< Obadiah 1 >

1 This is a message that Yahweh our God gave to me, Obadiah, about the Edom [people-group]. Yahweh our God has told me this about [the people of] Edom: “I, Yahweh, have sent a messenger to other nations, telling them to prepare to go and attack Edom.”
Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2 And Yahweh says this to the people of Edom: “I will soon cause you to become the weakest and most despised nation [on the earth].
“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
3 Your [capital city] is high in the rocky cliffs, and you are very proud; you think that you are safe from being attacked by your enemies [RHQ], but you [IDM] have deceived yourselves.
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
4 And I tell you that even if [you had wings and] could fly higher than eagles fly, and if you could make your homes among the stars, I would bring you [crashing] down from there.
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
5 When thieves break into someone’s house during the night, they certainly [RHQ] steal only the things that they want. And people who pick grapes always [RHQ] leave a few grapes on the vines. But your country will be completely destroyed!
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6 Everything that is valuable will be taken away. [Your enemies] will find and take away even the valuable things that you have hidden.
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
7 All (your allies/nations who promised to help you) will turn against you, and they will force you to leave your country/land. Those with whom you have peace now will trick/deceive you and defeat you. Those who eat meals with you now are planning to trap you, and [then they will say to you], ‘You are not [RHQ] as clever [as you thought you were]!’
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8 I, Yahweh, declare that at the time that I destroy Edom, I will punish the men who live in those cliffs who [thought that they] were wise.
Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9 The soldiers from Teman [town] will become terrified; all you people who are descendants of Esau will be (wiped out/killed).
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
10 You acted cruel in a cruel way toward your relatives who are descendants of Jacob, [the twin brother of your ancestor Esau]. So now you will be disgraced forever; you will be completely destroyed.
Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Foreigners entered the gates of Jerusalem and (cast lots/threw small stones that were marked) to decide what valuable things they would take away; but you were as bad as those foreigners, because you just stood there [and did not help the Israelis].
Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 You should not have (gloated/been happy) about the disaster that the Israelis were experiencing. You should not have been happy when their towns were ruined. You should not have made fun [of them] when they were suffering.
Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
13 They are my people, so you should not have entered their [city] gates when they were experiencing those disasters and you should not have laughed at them. And you should not have taken away their [valuable] possessions.
Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
14 You should not have stood at crossroads to catch those who were [trying to] escape. You should not have [captured them and] put them into the hands of [their enemies] when they were experiencing those disasters.”
Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
15 “There will soon be the time when I, Yahweh, will judge [and punish] all the nations. And you [people of Edom] will experience the same [disasters] that you caused [others to experience]. The same evil things that you have done to others will happen to you.
“Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 [My people in Jerusalem have been punished] because I was very angry with them. [It is as though] [MET] they drank [a cup of very bitter liquid] on Zion, my sacred hill. But [I] will punish [MET] all the other nations even more severely, and cause them to disappear completely.
Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 But some [people in Jerusalem will escape], and Jerusalem will become a very holy/sacred place. Then the descendants of Jacob will [conquer and] possess again the land that truly belongs to them.
Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
18 The descendants [MTY] of Jacob and his son Joseph will be like [MET] a fire, and the people [MTY] of Edom will be like [MET] stubble that will be completely burned in that fire. Not one person will remain alive. [That will surely happen because] I, Yahweh, have said it.”
Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
19 The Israeli people [who live] in the southern desert are the ones who will capture Edom. And those [who live in] the western foothills will capture the Phoenicia [region] and the areas of Ephraim and Samaria. And people of the tribe of Benjamin will conquer the Gilead [region].
Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Those who were (exiled in/forced to go to) [Babylon] will [return to their land] [and] capture the Phoenicia [region] as far north as Zarephath [on the coast of the Mediterranean Sea]. People of Jerusalem who were captured and taken to Sardis, [the capital city of the Lydia region], will capture the towns in the southern desert.
Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 The army of Jerusalem will attack Edom and conquer it, and Yahweh will be their king.
Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

< Obadiah 1 >