< John 11 >

1 [One time] there was a man whose name was Lazarus who was [very] sick. He lived in Bethany [village], where his [older] sisters Mary and Martha also lived.
Tsopano munthu wina dzina lake Lazaro anadwala. Iye anali wa ku Betaniya, mudzi wa Mariya ndi mchemwali wake Marita.
2 Mary was the woman who [later] poured perfume on the feet of the Lord [Jesus], and then wiped his feet with her hair.
Mariyayo ndi yemwe uja amene anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake. Lazaro wodwalayo anali mlongo wake.
3 So the two sisters sent [someone to tell] Jesus [about Lazarus], saying, “Lord, the one you love [very much] is very sick.”
Choncho alongo ake anatumiza mawu kwa Yesu kuti, “Ambuye, uja amene Inu mumamukonda akudwala.”
4 [They hoped that Jesus would come], but when Jesus heard the message, he said, “His being sick will not end in his dying. Instead, it will result in [people realizing] how great God is, and that I, God’s son, may be honored {that people may honor me, God’s son}, because of [what I will do].”
Atamva izi, Yesu anati, “Kudwalako safa nako. Koma akudwala kuti Mulungu alemekezedwe; ndi kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe chifukwa cha matendawo.”
5 Jesus loved Martha and her [younger] sister [Mary] and Lazarus.
Yesu anakonda Marita, mchemwali wake ndi Lazaro.
6 But when Jesus heard that Lazarus was sick, he stayed [where he was] for two more days.
Koma atamva kuti Lazaro akudwala, Iye anakhalabe kumene anali masiku ena awiri.
7 But Jesus [wanted to see Lazarus]. So he said to us disciples, “Let’s go back to Judea.”
Kenaka anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tibwerere ku Yudeya.”
8 We said, “Teacher, just a short while ago the Jewish [leaders] [SYN] wanted to [kill you by] throwing stones at you. So ([we think that you should not] go back there again!/[are you sure that you want to] go back there again?) [RHQ]”
Ophunzira akewo anati, “Rabi, posachedwa pomwepa Ayuda anafuna kukugendani ndi miyala, koma Inu mukupitanso komweko?”
9 [To show us that nothing bad could happen to him until the time that God had chosen] [MET], Jesus replied, “There are [RHQ] twelve hours in the daytime, [which is enough time to do what God wants us to do]. People who walk in the daytime will not stumble [over things they cannot see], because they see things by the light from the sun.
Yesu anayankha kuti, “Kodi sipali maora khumi ndi awiri pa tsiku? Munthu amene amayenda masana sapunthwa, popeza akuona chifukwa cha kuwala kwa dziko lapansi.
10 It is when people walk in the nighttime that they stumble over things, because they have no light.”
Koma amene akuyenda usiku amapunthwa, chifukwa kuwalako alibe.”
11 After he said that, he told us, “Our friend Lazarus has gone to sleep. But I will go there so that I can wake him up.”
Iye atatha kunena izi, anapitirira kuwawuza iwo kuti, “Bwenzi lathu Lazaro wagona tulo; koma Ine ndikupita kumeneko kukamudzutsa.”
12 So we said to him, “Lord, if he is sleeping, he will get well. [So you do not need to risk your life by going there].”
Ophunzira ake anayankha kuti, “Ambuye, ngati wagona adzapeza bwino.”
13 Jesus was speaking [figuratively] about Lazarus’ death, but we thought that he was talking about really being asleep.
Yesu ankayankhula za imfa yake koma ophunzira ake ankaganiza kuti amanena za tulo chabe.
14 So then he told us plainly, “Lazarus is dead.
Ndipo kenaka anawawuza momveka kuti, “Lazaro wamwalira.
15 But for your sake I am glad that I was not there [when he died], because I want you to believe [more firmly that I] ([am the Messiah/came from God]). So now, [instead of staying here], let’s go to him.”
Ine ndikukondwera chifukwa cha inu kuti kunalibe kumeneko; koma kuti mukakhulupirire tiyeni tipiteko.”
