< Deuteronomy 31 >

1 When Moses/I finished saying all that to the Israeli people,
Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
2 he/I said to them, “Now I am 120 years old. I am no longer able to go everywhere [that you go] (OR, to be your leader). Furthermore, Yahweh has told me that I will not cross the Jordan [River].
“Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
3 But Yahweh our God will go ahead of you. He will [enable you to] destroy the nations that are living there, in order that you can occupy their land. Joshua will be your leader, which is what Yahweh already told me.
Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
4 Yahweh will do to those nations what he did to Sihon and Og, the two kings of the Amor people-group when he destroyed their armies [MTY].
Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
5 Yahweh will enable you to conquer those nations, but you must [kill all of the people of those nations, which is] what I have commanded you to do.
Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
6 Be brave and confident. Do not be afraid of those people. [Do not forget that] it is Yahweh our God who will go with you. He will always help [LIT] you and never abandon you.”
Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
7 Then Moses/I summoned Joshua, and while all the Israeli people were listening, he/I said to him, “Be brave and confident. You are the one who will lead these people into the land that Yahweh promised to our ancestors that he would give to them, and you will enable them to occupy it.
Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
8 It is Yahweh who will go ahead of you. He will be with you. He will always help [LIT] you. He will never abandon you. So do not be afraid or dismayed.”
Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
9 Moses/I wrote down all these laws [on two scrolls] and gave [one scroll] to the priests, who carried the chest containing the Ten Commandments, and [gave the other scroll] to the Israeli elders.
Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
10 Moses/I told them, “At the end of every seven years, at the time that all debts are canceled, [read this to the people] during the Festival of [Living in Temporary] Shelters.
Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
11 Read it to all the Israeli people when they gather at the place that Yahweh chooses for them to worship him.
pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
12 Gather together everyone—men, women, children, even the foreigners [who are living] in your towns—in order that they may hear [these laws] and learn to revere Yahweh our God, and to faithfully obey everything that is written in these laws.
Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
13 [If they do that], your descendants who have never known these laws will hear them and will also learn to revere Yahweh our God, during all the years that they live in the land that you are about to cross the Jordan [River] to occupy.”
Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
14 Then Yahweh said to Moses/me, “Listen carefully. You will soon die. Summon Joshua, and you go to the Sacred Tent with him, in order that I may appoint him [to be the new leader].” So Joshua and Moses/I went to the Sacred Tent.
Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
15 There Yahweh appeared to them/us in a pillar of cloud, and that cloud was close to the door of the tent.
Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
16 Yahweh said to Moses/me, “You will soon die [EUP]. Then these people will become unfaithful [MET] to me. They will abandon me and (break/stop obeying) the agreement that I made with them. They will begin to worship the foreign/pagan gods [that are worshiped by the people] of the land that they will enter.
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
17 When that happens, I will become very angry with them. I will abandon them [DOU] and I will no longer help them [IDM], and I will destroy them {they will be destroyed}. Many terrible things will happen to them, with the result that they will say, ‘[We are certain that] [RHQ] these things are happening to us because our God is no longer with us.’
Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
18 And because of all the evil things that they will have done, and [especially because] they will have started to worship other gods, I will refuse to help [IDM] them.
Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
19 “So, [I am going to give you] a song. Write it [on a scroll] and teach it to the Israeli people and cause them to memorize it. It will be like a witness that accuses them.
“Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
20 I am about to take them into a very fertile [IDM] land, a land that I solemnly promised their ancestors that I would give to them. There they will have plenty to eat, with the result that their [stomachs] will [always] be full and they will become fat. But then they will turn to other gods and start to worship them, and they will despise me and (break/stop obeying) the agreement that I made with them.
Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
21 And they will experience many terrible disasters. After that happens, their descendants will never forget this song, and it will be like a witness [that says, ‘Now you know why Yahweh punished your ancestors].’ I will soon take them into the land that I vowed that I would give to them; but now, before I do that, I know what they are thinking [that they will do when they are living there].”
Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
22 So on the day that [Yahweh gave Moses/me this song], he/I wrote it down, and he/I taught it to the Israeli people.
Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
23 Then Yahweh (appointed/set apart) Joshua and said to him, “Be brave and confident, because you will lead the Israeli people into the land that I vowed that I would give to them. And I will be with you.”
Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
24 Then Moses/I finished writing on a scroll all the laws that Yahweh had told to him/me.
Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
25 Then Moses/I told the descendants of Levi, who were carrying the Sacred Chest that contained the Ten Commandments,
analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
26 “Take this scroll on which these laws [are written], and place it beside the Sacred Chest that contains the agreement that Yahweh our God made with you, in order that it may remain there to testify [about what Yahweh will do] to the people [if they disobey him].
“Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
27 [I say this] because I know that these people are very stubborn [DOU]. They have rebelled against Yahweh all during the time that I have been [with them], and they will rebel much more after I die!
Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
28 So gather all the elders of the tribes and your officials, in order that I can tell them the words [of this song], and request all those who are in heaven and on the earth to be witnesses to testify against these people.
Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
29 I say that because I know that after I die, the people will become very wicked. They will turn away from doing everything that I have commanded them to do. And in the future, because of all the evil things that they will do, they will cause Yahweh to become angry with them. And he will cause them to experience disasters.”
Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
30 Then, while all the Israeli people listened, Moses/I sang/recited this entire song to them:
Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:

< Deuteronomy 31 >