< Luke 11 >

1 One day Jesus was somewhere praying. When he finished [praying], one of his disciples said to him, “Lord, teach us [what to say when] we [(exc)] pray, as John [the Baptizer] taught his disciples!”
Tsiku lina Yesu amapemphera pamalo ena. Atamaliza, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Ambuye tiphunzitseni kupemphera, monga momwe Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”
2 He said to them, “When you pray, say [things like this]: ‘Father, we want you [(sg)] [MTY] to be honored/revered. [We want people to let you(sg)] [MTY, MET] rule over their lives.
Yesu anawawuza kuti, “Pamene mukupemphera muzinena kuti: “‘Atate, dzina lanu lilemekezedwe, ufumu wanu ubwere.
3 Give us [(exc)] each day the food [SYN] that we need.
Mutipatse chakudya chathu chalero,
4 Forgive us [for] the wrong things that we have done, because we forgive people for the wrong things that they do to us. Do not let us do wrong things when we are tempted {[someone or something] tempts us}.’”
mutikhululukire machimo athu, monga ifenso timakhululukira aliyense amene watilakwira. Ndipo musalole kuti tigwe mʼmayesero.’”
5 Then he said to them, “Suppose that one of you goes to the house of a friend at midnight. Suppose that you [(sg) stand outside and] call out to him, ‘My friend, please lend me three buns!
Kenaka anawawuza kuti, “Tiyerekeze: Mmodzi mwa inu atakhala ndi bwenzi lake, ndipo iye nʼkupita ku nyumba yake pakati pa usiku, nakanena kuti, ‘Mnzanga, bwereke malofu atatu abuledi,
6 Another friend of mine who is traveling has just arrived [at my house], but I have no food [ready] to give to him!’
chifukwa ndalandira bwenzi langa amene ali pa ulendo ndipo ine ndilibe choti ndimupatse.’
7 Suppose that he answers you from inside [his house], ‘Do not bother me! The door has been locked {[We(exc)] have locked the door} and all my family are in bed. [So] I cannot get up and give you [(sg)] anything!’
“Ndipo yerekezani kuti amene ali mʼnyumbamo ndi kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine, ndatseka kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona. Ine sindingadzukenso kuti ndidzakupatse.’
8 I will tell you that even if he does not [want to] get up and give you [any food], to avoid being ashamed [for not helping you] because you are his friend (OR, if without being ashamed you continue asking him to do that), he certainly will get up and give you whatever you need.
Ine ndikukuwuzani kuti adzadzuka ndi kumupatsa bulediyo, osati chifukwa ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha liwuma la munthu wopemphayo, ndipo kudzamupatsa zonse zimene akuzifuna.
9 So I tell you this: Keep asking [God for what you need]. If you do that, [he] will give it to you [(pl)]. Confidently keep expecting [God to give you the things that you need], and [he] will give them to you [MET]. [It will be like] looking for what you need and finding it. Keep on [praying urgently to God. Then God will answer you. It will be like] knocking [on a door] so that [God] will open [the way] for you [to get what you pray for].
“Choncho Ine ndikunena kwa inu kuti: Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza. Gogodani ndipo adzakutsekulirani.
10 Remember that [God] will give things to everyone who continues to ask [him for them]. [He] will give things to whoever confidently keeps asking. [He] will open [the way] for people [to get the things that they keep urgently praying for].
Pakuti aliyense amene amapempha amalandira. Munthu amene amafunafuna amapeza. Iye amene amagogoda amamutsekulira.
11 If one of you had a son who asked you [(sg)] for a fish [to eat], (you [(sg)] certainly would not give him a [poisonous] snake instead!/would you give him a [poisonous] snake instead?) [RHQ]
“Ndani mwa inu abambo, kodi mwana wanu atapempha nsomba, mʼmalo mwake mungamupatse njoka?
12 If he asked you for an egg, (you [(sg)] certainly would not give him a scorpion!/would you give him a scorpion?) [RHQ]
Kapena atapempha dzira, kodi mungamupatse chinkhanira?