16 Then Thomas, who was {whom they} called ‘The Twin’, said to the rest of us disciples, “Let’s all go, so that we may die with Jesus [when his enemies kill him].”
Pamenepo Tomasi, wotchedwa Didimo, anati kwa ophunzira anzake, “Tiyeni nafenso tipite, kuti tikafere naye pamodzi.”
17 When we arrived [close to Bethany], someone told Jesus that Lazarus [had died and had been buried and his body had] been in the tomb for four days.
Yesu atafika, anapeza kuti Lazaro anali atagona mʼmanda masiku anayi.
18 Bethany is less than (two miles/three kilometers) from Jerusalem.
Mudzi wa Betaniya unali pafupi ndi Yerusalemu pa mtunda wosachepera makilomita atatu,
19 Many Jews had come [from Jerusalem] to console Martha and Mary over [the death of] their [younger] brother.
ndipo Ayuda ambiri anabwera kwa Marita ndi Mariya kudzawatonthoza pa imfa ya mʼbale wawo.
20 When Martha heard [someone say] that Jesus was coming, she went [along the road] to meet him. But Mary stayed in the house.
Pamene Marita anamva kuti Yesu akubwera, anapita kukakumana naye. Koma Mariya anatsala ku nyumba.
21 When Martha [got to where Jesus was], she said to him, “Lord, if you had been here, my brother would not have died [because you would have healed him]!
Marita anati kwa Yesu, “Ambuye, mukanakhala muli kuno, mlongo wanga sakanamwalira.
22 But I know that even now God will do for you whatever you ask [concerning my brother].”
Koma ine ndikudziwa kuti ngakhale tsopano Mulungu adzakupatsani chilichonse chimene mudzamupempha.”
23 Jesus said to her, “Your brother will become alive again!”
Yesu anati kwa iye, “Mlongo wako adzauka.”
24 Martha said to him, “I know that he will become alive again when all people become alive again on the [Judgment] day.”
Marita anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti adzauka pa kuukanso pa tsiku lomaliza.”
25 Jesus said to her, “I am the one who [enables people to] become alive again and who [causes people to] live [eternally]. Those who believe in me, even if they die, will live [again].
Yesu anati kwa iye, “Ine ndine kuuka ndi moyo. Wokhulupirira Ine, angakhale amwalira adzakhala ndi moyo.
26 Furthermore, all those who believe in me while they are alive, [their souls] will not die [forever]. Do you believe that?” (aiōn g165)
Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?” (aiōn g165)
27 She said to him, “Yes, Lord! I believe that you are the Messiah, (the Son of God/the man who is also God). You are the one [God promised to send] into the world!”
Marita anamuwuza Iye kuti, “Inde Ambuye, ine ndikukhulupirira kuti ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu, amene abwera mʼdziko lapansi.”
28 After she said that, she returned [to the house] and took her [younger] sister, Mary, aside and said to her, “The Teacher is close [to our village], and he wants to talk to you.”
Ndipo iye atanena izi anabwerera ndi kukayitana mchemwali wake Mariya namuyankhula monongʼona pambali, nati, “Aphunzitsi abwera ndipo akukuyitana.”
29 When Mary heard that, she got up quickly and went to him.
Mariya atamva izi, anayimirira mofulumira napita kwa Iye.
30 Jesus had not yet entered the village; he was still at the place where Martha met him.
Tsopano nʼkuti Yesu asanalowe mʼmudzi, koma anali akanali pa malo pamene Marita anakumana naye.
31 The Jews who were in the house with Mary, consoling her, saw Mary get up quickly and go outside. So they followed her, thinking that she was going to the tomb [where they had buried Lazarus], in order to cry there.
Ayuda amene ankamutonthoza Mariya mʼnyumba, anaona mmene iye anayimira mofulumira ndi kutuluka kunja, iwo anamutsata akuganizira kuti ankapita ku manda kukalirira kumeneko.
32 When Mary got to where Jesus was and saw him, she prostrated herself at his feet and said, “Lord, if you had been here, my [younger] brother would not have died!”
