< Ruth 3 >

1 One day, Naomi said to Ruth, “My daughter, I think that I should [RHQ] try to arrange for you to have a husband [MTY] who will (take care of/provide for) you.
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 Boaz, the man with whose [servant] girls you have been [gathering grain], is a close relative [of our dead husbands]. Listen [carefully]. Tonight he will be at the ground where [the barley has] been threshed. He will be separating the barley grain from the chaff.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 Bathe yourself and put on some perfume. Put on your [best] clothes. Then go down to the ground where they have threshed [the grain]. But do not let Boaz know that you are there while he is eating [supper] and drinking.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 [When he has finished eating], notice where he lies down to sleep. Then [when he is asleep], take the blanket off his feet and lie [close to his feet]. [When he wakes up], he will tell you what to do.”
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 Ruth replied, “I will do everything that you have told me [to do].”
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 So she went down to the ground where they had threshed [the barley grain]. There she did everything that her mother-in-law had told her [to do].
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 When Boaz finished eating [supper] and drinking [wine], he felt happy. Then he went over to the far end of the pile of grain. He lay down [and went to sleep]. Then Ruth approached him quietly. She took the blanket off his feet and lay down [there].
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 In the middle of the night, he suddenly awoke. He sat up and saw that a woman was lying at his feet.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 He asked her, “Who are you?” She replied, “I am your servant, Ruth. Since you are the one who has a responsibility to take care of [someone like me whose dead husband was] your close relative, spread the corner of your cloak over my [feet to show that you will marry me].”
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 Boaz replied, “Young lady, I hope that Yahweh will (bless/be kind to) you! You have acted kindly [toward your mother-in-law], and now you are acting even more kindly [toward me by wanting to marry me, instead of wanting to marry a young man]. You have not looked for either a rich young man or a poor young man, [to marry him].
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 Now, young lady, I will do everything you ask. Don’t worry [that people in this town might think I am doing wrong by marrying you because you are a woman from Moab]. All the people in this town know that you are an honorable woman.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 But [there is one problem]. Although it is true that I am a close relative [of your mother-in-law’s dead husband], there is another man who is a closer relative [than I am], and therefore he should be the one to [marry you and] take care of you.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 You stay here for the rest of this night. Tomorrow morning [I will tell this man about you]. If he says that he will [marry you and] take care of you, fine, [we will] let him do that. But if he is not willing [to do that], I solemnly promise that as surely as Yahweh lives, I will [marry you and] take care of you. So lie/sleep here until it is morning.”
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 So she lay at his feet until morning. But she got up and left before it was light enough that people would be able to recognize her, because Boaz said, “I do not want anyone to know that a woman was here.”
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 He also said to her, “Bring to me your cloak and spread it out.” When she did that, he poured into it six measures/24 liters/50 pounds of barley, and put in on her back. Then he (OR, she) went back to the town.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 When Ruth arrived home, her mother-in-law asked her, “My daughter, how did (things go/Boaz act toward you)?” Then Ruth told her everything that Boaz had done for her [and said to her].
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 She also said [to Naomi], “He gave me all this barley, saying ‘I do not want you to return to your mother-in-law empty-handed.’”
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 Then Naomi said, “My daughter, just wait until we see what happens. [I am sure that] Boaz will take care of [LIT] the matter [of your marriage]. [LIT]”
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

< Ruth 3 >