< Isaiah 15 >

1 [I received] this message [from Yahweh] about the Moab [people-group]: In one night [two of your important cities], Ar and Kir, will be destroyed.
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 The people of Dibon, [your capital city, ] will go to their temple to mourn/weep; they will go to [their shrines] on the hilltops to weep. They will wail because of [what happened to] Nebo and Medeba [towns in the south]; they will all shave the hair of their heads, and the men will cut off their beards [to show that they are grieving].
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 In the streets people will wear rough sackcloth, and on their [flat] rooftops and in the [city] plazas everyone will wail, with tears streaming down their faces.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 [The people of] Heshbon [city] and Elealeh [towns in the north of Moab] will cry out; people as far away as Jahaz [town in the south] will hear them wailing. Therefore the soldiers of Moab will tremble and cry out and they will be very afraid [IDM].
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 I feel very sorry for [the people of] Moab; they will flee to Zoar and Eglath-Shelishiyah [towns in the far south]. They will cry as they walk up to Luhith [town]. All along the road to Horonaim [town] people will mourn because their country has been destroyed.
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 The water in Nimrim [Valley] will have dried up. The grass there will be withered; the green plants will [all] be gone, and there will be nothing left that is green.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 The people will pick up their possessions and carry them across Willows Brook.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Throughout the country of Moab, [people] will be crying; people as far away as Eglaim [in the south] and Beer-Elim [in the north] will hear them wailing.
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 The stream near Dimon will become red from the blood [of people who have been killed], but I will cause the people of Moab to experience even more [trouble]: Lions will attack those who [are trying to] escape from Moab and will [also] attack the people who remain in that country.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< Isaiah 15 >