< Isaiah 66 >

1 Yahweh [also] said this: “[All of] heaven is [like] my throne, and the whole earth is [like] my footstool. So you could certainly not [RHQ] build a house [that would be adequate] for me to live in and rest!
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 I [MTY] have created everything; all things exist because I made them. [That is true because I], Yahweh, have said it. The people I am [most] pleased with are those who are humble, who [patiently endure it when they] (suffer/are afflicted), and who tremble when they hear me [rebuking them].
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 You have enjoyed [continually] doing the things that you want to do: [Some of] you slaughter oxen [to sacrifice them to me], but you also bring human sacrifices [to your idols]! You sacrifice lambs [to me], but you kill dogs [to offer them to your gods]. You offer grain to me, but you also bring pigs’ blood [to your idols]. You burn incense [to me], but you also praise your idols. You enjoy doing those disgusting things.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 When I called [out to you], you did not answer. When I spoke, you did not pay attention. You did [many] things that I say are evil; you chose [to do] things that I did not like. So [now] I will punish you by causing you to experience the things that you are [very] afraid of.”
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 But you people who tremble when you hear what Yahweh says, listen to what he says [now]: “Some of your people hate you and reject you because you belong to me. They make fun of you, and they say, ‘Yahweh should show his glorious power! We want to see him [do something to cause] you to be truly happy.’ But [some day] those people will be [very] disgraced.”
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 [At that time], you will listen to the noise in the city. You will hear the shouting in the temple. It will be the sound of Yahweh shouting while he is punishing his enemies!
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 No one [RHQ] ever heard that a woman gave birth to a baby when she was just starting to have birth pains.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Certainly no one [RHQ] ever heard about such a thing happening, and no one has ever seen it happen. [Similarly], no one ever [RHQ] heard that a nation was created in one instant, not even in one day. But Jerusalem is like [MET] [a woman who] gives birth to children as soon as she starts to have birth pains.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Women certainly do not [RHQ] bring infants to the time when they are ready to be born and then do not allow them to be born. [Similarly, he will do for Jerusalem] [MET] [what he has promised to do]: [He will cause Jerusalem to be full of people again]. [That will happen because] Yahweh has said it.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 You people in [APO] Jerusalem, rejoice! And all you people who love Jerusalem should also be happy. You people who were sad because of [what happened to Jerusalem], you should now be glad.
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 [You people in Jerusalem] will [have everything that you need] like [MET] a baby that gets all it needs from its mother’s breasts. You will enjoy all the abundant and glorious things [MET] in the city.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Yahweh has promised, “I will cause Jerusalem to be full of valuable things that come from other nations; those things will pour into Jerusalem; it will be like [SIM] a big flood. I will take care of the people of Jerusalem like women care for the babies that they nurse.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 I will comfort you people in Jerusalem like [MET] mothers comfort their children.”
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 When you see [those things happen], you [SYN] will rejoice. Your [old] bones will become strong [again] like [SIM] grass [that grows quickly/well in the springtime]. [When that happens, everyone] will know that Yahweh has power [MTY] to help those who worship and obey him, but that he is angry with his enemies.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Yahweh will come down with flames of fire, and his chariots [will come down] like [SIM] a whirlwind; he will be extremely angry, and he will punish [his enemies] by burning them in a fire.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 [It is as though] [MET] Yahweh has a [big] sword, and he will judge and execute many people.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Yahweh says, “Some of you people purify/bathe yourselves and [then] go to a garden to worship your gods. You eat the meat of pigs and lizards and mice, [and other things that I have forbidden you to eat]. So I will get rid of you [for doing that].
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 I know [all] the [evil] things that you think and do. [It is now time] for me to gather together the people who live in all nations and who speak all languages, and to show them that I am very great.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 I will put a mark on them, and those whom I have spared will go to various [distant] countries: to Tarshish, Put, Lud, Meshech, Tubal, Javan, and to distant islands. I will send them to proclaim to nations that have never heard about me that I am very great and glorious.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Then they will bring back here your relatives [who have been (exiled/forced to go to other countries)], to be like [SIM] an offering to me. They will come on horses, in chariots, on mules, and on camels. They will come to [Zion, ] my sacred hill in Jerusalem. That will be like [SIM] the offerings that [my] Israeli people used to bring in the correct manner to the temple.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 [I solemnly promise that] I will appoint some of them to be priests, and others to do other work in my temple. [That will surely happen because I], Yahweh, have said it.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 I [also] promise that just like the new heaven and the new earth will last forever, you will always have descendants, and you [MTY] will always be honored.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 At every festival to celebrate the Sabbath [each week] and the new moon [each month], everyone will [come and] worship me. [That will surely happen because] I, Yahweh, have said it.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 Then they will go out [of Jerusalem] and look at the corpses of those who rebelled against me. The maggots in those corpses will never die, the fire will never stop burning them, and everyone [who sees their corpses] will detest them.”
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

< Isaiah 66 >