wind?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Does God pervert justice? Does the Almighty pervert righteousness?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Your children have sinned against him; we know this, for he gave them into the hand of their sins.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 But suppose you diligently sought God and presented your request to the Almighty.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 If you are pure and upright, then he would surely stir himself on your behalf and restore you to your rightful place.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Even though your beginning was small, still your final condition would be much greater.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Please ask the former generations, and give your attention to what our ancestors learned.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (We were only born yesterday and know nothing because our days on earth are a shadow).
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Will they not teach you and tell you? Will they not speak words from their hearts?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Can papyrus grow without a marsh? Can reeds grow without water?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 While they are still green and not cut down, they wither before any other plant.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 So also are the paths of all who forget God; the hope of the godless will perish.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 His confidence will break apart, and his trust is as weak as a spider's web.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He leans on his house, but it will not support him; he takes hold of it, but it does not stand.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Under the sun he is green, and his shoots go out over his entire garden.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 His roots are wrapped about the heaps of stone; they look for good places among the rocks.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 But if this person is destroyed out of his place, then that place will deny him and say, 'I never saw you.'
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 See, this is the “joy” of such a person's behavior; other plants will sprout out of the same soil in his place.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 See, God will not cast away an innocent man; neither will he take the hand of evildoers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 He will yet fill your mouth with laughter, your lips with shouting.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Those who hate you will be clothed with shame; the tent of the wicked will be no more.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >