< Genesis 34 >

1 One day Dinah, the daughter of Jacob and Leah, went to visit some of the women in that area.
Tsopano Dina, mwana amene Leya anaberekera Yakobo, anapita kukacheza ndi akazi ena a mʼdzikolo.
2 Shechem, one of the sons of Hamor, the ruler of that area who was descended from the Hiv people-group, saw her. He wanted her. So he grabbed her and forced her to have sex [EUP] with him.
Pamene Sekemu mwana wa Hamori Mhivi, mfumu ya deralo, anamuona, anamugwirira.
3 He [SYN] was very much attracted to her, and fell in love with her, and he tried to get her to love him.
Koma Sekemu anamukondadi namwali uja, Dina, mwana wa Yakobo motero kuti anamuyankhula mawu womutonthoza.
4 So Shechem said to his father Hamor, “Please get this girl for me. I want her to become my wife!”
Choncho Sekemu anati kwa abambo ake Hamori, “Mundipezere mtsikana uyu kuti akhale mkazi wanga.”
5 Jacob very soon found out that his daughter Dinah had been disgraced/defiled. But his sons were in the fields with his livestock, so he did nothing about it until they returned home.
Yakobo anamva kuti mwana wake Dina wagwiriridwa, koma sanachitepo kanthu msanga kudikira mpaka ana ake amuna omwe anali ku busa atabwerako.
6 In the meantime, Shechem’s father Hamor went to talk with Jacob.
Kenaka Hamori, abambo a Sekemu, anapita kukakambirana ndi Yakobo.
7 While they were still talking, Jacob’s sons came in from the field. When they found out what had happened, they were shocked and very angry. They said, “Shechem has done something that is very disgraceful among us Israeli people, something that never should be done!”
Pa nthawi iyi nʼkuti ana a Yakobo atabwererako ku busa kuja. Iwo atangomva zimene zinachitika, anawawidwa mtima. Iwo anapsa mtima kwambiri kuti Sekemu nʼkuchita chonyansa choterechi mu dziko la Israeli, kumugwirira Dina, mwana wa Yakobo.
8 But Hamor said to them, “My son Shechem really likes this girl. Please allow him to marry her.
Koma Hamori anawawuza kuti, “Mwana wanga Sekemu wamukonda kwambiri mwana wanu. Chonde muloleni kuti akhale mkazi wake.
9 Let’s make an agreement: You will give your daughters to our young men to be their wives, and we will give our daughters to your young men to be their wives.
Tiyeni tichite mgwirizano wa ukwati kuti ife tidzikwatira ana anu ndi inu mudzikwatira ana athu.
10 You can live among us, and live anywhere in our land that you wish. You can buy and sell things (OR, travel around) and if you find land that you want, then you can buy it.”
Khazikikani pakati pathu. Mukhoza kupeza malo wokhala kulikonse kumene mufuna. Mukhozanso kuchita malonda momasuka ndi kupeza chuma.”
11 Then Shechem said to Dinah’s father and brothers, “If you feel good toward me and do what I am asking for, I will give you whatever you ask for.
Pamenepo Sekemu anati kwa abambo ndi alongo ake a Dina, “Inu mundikomere mtima, ndipo ndidzakupatsani chilichonse munganene.
12 Tell me what gifts you want and what bride price you want, and I will give you what you ask for. I just want you to give the girl to me to be my wife.”
Tchulani mtengo wamalowolo umene ndiyenera kupereka, ndipo ndipereka. Ndidzakupatsani chilichonse chimene mukufuna malingana inu mukandipatsa namwaliyu kuti ndimukwatire.”
13 But because Shechem had done a shameful thing to their sister Dinah, the sons of Jacob deceived Shechem and his father Hamor
Ana a Yakobo anayankha Sekemu ndi abambo ake, Hamori mwachinyengo chifukwa mlongo wawo, Dina anali atayipitsidwa.
14 by saying to them, “No, we cannot do that. We cannot give our sister to be the wife of a man who is not circumcised, because that would be a shameful thing for us to do.
Iwo anati, “Sitingachite zimenezo, kupereka mlongo wathu kwa munthu wosachita mdulidwe. Chimenecho ndi chinthu cha manyazi kwa ife.
15 We will do that only if you do one thing: You must become like us by circumcising all the males that are among you.
Tikuvomerani pokhapokha mutakhala ngati ife, mutachita mdulidwe ana anu onse aamuna.
16 Then we will give our daughters to your young men to be your wives, and we will take your daughters to be the wives of our young men. We will live among you, and we will become one people-group.
Kenaka tidzakulolani kuti mukwatire ana athu, ifenso tizikwatira ana anu. Choncho tidzakhala pakati panu ndipo tidzakhala anthu amodzi.
17 But if you will not agree to being circumcised, we will take our sister and go back to our land.”
Koma ngati simuvomereza kuchita mdulidwe titenga mlongo wathu ndi kupita.”
