< Judges 16 >

1 One day Samson went to Gaza [city in the Philistia area]. He spent some time with a prostitute.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 People soon found out that Samson was there, so the men of Gaza gathered together at the city gate and waited all night. They said to themselves, “When it dawns tomorrow morning, we will kill him [when he tries to leave the city].”
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 But Samson did not stay there all night. At midnight, he got up. He went to the city gate, he took hold of its two posts, and he lifted it up out of the ground, with its [connecting cross] bar still attached. He put it on his shoulders and carried it [many miles] uphill to Hebron.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 Later Samson fell in love with a woman named Delilah, [and started to live with her]. She lived in Sorek Valley [in the Philistia area].
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 The Philistine leaders went to her and said, “Find out from Samson what makes him so strong. And find out how we can subdue him and tie him up securely. If you do that, each of us will give you 1,100 pieces of silver.”
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 So Delilah said to Samson, “Please tell me what makes you so strong, and tell me how someone can subdue you and tie you up.”
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 Samson said, “If someone ties me with seven new bowstrings, ones that are not dry yet, I will become as weak as other men.”
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 So [after Delilah told that to the Philistine leaders], they brought seven new bowstrings to Delilah.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Then she hid the men in one of the rooms in her house. Then [while Samson was sleeping], she tied him up with the bowstrings. Then she called out, “Samson! The Philistines have come here to capture you!” But Samson snapped the bowstrings as easily as though they were strings that had been singed in a fire. So the Philistines did not find out what made Samson so strong.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 Then Delilah said to Samson, “You have deceived me and lied to me! Now tell me [the truth, ] how someone can tie you up securely.”
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 Samson replied, “If someone ties me with new ropes, ones that have never been used, I will be as weak as other men.”
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 So again, [she told the Philistine leaders, and] they [came and] hid in the room as they had done before. And again, while Samson was sleeping, she took the new ropes and tied him up with them. Then she called out, “Samson! The Philistines have come to capture you!” But Samson snapped the ropes on his arms as easily as if they were threads.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 Then Delilah said, “You have deceived me and lied to me [again]! Please tell me how someone can tie you up securely!” Samson replied, “If you weave the seven braids of my hair into the threads you are weaving on the loom, and then fasten those threads with the pin [that makes the threads tight], then I will be as weak as other men.” So again, while Samson was sleeping on her lap, Delilah held the seven braids of his hair, and wove them into the threads on the loom,
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 and she tightened them with the pin. Then she called out, “Samson! The Philistines have come to capture you!” But Samson woke up and pulled out the pin, and pulled his hair from the threads on the loom.
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Then Delilah said to him, “How can you say that you love me when you do not tell me the truth about yourself? You have deceived me three times, and you still have not told me what really makes you so strong!”
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 Day after day she nagged him like that. He thought he would die from her nagging [IDM].
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 Finally Samson told her the truth. He said, “I have been set apart for God since the day I was born. And because of that, my hair has never been cut. If my hair were shaved off, my strength would be gone, and I would be as weak as other men.”
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 Delilah realized that this time he had told her the truth. So she summoned the Philistine leaders again, saying, “Come back one more time, because Samson has really told me everything [about why he is so strong]”. So the Philistine leaders returned and brought to Delilah the money [that they promised to give her].
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 Again she lulled Samson to sleep, with his head in her lap. Then she called one of the Philistine men to come and shave off Samson’s hair. As he did that, Samson began to get weaker. And finally his strength was all gone.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 Then [after she tied him up], she called out, “Samson! The Philistines have come to capture you!” He woke up and thought, “I will do as I did before. I will shake [these ropes] off myself and be free!” But he did not realize that Yahweh had left him.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 So the Philistine men seized him and gouged out his eyes. Then they took him to Gaza. There they put him in prison and bound him with bronze chains. They made him [turn a millstone to] grind grain [every day].
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 But his hair started to grow again.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 [Several months later] the Philistine leaders celebrated a big festival. During the festival they offered sacrifices to their god Dagon. They praised him, saying, “Our god has enabled us to defeat our great enemy Samson!”
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 And when the other people saw Samson, they also praised their god Dagon, saying, “Samson ruined our crops and killed many of our people, but our god has put our enemy into our hands. Our god helped us to capture the one who has killed so many of us!”
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 By that time the people were half-drunk. They shouted, “Bring Samson out of the prison! Bring him here so that he can entertain us!” So they brought Samson from the prison and made fun of him. Then they made him stand in the center of the temple. They made him stand between the two pillars that held up the roof.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 Samson said to the servant who was leading him by his hand, “Place my hands against the two pillars. I want to rest against them.”
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 At that time the temple was full of men and women. All the Philistine leaders were also there. And there were about 3,000 people on the roof, watching Samson and making fun of him.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 Then Samson prayed, saying, “Yahweh, my Lord, think about me again! Please give me strength one more time, so that I may get revenge on the Philistines for gouging out my eyes!”
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 Then Samson put his hands on the two center pillars of the temple. He put his right hand on one pillar and his left hand on the other pillar.
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 Then he shouted [to God], “Let me die with the Philistines!”, and he pushed with all his strength. [The pillars collapsed], and the temple crashed down on the Philistine leaders and all the other Philistine people, [and they all died]. So Samson killed more people when he died than he had killed all during his life.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 Later his brothers and their relatives went down [from Zorah to Gaza] to get his body. They took it back home and buried it between Zorah and Eshtaol, at the place where Samson’s father Manoah was buried. Samson had been Israel’s leader for 20 years.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< Judges 16 >