< Numbers 6 >

1 Yahweh also said this to Moses/me:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Tell this to the Israeli people: ‘If any of you [wants to] make a solemn promise to dedicate himself to belong to me in a special way, [after you obey these instructions], you will be called a Nazir-man, [which means “dedicated man”].
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
3 You must not drink any wine or other alcoholic/fermented drink. You must not drink any vinegar made from wine or from any other alcoholic/fermented drink. You must not drink grape juice or eat grapes or raisins.
sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
4 You must not eat anything that comes from grapevines, not even the skins or seeds of grapes, during the time that you are a Nazir-man.
Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
5 ‘Even your hair will be dedicated to me during the time that you area Nazir-man, so you must never allow anyone to cut your hair. Until the time that your solemn promise to dedicate yourself to me is ended, you must allow your hair to grow long.
“‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
6 And you must not go near a corpse during the time that you are a Nazir-man.
Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
7 Even if the person who died is your father or your mother or your brother or your sister, you must not cause yourself to become unacceptable to me [by coming close to the corpse]. Your long hair [MTY] shows that you belong to me in a special way, so you must not cut your hair.
Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
8 You are required to keep doing this all the time that you are dedicated to me in this special way.
Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
9 ‘If anyone dies very suddenly when he is near you, then your hair that you have dedicated to me is no longer sacred. So you must wait seven days and then shave it all off. Then you must perform a special ritual to cause yourself to become acceptable to me again.
“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
10 The next day you must bring two doves or two young pigeons to the priest at the entrance of the Sacred Tent.
Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
11 ‘The priest must [kill the birds and] offer them as sacrifices. One of them will be an offering to enable me to forgive you for the sins you have committed, and the other will be an offering that is burned completely to please me. [After the priest burns them on the altar], I will forgive you for having come close to a corpse, and [when] your hair [grows again it] will be dedicated to me again.
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
12 The amount of time that you were set apart for me the previous time does not count, because you had become unacceptable to me [by coming close to a corpse] during the time that you were a Nazir-man. So you must again make a solemn promise to dedicate yourself to me for the entire amount of time that you indicated the previous time. And you must also sacrifice a one-year-old lamb for not doing what you were required to do.
Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
13 ‘When the time that you promised to dedicate yourself to me is ended, go to the entrance of the Sacred Tent
“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
14 and offer as sacrifices to me three animals that have no defects: Offer a one-year-old ram that will be burned completely, a one-year-old female lamb as a sacrifice to enable me to forgive your sins, and one full-grown ram as a sacrifice to maintain fellowship with me.
Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
15 ‘When you bring those animals, you must also bring some wine to offer as a sacrifice. And you must also bring a basket of bread that you have made with very good flour and [olive] oil. But you must not put any yeast in the bread. Also brush/spread some [olive] oil on some thin wafers and bring them to the priest.
ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
16 ‘The priest will put the young lamb and the young ram on the altar and completely burn them, in order that I will be pleased and will forgive you for your sins.
“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
17 Then he will kill the full-grown ram as an offering to restore fellowship with me, and he will also burn on the altar some of the bread and the grain and wine.
Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
18 ‘After that, you must [stand at] the entrance of the Sacred Tent and shave off your hair. Then you must put that hair in the fire that is under the [animal that has been sacrificed] on the altar to maintain fellowship with me.
“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
19 ‘The meat from the ram’s shoulder must be boiled. After it is cooked, the priest will take it along with one of the loaves of bread and one wafer which has been brushed with [olive] oil, and he will put them in your hands.
“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
20 Then the priest will [take them back and] lift them up high to dedicate them to me. They now belong to the priest, and he is permitted to eat some of the meat from the ram’s shoulder and from its ribs and from one of its thighs, because that meat is his share of the sacrifice. After that, you will no longer be a Nazir-man, and you will again be permitted to drink wine.
Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
21 ‘Those are the regulations about the offerings that Nazir-men solemnly promise to bring to me to end their time of being dedicated to me. They must bring these offerings, but if they want to, they may bring additional offerings. And they must do everything that they solemnly promised to do when they dedicated themselves to me.’”
“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
22 Yahweh also said to Moses/me,
Yehova anawuza Mose kuti,
23 “Tell Aaron and his sons that when they [ask me to] bless the people, they must say,
“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
24 ‘I desire that Yahweh will bless you and protect you,
“‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
25 and that he will smile at you and act kindly toward you,
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
26 and that he will be good to you [IDM] and cause things to go well for you.’”
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
27 Then Yahweh said, “If Aaron and his sons ask me to bless the Israeli people, truly I will bless them.”
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

< Numbers 6 >