Mariya anafika pamalo pamene panali Yesu ndipo atamuona, anagwa pa mapazi ake ndipo anati, “Ambuye mukanakhala muli kuno mlongo wanga sakanamwalira.”
33 When Jesus saw her crying, and saw that the Jews who had come with her were also crying, he was very angry [that Satan had caused Lazarus to die] (OR, very troubled) and disturbed in his spirit.
Yesu ataona iye akulira, ndi Ayuda amene anabwera naye akuliranso, anakhudzidwa kwambiri ndi kuvutika mu mzimu.
34 He said, “Where have you buried (him/his body)?” They said to him, “Lord, come and see.”
Iye anafunsa kuti, “Kodi mwamuyika kuti?” Iwo anayankha kuti, “Ambuye tiyeni mukaone.”
35 Jesus began to cry.
Yesu analira.
36 Then [some of] the Jews said, “Look how much he loved Lazarus!”
Pamenepo Ayuda anati, “Taonani mmene Iye anamukondera Lazaro!”
37 But some others said, “He enabled a blind man to see. So (he should have been able to [heal this man so that] he did not die!/why did he not [heal this man so that] he did not die?) [RHQ]”
Koma ena a iwo anati, “Iye amatsekula maso a munthu wosaona, kodi sakanakhoza kuletsa kuti munthu uyu asamwalire?”
38 Within himself Jesus was again very angry [about Lazarus dying] (OR, very troubled). He came to the tomb. It was a cave. The entrance had been covered with a large stone.
Yesu atakhudzidwanso kwambiri anafika ku manda. Manda akewo anali phanga ndipo anatsekapo ndi mwala.
39 Jesus said, “Take away the stone!” Martha, [who, as I mentioned before, was an older] sister of the man who had died, said, “Lord, his [body] has been [in the tomb] for four days, so now there will be a bad smell!”
Yesu anati, “Chotsani mwala.” Marita mlongo wa womwalirayo anati, “Koma Ambuye, nthawi ino wayamba kununkha, pakuti wakhala mʼmenemu masiku anayi.”
40 Jesus said to her, “I told [RHQ] you that if you believed [in] ([me/what I can do]), you would see how great God is! Have [you forgotten that]?”
Kenaka Yesu anati, “Kodi Ine sindinakuwuze kuti ngati iwe ukhulupirira, udzaona ulemerero wa Mulungu?”
41 So they took away the stone. Then Jesus looked up [toward heaven] and said, “My Father, I thank you that you heard me [when I prayed about this earlier].
Choncho iwo anachotsa mwalawo. Kenaka Yesu anayangʼana kumwamba ndikuti, “Atate, Ine ndikukuthokozani chifukwa mumandimvera.
42 I know that you always hear me [when I pray]. But instead [of just praying silently], I said that for the sake of the people who are standing here. I want them to believe that you sent me.”
Ine ndimadziwa kuti Inu mumandimvera nthawi zonse, koma Ine ndanena izi chifukwa cha anthu amene ayima pano, kuti iwo akhulupirire kuti Inu munandituma Ine.”
43 After he said that, he shouted, “Lazarus, come out!”
Yesu atanena izi, Iye anayitana ndi mawu ofuwula kuti, “Lazaro, tuluka!”
44 The man who [had been] dead came out! The strips of cloth were still wrapped around his [hands and feet], and a cloth was still around his face, [but he came out]! Jesus said to them, “Take off the cloths so that he can walk easily!” [So they did that].
Munthu womwalirayo anatuluka, womangidwa miyendo ndi manja ndi nsalu za ku manda, ndi nkhope yake yokulungidwa nsalu. Yesu anawawuza kuti, “Mʼmasuleni, ndipo muloleni apite.”
45 As a result, many of the Jews who had come to [see] Mary and who had seen what Jesus did, believed that he ([was the Messiah/had come from God]).
Choncho Ayuda ambiri amene anabwera kudzamuchereza Mariya ndi kuona zimene Yesu anachita anamukhulupirira Iye.
