< Genesis 19 >

1 That evening, the two angels arrived in Sodom. Lot was sitting at the gateway of the city. When he saw them, he got up to greet them, and prostrated himself with his face on the ground.
Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu.
2 He said to them, “Gentlemen, please stay in my house tonight. You can wash your feet, and tomorrow you can continue your journey.” But they said, “No, we will just sleep in the city square.”
Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.” Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”
3 But Lot kept insisting strongly that they sleep in his house. So they entered his house with him, and he prepared a meal for them. He baked some bread without yeast, and they ate it.
Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya.
4 After they finished eating, before they went to bed, the men of Sodom [city], all of them, from the young ones to the old ones, surrounded the house.
Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti.
5 They called out to Lot, saying, “Where are the men who came to your house this evening? Bring them out, so that we can have sex with them!” [EUP]
Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”
6 Lot went outside the house and shut the door behind him, so that they could not go inside.
Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko
7 He said to them, “My friends, don’t do such an evil thing!
ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere.
8 Listen to me. I have two daughters who have never had sex with any man. Let me bring them out to you now, and you can do with them whatever pleases you. But don’t do anything to these men, because they are guests in my house, [so I must protect them]!”
Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”
9 But they replied, “Get out of our way! You are a foreigner; so you have no right to tell us what is right! [If you don’t get out of our way], we will do worse things to you than we will do to them!” Then they lunged towards Lot, and tried forcefully to break down the door.
Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.
10 But the two angels opened the door carefully, reached out their hands, and pulled Lot to them inside the house. Then they quickly shut the door.
Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko.
11 Then they caused all the men who were outside the door of the house, young and old, to become blind, so that they could not find the door.
Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.
12 Then the two angels said to Lot, “Who else is with you here? If you have sons or sons-in-law or daughters or anyone else in the city who is related to you, take them out of the city,
Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno,
13 because we are the ones who are going to destroy this place. Yahweh considers that these people are so evil that he sent us to destroy the city.”
chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”
14 So Lot went and spoke to the men who had pledged to marry his daughters. He said to them, “Hurry! Get out of this city, because Yahweh is about to destroy it!” But his future sons-in-law thought he was joking.
Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.
15 As it was about to dawn the next morning, the two angels urged Lot, saying, “Get up quickly! Take your wife and your two daughters who are here with you and leave! If you don’t, you will die when [we destroy/Yahweh destroys] the city!”
Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”
16 When Lot hesitated, the angels grasped his hand and his wife’s hand and the hands of his two daughters. They led them outside the city safely. The angels did that because Yahweh was acting mercifully toward them.
Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo.
17 When they were outside the city, one of the angels said, “[If you want to remain alive], run away quickly! Don’t look back! And don’t stop anywhere in the valley! Flee to the hills! If you don’t, you will die!”
Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”
18 But Lot said to one of the angels, “No, sir, don’t make me do that!
Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero!
19 Please, listen. You have been pleased with me and have been very kind to me and spared my life. But I cannot flee to the mountain. If I try to do that, I will die in this disaster [PRS].
Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe.
20 But listen to me. There is a town nearby. Let me run to that small town. Let me go there now. It is a small town, but our lives will be saved if we go there.”
Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”
21 One of the angels said to Lot, “I will allow you to do what you have requested [MTY]. I will not destroy the little town you are speaking about.
Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo.
22 But hurry! Run there, because I cannot destroy anything until you arrive there.” People later called the name of the town Zoar [which means ‘small’, ] because Lot said it was small.
Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).
23 As the sun was rising, Lot and his family arrived in the town which is now called Zoar.
Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka.
24 Then Yahweh caused fire and [burning] sulfur to fall down on Sodom and Gomorrah like rain.
Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora.
25 In that way, he destroyed those cities and all the people who were living in those cities. He also destroyed everything in the valley, including all the plants/vegetation.
Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo.
26 But Lot’s wife stopped and looked back [to see what was happening], so she died, and her body [later] became a pillar of salt.
Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.
27 That morning, Abraham got up and went to the place where he had stood in front of Yahweh.
Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja.
28 He looked down toward Sodom and Gomorrah, and he [was surprised to] see that all over the valley, smoke was rising, like the smoke of a huge furnace.
Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.
29 So, when God destroyed those cities in the valley, he remembered what he had promised Abraham, and he rescued Lot from the disaster that occurred in the cities where Lot had lived.
Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.
30 Lot was afraid to stay in Zoar, so he left there and moved with his two daughters to the mountain, and they lived in a cave.
Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga.
31 One day the older daughter said to (the younger daughter/her sister), “Our father is old, and there is no man in this area who can have sex [EUP] with us, as people all over the earth do.
Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi.
32 Let’s make our father drink wine until he gets drunk. Then we can have sex with him [EUP] [without him knowing it]. In that way [he will cause us to become pregnant] and we can bear children.”
Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”
33 So that night they caused their father to become drunk. And the older daughter went in and lay in bed with her father, and he had sex with her, but he was so drunk that he did not know when she lay down with him or when she got up.
Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
34 The next day, his older daughter said to (his younger daughter/her sister), “Listen to me. Last night I slept with our father. Let’s cause him to become drunk again tonight! This time you can go and sleep with him. If he has sex with you, you can become pregnant, and that way you can have a child, too.”
Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.”
35 So that night, they caused their father to become drunk with wine again, and then his younger daughter went and slept with him. But again, he was so drunk that he did not know when she lay down with him or when she got up.
Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
36 So Lot caused his two daughters to become pregnant.
Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo.
37 The older one later gave birth to a son, whom she named Moab. He became the ancestor of the Moab people-group.
Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse.
38 The younger one also gave birth to a son, whom she named Ben-Ammi. He became the ancestor of the Ammon people-group.
Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.

< Genesis 19 >