< Genesis 12 >

1 Now Yahweh said to Abram, “Go from your country, and from your relatives, and from your father's household, to the land that I will show you.
Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
2 I will make of you a great nation, and I will bless you, and make your name great, and you will be a blessing.
“Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
3 I will bless those who bless you, but whoever dishonors you I will curse. Through you will all the families of the earth be blessed.”
Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
4 So Abram went, as Yahweh had told him to do, and Lot went with him. Abram was seventy-five years old when he left Haran.
Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
5 Abram took Sarai, his wife, Lot, his brother's son, all their possessions that they had accumulated, and the people that they had acquired in Haran. They left to go into the land of Canaan, and came to the land of Canaan.
Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
6 Abram passed through the land as far as Shechem, to the oak of Moreh. At that time the Canaanites lived in the land.
Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
7 Yahweh appeared to Abram, and said, “To your descendants I will give this land.” So there Abram built an altar to Yahweh, who had appeared to him.
Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
8 From there he moved to the hill country to the east of Bethel, where he pitched his tent, with Bethel to the west and Ai to the east. There he built an altar to Yahweh and called on the name of Yahweh.
Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
9 Then Abram continued journeying, going toward the Negev.
Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
10 There was a famine in the land, so Abram went down into Egypt to stay, for the famine was severe in the land.
Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
11 When he was about to enter into Egypt, he said to Sarai his wife, “See here, I know that you are a beautiful woman.
Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
12 When the Egyptians see you they will say, 'This is his wife,' and they will kill me, but they will keep you alive.
Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
13 Say that you are my sister, so that it may be well with me because of you, and so that my life will be spared because of you.”
Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
14 It came about that when Abram entered into Egypt, the Egyptians saw that Sarai was very beautiful.
Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
15 The princes of Pharaoh saw her, and praised her to Pharaoh, and the woman was taken into Pharaoh's household.
Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
16 Pharaoh treated Abram well for her sake, and gave him sheep, oxen, male donkeys, male servants, female servants, female donkeys, and camels.
Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
17 Then Yahweh afflicted Pharaoh and his house with great plagues because of Sarai, Abram's wife.
Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
18 Pharaoh summoned Abram, and said, “What is this that you have done to me? Why did you not tell me that she was your wife?
Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
19 Why did you say, 'She is my sister,' so that I took her to be my wife? Now therefore, here is your wife. Take her, and go your way.”
Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
20 Then Pharaoh gave orders to his men concerning him, and they sent him away, along with his wife and all that he had.
Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

< Genesis 12 >