< 2 Samuel 7 >

1 It happened that after the king had settled in his house, and after Yahweh had given him rest from all his surrounding enemies,
Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
2 the king said to Nathan the prophet, “Look, I am living in a house of cedar, but the ark of God is staying in the middle of a tent.”
mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 Then Nathan said to the king, “Go, do what is in your heart, for Yahweh is with you.”
Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 But that same night the word of Yahweh came to Nathan, saying,
Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 “Go and tell David my servant, 'This is what Yahweh says: Will you build me a house in which to live?
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
6 For I have not lived in a house from the day that I brought up the people of Israel out of Egypt until this present day; instead, I have been moving about in a tent, a tabernacle.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
7 In all places where I have moved among all the people of Israel, did I ever say anything to any of Israel's leaders whom I appointed to shepherd my people Israel, saying, “Why have you not built me a house of cedar?”'”
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
8 Now then, tell my servant David, “This is what Yahweh of hosts says: 'I took you from the pasture, from following the sheep, so that you would be ruler over my people Israel.
“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
9 I have been with you wherever you went. I have cut off all your enemies from before you. Now I will make your name great, like the names of the great ones of the earth.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
10 I will appoint a place for my people Israel and will plant them there, so that they may live in their own place and be troubled no more. No longer will wicked people oppress them, as they did before,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
11 as they were doing from the days that I commanded judges to be over my people Israel. Now I will give you rest from all your enemies. Moreover, I, Yahweh declare to you that I will make you a house.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
12 When your days are fulfilled and you lie down with your fathers, I will raise up a descendant after you, one who will come out from your body, and I will establish his kingdom.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
13 He will build a house for my name, and I will establish the throne of his kingdom forever.
Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
14 I will be a father to him, and he will be my son. When he sins, I will discipline him with the rod of men and with the whipping of the sons of men.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
15 But my covenant faithfulness will not leave him, as I took it from Saul, whom I removed from before you.
Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
16 Your house and kingdom will be confirmed forever before you. Your throne will be established forever.'”
Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
17 Nathan spoke to David and reported to him all these words, and he told him about the entire vision.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
18 Then David the king went in and sat before Yahweh and said, “Who am I, Yahweh God, and what is my family that you have brought me to this point?
Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
19 Now this was a small thing in your sight, Lord Yahweh. You have even spoken about your servant's family for a great while to come, and have shown me future generations, Lord Yahweh!
Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 What more can I, David, say to you? You have known your servant, Lord Yahweh.
Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
21 For your word's sake, and to fulfill your own purpose, you have done this great thing and revealed it to your servant.
Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 Therefore you are great, Lord Yahweh, for there is no one like you, and there is no God besides you, as we have heard with our own ears.
Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
23 What nation is like your people Israel, the one nation on earth whom you, God, went and rescued for yourself? You did this so that they would become a people for yourself, to make a name for yourself, and to do great and fearful deeds for your land. You drove out nations and their gods from before your people, whom you rescued from Egypt.
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
24 You established Israel as your own people forever, and you, Yahweh, became their God.
Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 So now, Yahweh God, may the promise that you made concerning your servant and his family be established forever. Do as you have spoken.
“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
26 May your name be forever great, so the people will say, 'Yahweh of hosts is the God of Israel,' while the house of me, David, your servant is established before you.
kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 For you, Yahweh of hosts, the God of Israel, have revealed to your servant that you will build him a house. That is why I, your servant, have found courage to pray to you.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
28 Now, Lord Yahweh, you are God, and your words are trustworthy, and you have made this good promise to your servant.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
29 Now then, let it please you to bless the house of your servant, so that it may continue forever before you. For you, Lord Yahweh, have said these things, and with your blessing your servant's house will be blessed forever.”
Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 2 Samuel 7 >