46 But some of the [others] went to the Pharisees and told them what Jesus had done.
Koma ena a iwo anapita kwa Afarisi ndi kukawawuza zimene Yesu anachita.
47 So the chief priests and the Pharisees gathered all the members of the [Jewish] Council together. They started saying [to each other], “What are we going to do [about Jesus]? He is performing many miracles!
Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anayitanitsa msonkhano wa akulu olamulira. Iwo anafunsa kuti, “Kodi ife tikuchita chiyani? Pano pali munthu uyu akuchita zizindikiro zodabwitsa zambiri.
48 If we allow him to keep [doing this], everyone will believe (in him/that he [is the Messiah]), [and they will make him their king]. Then the Roman [army] will come and destroy our Temple and our whole nation of Israel!”
Ngati ife timuleka kuti apitirize chotere, aliyense adzamukhulupirira Iye, ndipo kenaka Aroma adzabwera ndi kudzatenga malo athu pamodzi ndi dziko lathu.”
49 One of the [Jewish Council] members was Caiaphas. He was the Jewish high priest that year. [Hinting that they should get rid of Jesus], he said to them, “You [talk as though you] do not know anything [HYP]!
Kenaka mmodzi wa iwo, dzina lake Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe chaka chimenecho, anayankhula kuti, “Inu simukudziwa kanthu kalikonse!
50 You do not realize that it would be much better for us if one man died for the sake of the people rather than that [the Romans kill] all the [people of our Jewish] nation.”
Inu simukuzindikira kuti kuli bwino kwa inu kuti munthu mmodzi afe mʼmalo mwa anthu kusiyana ndi kuti mtundu wonse uwonongeke.”
51 He said that, not because he thought of it himself. Instead, since he was the high priest that year, he was prophesying that Jesus would die for the whole [Jewish] nation.
Iye sananene izi mwa iye yekha, koma monga mkulu wa ansembe chaka chimenecho ananenera kuti Yesu anayanera kufera mtundu wa Ayuda,
52 But he was also prophesying that Jesus would die, not just for the Jews, but for all the people living in other lands who [would belong] to God, in order that he would unite [all of them into] one [group].
ndipo osati mtundu okhawo komanso kwa ana ena a Mulungu onse obalalikana, kuti awabweretse pamodzi ndi kuwapanga kukhala amodzi.
53 So from that day the [Jewish leaders] started to make plans how they could kill Jesus.
Choncho kuyambira tsiku limeneli iwo anakonzekera za kuti amuphe.
54 Because of that, Jesus no longer traveled around publicly among the Jewish people. Instead, he left [Jerusalem, along] with us disciples, and went to a village called Ephraim, in an area near the desolate region. We stayed there [for a while].
Chifukwa cha ichi Yesu sanayendenso moonekera pakati pa Ayuda. Mʼmalo mwake Iye anapita ku chigawo cha kufupi ndi chipululu, ku mudzi wa Efereimu, kumene Iye anakhalako ndi ophunzira ake.
55 When it was almost time for the Jewish Passover [celebration], many [Jews] went up to Jerusalem from other places in the country. They went there to perform the rituals to make themselves acceptable [to God] before the Passover [celebration started].
Nthawi ya Paska wa Ayuda itayandikira, ambiri anakwera kupita ku Yerusalemu kuchokera ku madera a ku midzi chifukwa cha mwambo wa kuyeretsedwa Paska asanafike.
56 The Jewish chief priests and Pharisees issued an order that if anyone found out where Jesus was, that person should report it to them, in order that they could seize him. [So the people thought that Jesus would] probably [not dare to come to the celebration]. But they kept looking for him, and as they were standing in the Temple [courtyard] they were saying to each other, “What do you think? He will not come to the celebration, will he?”
Iwo anapitiriza kumufunafuna Yesu, ndipo pamene ankayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi ukuganiza chiyani? Kodi Iye sabwera konse kuphwando?”
Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anapereka lamulo kuti ngati wina aliyense adziwe kumene kunali Yesu, iye akawawuze kuti akamugwire.

< John 11 >