18 What they said pleased Hamor and his son Shechem.
Mawu amenewa anakondweretsa Hamori ndi mwana wake Sekemu.
19 Shechem was very much in love with Jacob’s daughter, so he quickly agreed to do what they suggested.
Mnyamata uja amene anali wolemekezeka kwambiri pa banja lake lonse, sanachedwe kuchita mdulidwe popeza anamukonda kwambiri mwana wa Yakobo.
20 Shechem went with Hamor to the meeting place near the city gate, and they spoke to the city leaders, saying,
Choncho Hamori ndi mwana wake Sekemu anapita ku chipata cha mzinda wawo kukayankhula ndi anthu a mu mzindawo.
21 “These men are friendly toward us. We should let them live here and travel around (OR, buy and sell things) and if they find land that they want, they can buy it. There is plenty of land for them to live here. Our young men can marry their daughters, and their young men can marry our daughters.
Iwo anati, “Anthu awa ndi a mtendere. Aloleni kuti akhale mʼdziko mwathu muno nachitamo malonda. Dzikoli lili ndi malo ambiri woti iwo nʼkukhalamo. Tingathe kukwatira ana awo aakazi ndipo angathe kukwatira ana athu aakazi.
22 But these men will agree to live among us and become one people-group with us only if all our males are circumcised, as they are.
Komatu anthuwa adzavomereza kukhala amodzi a ife pokhapokha ngati amuna onse pakati pathu atachita mdulidwe monga alili iwo.
23 But if we do that, just think! Their livestock and their possessions and their other animals will become ours [RHQ]! So we should agree to do what they suggest, and then they will live among us!”
Tikatero, ndiye kuti ziweto zawo zonsezi, katundu wawo yenseyu ndi ziweto zawo zina zonsezi zidzakhala zathu. Choncho tiyeni tiwavomereze ndipo adzakhazikika pakati pathu.”
24 Shechem was the most respected person in his father’s household, so all the men who were there at the city gate agreed to what Hamor and Shechem suggested. So every male in the city was circumcised.
Amuna onse amene anatuluka ku chipata cha mzinda anavomerezana ndi Hamori ndi mwana wake Sekemu, ndipo aliyense wamwamuna mu mzindamo anachita mdulidwe.
25 On the third day after that, when the men of the city were still sore because of being circumcised, two of Jacob’s sons, Simeon and Levi, who were Dinah’s brothers, took their swords and entered the city without anyone opposing them, and killed all the men.
Patapita masiku atatu, amuna onse akumvabe ululu wa kuchita mdulidwe uja, ana awiri a Yakobo, Simeoni ndi Levi, alongo ake a Dina, anatenga malupanga ndi kulowa mu mzindawo mwakachetechete napha amuna onse.
26 They even killed Hamor and his son Shechem. Then they took Dinah out of Shechem’s house and left the city.
Anapha Hamori ndi Sekemu. Anakatenga Dina ku nyumba kwa Sekemu nanyamuka.
27 Then the other sons of Jacob went into the city where all those dead bodies were. They (looted/took everything in) the city to get revenge for the shameful thing that had been done to their sister.
Ana a Yakobo anafika kwa anthu ophedwawo ndi kututa katundu mu mzindawo chifukwa anagwiririra mlongo wawo.
28 They took away the people’s sheep and goats, their cattle, their donkeys, and everything else that they wanted from inside the city and from out in the countryside.
Analanda nkhosa zawo, ngʼombe zawo, abulu awo ndi china chilichonse chawo mu mzindamo pamodzi ndi za ku minda.
29 They took away everything that was valuable, even the children and the women. They seized and took away everything that was in the houses.
Anawatengera chuma chawo chonse, akazi ndi ana awo, pamodzi ndi zonse zimene zinapezeka mʼnyumba zawo. Zonsezi zinayesedwa ngati zolandidwa ku nkhondo.
30 Then Jacob said to Simeon and Levi, “You have caused a lot of trouble for me! Now the Canaan people-group and the Perizzi people-group and everyone else who lives in this land will (hate me/say my name stinks)! I do not have many men to fight for us, so if they all gather together and come to me and attack us, they will destroy us and all our household!”
Pamenepo Yakobo anati kwa Simeoni ndi Levi, “Mwandiputira mavuto, ndi kundiyipitsira dzina pakati pa anthu a mʼdziko lino, Akanaani ndi Aperezi. Ife ndife owerengeka, ndipo atati aphatikizane kudzandithira nkhondo, ndiye kuti ine ndi banja langa tidzawonongeka.”
31 But they replied, “(Should we have allowed Shechem to treat our sister like a prostitute?/We could not just let Shechem treat our sister like a prostitute!)” [RHQ]
Koma iwo anayankha kuti, “Pepani, nanga achite kumusandutsa mlongo wathu ngati mkazi wachiwerewere?”

< Genesis 34 >