< Ezekiel 19 >

1 [Yahweh said to me, “Ezekiel], sing a sad funeral [a which will be a parable] [two of the] kings of Israel.
“Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
2 Say [to the Israeli people], ‘[It is as though] [MET] your mother was a brave female lion who raised her cubs among [other] lions.
Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
3 She taught one of them to [for other animals to kill], and he [even] learned [kill and] eat people.
Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
4 [When people from other] nations heard about him, they trapped him in a pit. Then they used hooks to drag him to Egypt.
Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
5 His mother waited for him [to return], but [soon] she stopped hoping/expecting [that he would return]. So she raised another cub who [also] became very fierce.
“‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
6 He hunted along with [other] [for animals to kill], and he even learned [kill and] eat people.
Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
7 He destroyed forts, and he ruined cities. When he roared [loudly], everyone was terrified.
Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
8 So [people of other] nations planned to kill him, and men came from many places to spread out a net for him, and they caught him in a trap.
Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
9 They tied him with chains and took him to Babylonia. And [there] he was locked in a prison, with the result that [no one on] the hills of Israel ever heard him roar again.’ [Also, say to the Israeli people, ]
Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
10 ‘[It is as though] [SIM] your mother was a grapevine that was planted along a stream. There was plenty of water, so it had lots of branches and produced [a lot of] grapes.
“‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11 That grapevine grew and became taller than all the nearby trees; [everyone could] see that it was very strong and healthy. And those branches were good for making scepters that symbolize the power/ [of a king].
Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
12 [Yahweh] became very angry, so he pulled up the vine by its roots and threw it on the ground, where the [very hot] winds from the desert dried up all its fruit. The strong branches wilted and were burned in a fire.
Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13 Now that vine has been planted in a hot, dry desert.
Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14 A fire started to burn its stem, and then started to burn the branches and burned all the grapes. [Now] not [even] one strong branch remains; they will never become scepters for a king.’ That funeral song must be sung very sadly.”
Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”

< Ezekiel 19 >