13 Even though you people are evil, you know how to give good things to your children. So your Father in heaven will certainly [give good things] to those who ask him, [including] giving the Holy Spirit, [who is the best gift].”
Tsono ngati inu, anthu oyipa, mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, koposa kotani Atate anu akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene awapempha!”
14 [One day there was a man there who, because a demon controlled him] [MTY], was unable to speak. After [Jesus expelled] the demon, the man [began to] talk. [Most of] the people [there] were amazed.
Yesu amatulutsa chiwanda chimene chinali chosayankhula. Chiwandacho chitatuluka, munthu wosayankhulayo anayankhula, ndipo gulu la anthu linadabwa.
15 But some of them said, “It is Beelzebub, the ruler of the demons, who enables [this man] to expel demons!”
Koma ena mwa iwo anati, “Iye akutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mfumu ya ziwanda.”
16 Other [people there] asked Jesus to perform a miracle [to prove (he was the Messiah/that he had come] from God) [MTY/EUP]. They wanted to trap him [into not being able to perform a miracle or into doing something ridiculous].
Ena anamuyesa pomufunsa chizindikiro chochokera kumwamba.
17 But Jesus knew what they were thinking. So he said to them, “If [the people in] one nation fight against each other, their nation will be destroyed {[they] will destroy their nation}. If [the people in] [MTY] one house are divided, they will cease to remain as one [family].
Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse wogawikana udzawonongeka, ndipo nyumba yogawikana idzapasuka.
18 [Similarly], if Satan [and his demons] were fighting against each other, (his rule over them would [certainly] not last!/how would his rule over them last?) [RHQ] [I say this] because you are saying that I am expelling demons by [the power of] the ruler of [his own demons]
Ngati Satana adziwukira yekha, ufumu wake ungalimbe bwanji? Ine ndikunena izi chifukwa inu mukuti Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu.
19 Furthermore, if [it is true that] Satan enables me to expel demons, [is it also true that] your disciples [who] expel demons [do so] by [Satan’s] power [RHQ]? [No, that is not true]. So they will show that you [are not thinking logically].
Tsopano ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu, nanga ophunzira anu amazitulutsa ndi mphamvu ya ndani? Choncho, iwowo ndiye adzakhala oweruza anu.
20 But because it is by the power [MTY] of God [that I expel demons], I am showing you [that the power of] God to [MET] rule [people’s lives] has come to you.”
Koma ngati ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Mulungu, ndiye kuti ufumu wa Mulungu wafika pakati panu.
21 Then, [to show that by expelling evil spirits he was making it clear that he was much more powerful than Satan, Jesus said] [MET], “When a strong man who has many weapons guards his own house, no one can steal the things in his house.
“Munthu wamphamvu, amene ali ndi zida, akamalondera nyumba yake, katundu wake amatetezedwa.
22 But when someone else who is stronger attacks that man and subdues him, he is able to take away the weapons in which the man trusted. Then he can take from that man’s house anything he [wants to].
Koma pakabwera wina wamphamvu zoposa namugonjetsa, amalanda zida zimene munthuyo amazidalirazo ndi kugawa katundu wake.
23 [No one can be neutral]. Those who do not help me [are opposing] me, and those who do not gather [people to become] my [disciples] are causing [those people] to go away [from me].”
“Munthu amene sali mbali yanga ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ameneyo ndi womwaza.
24 [Then Jesus said this]: “[Sometimes when] an evil spirit leaves someone, it wanders around in desolate areas seeking [someone in whom it can] rest. If it does not find anyone, it says [to itself], ‘I will return to the person in whom I used to live!’
“Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’
25 So it goes back and finds that [the Spirit of God is not in control of that person’s life. The person’s life is like] a house that has been {that someone has} swept clean and everything put {put everything} in order, [but a house that is empty].
Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza.
26 Then [this evil spirit] goes and gets seven other spirits that are [even] more evil than it is. They [all] enter [that person] and [begin] living there. [So], [although] that person’s condition [was bad] before, it became much worse.”
Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”
27 When Jesus said that, a woman who was listening called out [to him], “[God is] pleased with the woman who gave birth to you [(sg)] and let you nurse [at her breasts]!”
Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”
28 But he replied, “God [is] much more pleased with those who hear his message and obey it!”
Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”
29 When the group of people around [Jesus] got larger, he said, “[Many of] you people who have been observing my ministry are evil. You want [me to perform] a miracle [to prove that I have come from God], but the only miracle that [I] will perform for you is one [like happened to] Jonah.
Pamene gulu la anthu limachuluka, Yesu anati, “Uno ndi mʼbado oyipa. Umafuna kuona chizindikiro chodabwitsa. Koma sadzachiona kupatula chizindikiro chija cha Yona.
30 [After Jonah was inside a huge fish for three days, God performed] a miracle [to restore] Jonah. [Jonah then went and testified about that] to the people in Nineveh [city. God will perform] a similar miracle [for me], the one who came from heaven. [When you people have seen that miracle, you will believe my message].
Monga Yona uja anali chizindikiro kwa anthu ku Ninive, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala chizindikiro kwa anthu a mʼbado uno.
31 [Long ago the] queen from [Sheba], [far] south [of Israel, traveled a long distance to hear Solomon speak many] wise things. But now [I, a man] who [is much] greater [and wiser] than Solomon, am here, [but you have not listened to what I have told you]. Therefore, at the time when [God] judges [all people], the queen from [Sheba] will stand there, [along] with you people, and will condemn you.
Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi anthu a mʼbado uno ndipo idzawatsutsa, chifukwa iyo inachokera kumapeto a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Solomoni.
32 The people who lived in Nineveh [city] turned from their sinful ways when Jonah preached to them. But now I, who am greater than Jonah, have come [and preached to you], [but you have not turned from your sinful ways]. Therefore, at the time when God judges [all people], the people who lived in Nineveh will stand there with you and condemn you.”
Anthu a ku Ninive adzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi mʼbado uno ndipo adzawutsutsa, pakuti anatembenuka mtima ndi ulaliki wa Yona. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Yona.
33 [Then, to show them that they did not need more miracles, but that they needed only to understand better what he had already told them, he said to them] [MET], “People who light a lamp do not then hide it, or put it under a basket. Instead, they put it on a lampstand so that those who enter [their house] can see [things from] its light. [Similarly, I have not concealed God’s truth. I have revealed it to you].
“Palibe amene amayatsa nyale ndi kuyiika pa malo poti sionekera, kapena pansi pa mtsuko. Mʼmalo mwake amayika pa choyikapo chake, kuti iwo amene akulowamo aone kuwunika.
34 Your eyes [MET] are like a lamp for your body, because they enable you to see things. If your eyes are healthy, you are able to see everything well [MET]. [Similarly, if you(sg) accept my teaching, you will be able to know all that God wants you to know]. But if your eyes are bad, you are not able to see anything. It is like being in darkness [MET]. [And similarly, if you(pl) do not accept what I teach, you will not be able to know all the things that God wants you to know].
Diso lanu ndi nyale ya thupi lanu. Pamene maso anu ali bwino, thupi lanu lonse limadzaza ndi kuwunika. Koma ngati ali oyipa, thupi lanunso ndi lodzaza ndi mdima.
35 Therefore, [you(pl) do not need to see more miracles. You need to think carefully about what I have already] told you, so that the things that you have heard from others do not cause you to remain in spiritual darkness [MET].
Onetsetsani tsono, kuti kuwunika kuli mwa inu si mdima.
36 If you [live completely according to God’s truth, you will be able to know everything that God wants you to know. It will be like] being in a room with a lamp shining brightly, enabling you to see everything clearly.”
Choncho, ngati thupi lanu lonse ndi lodzaza ndi kuwunika, ndiye kuti palibe dera lina lili mdima, lonselo lidzakhala kuwunika, monga momwe kuwunika kwa nyale kumakuwalirani.”
