< Galatians 1 >

1 [I], Paul, [write this letter to you. I remind you that I am] an apostle. That is not because a group of people [appointed me], nor because a human being [sent me to be an apostle]. Instead, Jesus Christ and God [our heavenly] Father, who caused Jesus to become alive again after he died, have [appointed and] sent [me to be an apostle].
Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
2 All the fellow believers [who are here] with me [approve of this message that I am writing. I am sending this letter] to the congregations that [are] in Galatia [province].
pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 [I pray that] God, our Father, and the Lord Jesus Christ will kindly [help] you and enable [you to have inner] peace.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
4 Christ offered himself [as a sacrifice] in order that [he might remove the guilt for] our sins. He did that in order that he might enable us to not [do the evil things that people who do not know him] do. [He did this] because God, who is our Father, wanted it. (aiōn g165)
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
5 [I pray that people will] praise God forever. (May it be so!/Amen!) (aiōn g165)
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
6 I am very disappointed [IRO] that so soon [after you trusted in Christ] you have turned away from [God]. He chose you in order that [you might have what] Christ freely/kindly gives. I am also disappointed that so soon you are believing a different [message which some say is] “good news.”
Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
7 Their message is not a true message. [What is happening is that] certain persons are confusing your [minds]. They are desiring to change the good message (that Christ [revealed/about] Christ) [and are creating another message].
umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
8 But even if we [(exc) apostles] or an angel from heaven would tell you a message that is different from the good message that we told you [before], I [appeal to God] that [he] punish such a person [forever].
Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
9 As I told you previously, so now I tell you this once more: Someone is telling you [what he says is] a good message, but it is a message that is different from [the good message] that I gave you. So I [appeal to God] that [he] severely punish that person.
Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
10 [I said that] because [RHQ] I do not desire that people approve me, [contrary to what some have said about me]. It is God whom I desire to approve me. [Specifically, I do not say and do] [RHQ] things just to please people. If it were still people whom I was trying to please, then I would not be one who [willingly and completely] serves Christ.
Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
11 My fellow believers, I want you to know that the message about Christ that I proclaim to people is not one that some person [created/thought up].
Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
12 I did not receive this message from a human [messenger], and no [human being] taught it to me. Instead, Jesus Christ revealed it to me.
Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
13 People have told you how I used to behave when [I practiced] the Jewish religion. They told you that I continually did very harmful things to the groups of believers that God [established], and they told you that I tried to get rid of those people.
Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
14 I practiced the Jewish religion more thoroughly than many [other Jews] who were my age practiced it. I much more enthusiastically tried to get others to obey the traditions that my ancestors [kept].
Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
15 Nevertheless, before I was born, [God] (set me apart/selected me). He chose me [to live eternally], something that I did not deserve.
Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
16 He wanted me to know that Jesus is (his Son/the man who is also God), so that I would tell others the message about him in regions where non-Jews live. But I did not immediately go to any human beings [SYN] in order to gain [an understanding of that message. I received it directly from Christ!]!
kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 I did not [immediately] leave Damascus and go to Jerusalem [for that purpose] to those who were apostles before I was. Instead, I went away to Arabia [region, a desert area]. Later I returned once more to Damascus [city].
Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
18 Then three years after [God revealed this good message to me], I went up to Jerusalem in order that I might meet Peter. But I stayed with him for [only] 15 days, [which was not long enough for him to teach me thoroughly about Christ].
Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
19 I also saw James, the brother of our Lord [Jesus and the leader of the believers there, but] I did not see any other apostle.
Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
20 God knows that what I am writing to you is completely true [LIT]!
Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
21 After [I left Jerusalem], I went to [the regions of] Syria and Cilicia.
Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
22 [At that time, people in] the Christian congregations that are in Judea [province] still had not met me [SYN] personally.
Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
23 They only heard [others say about me] repeatedly, “[Paul], the one who was formerly doing harmful things to us, is now telling the [same message] which we believe and which formerly he was trying (to destroy/to cause people to stop believing)!”
Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
24 And they praised God because of [what had happened to] me.
Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

< Galatians 1 >