< Acts 16 >

1 Paul [and Silas] to Derbe [city and visited the believers there]. Next [they went to] Lystra [city]. A believer whose name was Timothy lived there. His mother was a Jewish believer, but his father was a Greek.
Paulo anafika ku Derbe ndi Lusitra, kumene kumakhala ophunzira wina dzina lake Timoteyo. Amayi ake anali Myuda wokhulupirira, koma abambo ake anali Mgriki.
2 The believers in Lystra and Iconium said good things about Timothy,
Abale a ku Lusitra ndi Ikoniya anamuchitira iye umboni wabwino.
3 and Paul wanted to take Timothy with him [when he went] to other places, so he circumcised Timothy. [He did that so that] the Jews who lived in those places [would accept Timothy], because they knew that his non-Jewish father [had not allowed him to be circumcised] {[anyone to circumcise his son]}.
Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki.
4 [So Timothy went with Paul and Silas] and they traveled to many other towns. [In each town] they told [the] believers the rules that had been decided by the apostles and elders in Jerusalem {that the apostles and elders in Jerusalem had decided} that [non-Jewish] believers should obey.
Pamene amayenda mzinda ndi mzinda, amafotokoza zimene atumwi ndi akulu ampingo ku Yerusalemu anagwirizana kuti anthu azitsatire.
5 [God was helping] the believers in those towns to trust more strongly [in the Lord Jesus], and every day more people became believers.
Kotero mipingo inalimbikitsidwa mʼchikhulupiriro ndipo anthu amachulukirachulukirabe tsiku ndi tsiku.
6 Paul and his companions wanted/planned to enter Asia [province] preach the message [about Jesus] there, but they were prevented by the Holy Spirit {the Holy Spirit prevented them} [from going there. So] they traveled through Phrygia and Galatia [provinces].
Paulo ndi anzake anadutsa mayiko a Frugiya ndi Galatiya, Mzimu Woyera atawaletsa kulalikira Mawu a Mulungu ku Asiya.
7 They arrived at the border of Mysia [province] and they wanted to go [north] Bithynia [province]. But [again] the Spirit of Jesus showed them that they should not [go there].
Atafika ku malire a Musiya, anayesa kulowa ku Bituniya, koma Mzimu wa Yesu sunawalole kutero.
8 So they went through Mysia [province] and arrived at Troas, a [port city. I, Luke, joined them there].
Ndipo iwo anadutsa Musiya ndipo anapita ku Trowa.
9 That night [God gave] Paul a vision in which he saw a man [who was a native] of Macedonia [province]. He was standing [some distance away], and he was earnestly calling to Paul, “[Please] come over [here] to Macedonia and help us!”
Nthawi ya usiku Paulo anaona masomphenya, munthu wa ku Makedoniya atayimirira ndi kumupempha kuti, “Bwerani ku Makedoniya, mudzatithandize.”
10 [The next morning] we [(exc)] immediately got ready to go to Macedonia, because we believed that God had called us to [go and] preach the good message to the people there.
Paulo ataona masomphenyawa, tinakonzeka kupita ku Makedoniya, kutsimikiza kuti Mulungu anatiyitana kuti tikalalikire Uthenga Wabwino.
11 So we [(exc)] got on a ship in Troas and sailed across [the sea] Samothrace [Island. We spent the night there], and the next day [we sailed again across the sea and arrived] at Neapolis [port/town].
Kuchokera ku Trowa tinakwera sitima ya pamadzi kupita ku Samotrake ndipo mmawa mwake tinapitirira mpaka ku Neapoli.
12 Then we [left Neapolis and] went [by land] to Philippi. It was a very important city in Macedonia [province, where many] Roman citizens lived. We stayed in Philippi several days.
Kuchokera kumeneko tinapita ku Filipi, boma la Aroma ndiponso mzinda waukulu wa dera la Makedoniya. Tinakhala kumeneko masiku owerengeka.
