< Isaiah 14 >

1 [But] Yahweh will act mercifully toward the Israeli people; he will choose [the people of] Israel [to be his people again], and he will allow them to [return here and] live in their own land again. Then people from [many] other countries will come here and unite with the Israeli people.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 People of other nations will help them to return to their [own] land, and those who come from other countries will (work for/become the servants of) the Israeli people. Those who captured people of Israel will be captured by Israeli soldiers, and the people of Israel will rule over the people who [previously] oppressed them.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 Some day Yahweh will free you [Israeli people] from suffering and trouble and from being afraid, and from being cruelly treated as slaves [MTY].
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 When that happens, you will make fun of the King of Babylon by saying this: “You treated us cruelly, but that has ended! Your insolently causing others to suffer is finished!
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 You evil ruler, Yahweh will get rid of your power, and you will oppress people no longer!
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 You attacked people many times because you were very angry with them, and you subdued/conquered [other] nations by causing them to suffer endlessly.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 [But soon] everything will be quiet and peaceful on the earth. Everyone [PRS] will sing [again]!
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 [It will be as though] even the trees in the forests will joyfully sing this song, the cyprus/pine [trees] and the cedar [trees] in Lebanon will sing it: ‘You (have been overthrown/are no longer a ruler), and now no one comes to get rid of us [MET].’
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 The dead people are [PRS] are eagerly waiting for you to come to the place where they are. The spirits of the world leaders will be delighted to welcome you; those who were kings of many nations [before they died] will stand up [to welcome you]. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 They will all shout to you [together], ‘Now you are as weak as we are!’
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 You were very proud and powerful, [but all] that ended when you died, along with the sounds of harps [being played in your palace]. [Now in your grave] maggots will be under you [like a sheet] [MET], and worms will cover you [like a blanket] [MET]. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 You have [disappeared from the earth like] [MET] a star which has fallen from the sky; you [were very well-known] [like] [MET] the morning star [which is seen by everyone]; you destroyed [many] nations, but now you have been destroyed.
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 You [proudly] said to yourself, ‘I will ascend to heaven, to my throne above God’s stars. I will rule on the mountain where [the gods] gather together, far in the north.
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 I will ascend above the clouds and become like the highest/greatest god!’
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 [But you were not able to do that]; instead, you were carried down to your grave, and you went to the place where the dead people are. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 The [other dead] people there stare at you; they wonder what happened to you. [They say], ‘Is this the man who caused the earth to shake and caused the [people in many] kingdoms to tremble?
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 Is this the man who [tried to] cause the world to become a desert, who conquered its cities and did not allow the people whom he captured to return to their homes?’
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 All the kings of the earth [who have died] were greatly honored when they were buried,
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 but your [corpse will] not be buried; it will be thrown away like [SIM] a worthless branch [of a tree]. Your corpse will be under a heap of other corpses of soldiers that were killed by [their enemies’] swords, and [their corpses] were not buried; you will be with those who have gone down to the stony ground in a big pit.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Your [corpse] will not be buried because you have destroyed your nation and have caused your people to be killed. The descendants of wicked people [like you] will never be honored again.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 [People will say], ‘Slaughter this man’s children because of the sins that their ancestors committed! Do not allow them to become rulers and conquer [all the nations in] the world, and fill the world with the cities [that they rule]!’”
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 [This is what] the Commander of the armies of angels says: “I [myself] will cause Babylon to be conquered. I will get rid of Babylon and its people and their descendants.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 I will cause Babylon to be a place where owls live, a place full of swamps; I will get rid of it completely [as though] [MET] I were sweeping it with a broom. [That is what I], the Commander of the armies of angels, say.”
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 The Commander of the armies of angels has [also] solemnly promised this: “The things that I have planned will surely happen [DOU].
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 [When the army of] Assyria is in my land [of Israel], I will crush them. [It will be as though] I will trample them on my mountains. My people will no longer be the slaves [MET] of the people of Assyria; [it will be as though] [MET] I will take away the burdens that are on their shoulders.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 I have a plan for everyone on the earth, a plan to show my power [MTY] to punish all the nations.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 [I], the Commander of the armies of angels, have spoken, and no one can [RHQ] change my mind. When I raise my fist [to strike Assyria], no one [RHQ] will be able to stop me [from doing that].”
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 I received this message [from Yahweh] during the year that King Ahaz died:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 You people of Philistia, do not rejoice that the enemy army [MET] that attacked you has been defeated and that their king is dead. He was [as dangerous as] [MET] a snake, but there will be another king, who will be more [dangerous] than a cobra; he will be [like] [MET] a quick-moving poisonous snake.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Those of my people who are very poor will take care of their flocks of sheep, and the needy people will lie down safely, but I will cause you people [of Philistia] who are still alive [DOU] to die from famine.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 [So], you people of Philistia, wail at the gates of your cities! You should be extremely afraid, because [a very powerful army] will come from the north [to attack you]; [their chariots will stir up the dust like] [MET] a cloud of smoke. Each of their soldiers is ready to fight.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 If messengers [from Philistia] come to us [Israeli people], this is what we must [RHQ] tell them: “Yahweh has established Jerusalem, [not Philistia], and his people who are oppressed will be safe inside [the walls of] Jerusalem.”
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Isaiah 14 >