< Exodus 24 >

1 Then Yahweh said to Moses/me, “Come to me, up [on top of this mountain], you and Aaron and [his sons] Nadab and Abihu. Also [take along] 70 of the Israeli elders/leaders. While you are still some distance [from the top of the mountain], prostrate yourselves [on the ground] and worship me.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
2 Moses, [I will allow] you alone to come near to me. The others must not come near, and the [rest of the] people must not come up the mountain.”
Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
3 Moses/I went and told the people everything that Yahweh had said and all that he had commanded. The people all replied together, saying, “We will do everything that Yahweh has told us [to do].”
Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
4 Then Moses/I wrote down everything that Yahweh had commanded. Early the next morning Moses/I built a [stone] altar. He/I also set up twelve stones, one for each of the Israeli tribes.
Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
5 He/I also selected some young men. They burned sacrifices to Yahweh and they also sacrificed some cattle [that they did not burn completely], for the purpose of maintaining fellowship with Yahweh.
Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
6 Moses/I took half of the blood of the animals that were slaughtered and put it in bowls. The other half of the blood [he/I] threw/splashed against the altar.
Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
7 Then he/I took the scroll on which he/I had written [everything that Yahweh had commanded in] the agreement that he had made, and he/I read it [aloud], while all the people were listening. Then all the people said, “We will do all that Yahweh has told us to do. We will obey [everything].”
Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
8 Then Moses/I took the blood [that was in the bowls] and threw/splashed it on the people. He/I said, “This is the blood [that (confirms/puts into effect)] the agreement that Yahweh made with you when he gave you all these commands.”
Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
9 Then Moses/I, along with Aaron, Nadab, Abihu, and the 70 Israeli elders/leaders, went up [the mountain],
Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
10 and they/we saw God, the one whom the Israeli people worship. Under his feet was something like a pavement [made of expensive blue stones called] sapphires. They were as clear as the sky is [when there are no clouds].
ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
11 God did not harm [MTY] those Israeli elders/leaders [because of their having seen him]. They saw God, and they ate and drank together! [Then we all went back down the mountain].
Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
12 Then Yahweh said to Moses/me, “Come up to me [again] on [top of this] mountain. While you are here, I will give you [two] stone slabs on which I have written all the laws [DOU] that I have given to you to instruct/teach [the people].”
Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
13 So Moses/I told the elders, “Stay here [with the other people] until we return! Do not forget that Aaron and Hur will be with you. So if anyone has a dispute [while I am gone], he can go to those two men.” Then Moses/I went with his/my servant Joshua [part of the way] up the mountain that [was dedicated to] God.
Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
15 Then Moses/I went the [rest of the way] up the mountain. A cloud covered the mountain.
Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
16 The (glory/brilliant light) of Yahweh came down on the mountain and covered it for six days. On the seventh day, Yahweh called to Moses/me from the middle of the cloud.
Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
17 When the Israeli people [looked at] the top of the mountain, the glory of Yahweh was like a big fire that was burning [there].
Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
18 Moses/I went into the cloud on top of the mountain. He/I was there for 40 days and nights.
Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.

< Exodus 24 >