< Jeremiah 15 >

1 Then Yahweh said [this] to me: “Even if Moses and Samuel could [come back from their graves and] and stand in front of me [and plead with me for these Israeli people], I would not act mercifully [IDM] toward these people. [I would tell you], ‘Send them away from me. Cause them to leave me!’
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 And if they ask you, ‘Where shall we go?’, tell them, ‘This is what Yahweh says: The ones that I say must die, will die: The ones that I say must die in wars [MTY], will die in wars. The ones that I say must die from hunger, will die from hunger. The ones that I say must be captured [and taken to other countries], will be captured [and taken to other countries].
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 I will send four things that will get rid of them: I will send [enemy soldiers using] swords to kill them. I will send wild dogs to drag away [their corpses]. I will send vultures to eat [their corpses]. And I will send [other] wild animals to eat what remains [of their corpses].
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 Because of [the wicked things that] King Manasseh did in Jerusalem, I will cause [people in] all the kingdoms of the earth to be horrified about [what will happen in Judah to] my people.
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 You [people of], no one will [RHQ] feel sorry for you. No one will [RHQ] weep/cry for you. No one will [RHQ] ask (how you are/if you are well).
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 You people have abandoned me; you have continued to walk away [from me] [DOU]. So, I will lift up my fist to smash you; I will not act mercifully toward you any longer.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 At the gates of your cities, I will [scatter you like a farmer scatters the chaff from his grain by] (winnowing it/throwing it up to allow the wind to blow the chaff away) [MET]. You, my people, have refused to turn away from your evil behavior. [So], I will get rid of you, and I will even cause your children to be killed.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 I will cause there to be more widows [in Judah] than [there are grains of] sand on the seashore [HYP]. At noontime, [when people will not be expecting it to happen], I will cause [an enemy army] to attack you, an army that will destroy your young men and cause their mothers to weep. I will cause you to suddenly experience great suffering/pain and become very terrified.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 A woman who has seven children will become faint and (gasp for breath/be hardly able to breathe); [it will be as though] daylight will become darkness for her, [because most of] her children will be dead, and she will be disgraced and humiliated [DOU]. And her children who are still alive, I will enable your enemies to kill them. [That will surely happen because I], Yahweh, have said it.’”
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 [I said to] my mother, “I am very sad; I wish that you had not given birth to me; everyone in this land opposes me and quarrels with me. I am not a person who lends [money to people and threatens to sue/harm them if they do not pay me back when they should], and I am not a person who borrows [money from others and then refuses to pay it back], but everyone [HYP] curses me.”
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 But Yahweh replied to me, “[Jeremiah], I will take care of you. And at times when your enemies have troubles and disasters, they will [come to you and] plead for you [to help them].”
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 [Yahweh also told me to say to the people] of Judah, “Your enemies, who are [as strong as] iron or bronze, [will attack you] from the north; no one will be able to stop them.
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 I will give all the valuable possessions [of the people of Judah] to their enemies, without them paying for it. Their valuable possessions will be the payment/reward [that I will give them] because of all the sins that you have committed throughout your country.
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 I will tell your enemies to force you to become their prisoners, and to take you to other lands that you do not [even] know about, and force you to become their slaves. [That will happen] because I am extremely angry [with you]; my being angry is [like] [SIM] a fire that will burn forever.”
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 [Then I said], “Yahweh, you know [what is happening to me]. [Please] come and (help me/take care of me). Punish those who are (persecuting me/causing me to suffer). [Please] do not continue to be patient with them and do not allow me to die now. It is (for your sake/because I serve you) that I am suffering.
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Yahweh my God, you are the Commander of the armies of angels; and when you spoke to me, I was delighted with your message; it caused me to be joyful, and I eagerly accepted [MET] what you said because I belong to you. [IDM, MTY]
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 When the people were carousing together, I never joined them; I sat alone, because you [MTY] are the one who controls what I do. I was very angry [with those people because of their sins].
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 So, (why do you [allow] me to continue to suffer?/I do not understand why you allow me to continue to suffer.) [RHQ] It seems that [RHQ] my wounds cannot be healed. [Sometimes you help me, sometimes you do not help me]. It seems that you are as undependable as a brook that has water in it only during certain seasons; you are like a spring that has dried up.”
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Then Yahweh [replied], “If you begin again to [trust in] me, I will restore you, in order that you can continue to serve me. If you proclaim good/valuable messages and not worthless ones, you will continue to be the one who speaks what I tell you to say. You must cause the people to pay attention to what you say; you must not pay attention to what they say.
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 They will fight against you, but I will protect you, like [SIM] people are protected from their enemies by a bronze wall. They will not defeat you, because I will be with you, and I will protect and rescue [DOU] you.
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 [Truly], I will keep you safe from those wicked people, I will rescue you when you are seized by cruel people. [That will happen because I], Yahweh, have said it.”
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Jeremiah 15 >