13 On the first (Sabbath/Jewish day of rest) [after we(exc) arrived], we went outside the city gate [down] to the river. We had heard [someone say] that [Jewish] people gathered to pray there. [When we arrived there, we saw] some women who had gathered [to pray]. So we sat down and began to tell them [the message about Jesus].
Pa tsiku la Sabata tinatuluka mu mzindawo kupita ku mtsinje kumene timayembekezera kukapeza malo opempherera. Tinakhala pansi ndipo tinayamba kuyankhula ndi amayi amene anasonkhana pamenepo.
14 A woman whose name was Lydia was one of those who were listening [to Paul. She was a non-Jewish woman], from Thyatira [city, who bought and] sold [expensive] purple cloth. She had accepted what the Jews believe about God. The Lord [God] caused her to pay attention to the message that Paul preached, and she believed it. [The members of her household also heard the good message and believed in Jesus] [MTY].
Mmodzi wa amayi amene amamvetserawo ndi Lidiya amene amagulitsa nsalu zofiira, wochokera ku mzinda wa Tiyatira, ndipo amapembedza Mulungu. Ambuye anatsekula mtima wake kuti amve mawu a Paulo.
15 After [Paul and Silas] baptized Lydia and the others who lived in her house [MTY] {After Lydia and the others who lived in her house were baptized}, she invited us to [go and stay in] her home. She said, “You [(pl)] know that I [now] believe in the Lord [Jesus], so [please] come and stay in my house.” She persuaded us [to do that, so we(exc) stayed there].
Iye ndi a mʼbanja lake atabatizidwa, anatiyitana kuti tipite ku nyumba yake. Iye anati, “Ngati mwanditenga ine kukhala wokhulupirira mwa Ambuye, bwerani mudzakhale mʼnyumba mwanga.” Ndipo anatiwumiriza ife kwambiri.
16 Another day, while we [(exc)] were going to the place where people regularly gathered to pray, we met a young woman who was a slave. An evil spirit was enabling her to be a ventriloquist and to tell people what would happen [to them]. People paid a lot of money to [the men who were] her owners, in return for her telling them things that [she said] would happen [to them].
Tsiku lina pamene timapita kumalo wopempherera, tinakumana ndi mtsikana wina amene anali ndi mzimu woyipa umene umanena zamʼtsogolo. Iye amapezera ndalama zambiri ambuye ake pa ulosi wake.
17 This young woman followed Paul and the rest of us. She continually shouted, “These men serve the God who is the greatest [of all gods]! They are telling you how ([God] can save you [so that he will not punish you/to be] saved)”
Mtsikanayu anatsatira Paulo ndi ife, akufuwula kuti, “Anthu awa ndi atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, amene akukuwuzani inu njira yachipulumutso.”
18 She continued to do that for many days. Finally Paul became irritated. So he turned [toward the young woman] and rebuked the evil spirit [that was in her. He said], “By the authority [MTY] of Jesus Christ, I command you [(sg)] to come out of this young woman!” Right away the evil spirit left her.
Iye anachita izi masiku ambiri. Kenaka Paulo anavutika mu mtima, natembenuka ndipo anati kwa mzimuwo, “Ndikukulamula iwe mʼdzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa iye!” Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.
19 And then her owners realized that she could no longer earn money for them [because she could no longer predict what would happen to people, so they were angry]. They grabbed Paul and Silas and forcefully took them to the public square, to [the place where] the government authorities and [a lot of other people were gathered].
Pamene ambuye a mtsikana uja anazindikira kuti chiyembekezo chawo chopezera ndalama chatha, anagwira Paulo ndi Sila nawakokera ku bwalo la akulu.
20 The owners [of the young woman] brought Paul and Silas to the city officials and told them, “These men are Jews, and they are greatly troubling [the people in] [MTY] our city.
Anawabweretsa iwo kwa oweruza milandu ndipo anati, “Anthu awa ndi Ayuda, iwo akuvutitsa mu mzinda wathu.