37 While Jesus finished saying those things, a Pharisee invited him to eat a meal with him. So Jesus went to [his house] and ate with him.
Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera.
38 The Pharisee was surprised when he saw that Jesus did not follow the Pharisees’ ritual by washing his hands before eating. [The Pharisees washed their hands in a certain way to be cleansed from anything that might have contaminated them. They were afraid that God might reject them if they] had [touched something unacceptable to God].
Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.
39 The Lord [Jesus] said to him, “You Pharisees are [concerned about things that are outside your bodies, not with what is in your] ([inner beings/hearts]) [MET]. You wash the outside of cups and dishes [before you eat because you think that doing that will make you acceptable to God], but within yourselves you are very greedy and wicked.
Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa.
40 You foolish people! [God] is concerned about things that are outside [our bodies], but (he is certainly also concerned about our inner [beings]!/isn’t he also concerned about our hearts?) [RHQ]
Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja?
41 Give [money] to those who are poor. [Give according to what you know within] your (inner [/heart]) [that you should give]. Then you [will be surprised to realize that] you will be acceptable [to God without having to perform all those rituals about washing].
Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.
42 But there will be terrible punishment for you Pharisees! You give to God a tenth of [all you produce, even] the various herbs that you grow, but you do not [remember that you must act] justly [toward others] and love God! It is good to [give a tenth of your income to God], but you ought to do these other things also!
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.
43 There will be terrible punishment for you Pharisees, because you like [to sit in] the best seats in our worship places [so that people will think highly of you], and you like people to greet you [respectfully] in the marketplaces.
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.
44 There will be terrible punishment for you, because you are like ground where there is no marker [to indicate that there is a] grave [underneath]. People walk there, but they cannot see [what is rotten down below] [MET]! [Similarly, people who see you do not realize how polluted you are within yourselves].”
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”
45 One of those who taught the [Jewish] laws replied, “Teacher, by saying this you [(sg)] are criticizing us [also]!”
Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”
46 Jesus said, “It will be terrible also for you who teach the [Jewish] laws! You require people [to obey many rules that are difficult to obey] [MET]. [That is like making them] carry heavy burdens on their backs. But you yourselves do not obey the laws [that you require others to obey]. (OR, you do not do anything to help [others to obey the laws].)
Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.
47 There will be terrible punishment for you! You decorate the tombs of the prophets whom your ancestors killed, [but you do not live according to what the prophets taught].
“Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha.
48 So you are declaring that you approve of what your ancestors did. They killed the prophets, and you [are not honoring the prophets! You just] decorate their tombs!
Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo.
49 So God, who is very wise [PRS], said, ‘I will send prophets and apostles [to you Jews]. [You] will kill some of them and cause some of them to suffer greatly.
Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’
50 [As a result, I] will consider that many of you people [who have observed my Son’s ministry] will be guilty [MTY] [of murder, as if you had] killed all the prophets that other people have killed, from the time I created the world,
Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko,
51 starting from [Adam’s son Cain] killing [his brother] Abel and continuing until they killed the prophet Zechariah [in the holy place] between the altar and the temple.’ Yes, what I am saying [is true] [MTY]. [God] will punish you people who have observed my ministry, you people whom [he] considers to be guilty [MTY] for [killing] all those prophets!
kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.
52 There will be terrible punishment for you men who teach the [Jewish] laws, because you have [not let people] know [God’s truth] [MET]! [It is as though you are] taking away a key [to a house]. You are not going into [the house] yourselves, and you are not letting other people enter it, either.”
“Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”
53 After Jesus finished saying those things, he left there. Then the men who taught the [Jewish] laws and the Pharisees began to act in a very hostile way toward him. They tried to make him say what he thought about many things.
Pamene Yesu anachokamo, Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo anayamba kumamutsutsa koopsa ndi kumupanikiza ndi mafunso,
54 They kept waiting for him to say something [wrong] for which they could accuse him.
pofuna kumukola muchina chilichonse chimene Iye angayankhule.

< Luke 11 >