21 They are teaching that we [(inc)] should follow customs that our laws do not allow us Romans to consider [to be correct] or to obey!”
Ndipo akuphunzitsa miyambo imene ife Aroma sitiloledwa kuyilandira kapena kuyichita.”
22 Many of the crowd joined [those who were accusing] Paul and Silas, and started beating them. Then the [Roman] authorities commanded [soldiers] to tear the shirts off Paul and Silas and to beat them [with rods/sticks].
Gulu la anthu linatsutsana ndi Paulo ndi Sila, ndipo woweruza milandu analamula kuti avulidwe ndi kumenyedwa.
23 [So the soldiers] beat Paul and Silas vigorously [with rods]. After that, they [took them and] shoved them into the prison. They told the jailer that he should lock them up securely.
Atawakwapula kwambiri anawaponya mʼndende, nalamula woyangʼanira kuti awasunge mosamalitsa.
24 [Because the officials] had [commanded] him [to do that], the jailer shoved Paul and Silas into the cell that was farthest inside. [There, he made them sit down on the floor/ground and stretch out their legs]. Then he fastened their ankles in [grooves] between two large wooden beams, [so that Paul and Silas could not move their legs].
Chifukwa cha mawu amenewa woyangʼanira ndende anakawayika mʼchipinda chamʼkati mwa ndende, nawamangirira miyendo yawo mʼzigologolo.
25 About midnight, Paul and Silas were praying [aloud] and praising God by singing hymns. The [other] prisoners were listening attentively to them.
Koma pakati pa usiku Paulo ndi Sila ankapemphera ndi kuyimba nyimbo zolemekeza Mulungu, ndipo akayidi ena ankamvetsera.
26 Suddenly there was a very strong earthquake. It shook the entire jail [SYN] and its foundation [SYN]. [The earthquake caused] all the doors [of the jail] to open suddenly, and [caused] all the chains that fastened the prisoners to fall off.
Mwadzidzidzi kunachitika chivomerezi champhamvu kotero kuti maziko a ndende anagwedezeka. Nthawi yomweyo zitseko zonse za ndende zinatsekuka, ndipo maunyolo a aliyense anamasuka.
27 The jailer woke up and saw that the doors of the jail were open. He thought that the prisoners had escaped. So he pulled out his sword in order to kill himself, [because he knew that the officials would kill him if the prisoners escaped].
Woyangʼanira ndende uja atadzuka ku tulo, anaona kuti zitseko za ndende zinali zotsekula, ndipo anasolola lupanga lake nafuna kudzipha chifukwa ankaganiza kuti amʼndende athawa.
28 Paul [saw the jailer and] shouted to him, “Do not harm yourself! We [(exc) prisoners] are all here!”
Koma Paulo anafuwula kuti, “Usadzipweteke! Tonse tilipo!”
29 The jailer shouted [to someone] to bring torches/lanterns, [and after they brought them], he rushed into the jail and knelt down in front of Paul and Silas. [He was very afraid, so] much so that he was trembling/shaking.
Woyangʼanira ndendeyo anayitanitsa nyale, nathamangira mʼkati ndipo anadzigwetsa pa mapazi a Paulo ndi Sila akunjenjemera.
30 Then he brought Paul and Silas out [of the jail] and asked: “Sirs, what do I need to do to be saved [from being punished for my sins]?”
Iye anawatulutsa kunja ndipo anawafunsa kuti, “Amuna inu, ndichite chiyani kuti ndipulumuke?”
31 [They answered], “Trust in [what] the Lord Jesus [has done for you], and you will be saved {[God] will save you}, and the others who live in [MTY] your house will [also] be saved [if they believe in Jesus].”
Iwo anayankha kuti, “Khulupirira Ambuye Yesu ndipo udzapulumuka, iwe ndi a mʼbanja lako.”
32 Then the jailer took Paul and Silas into his house, washed their wounds, and gave them a meal. [He woke up all the people in his house, and] Paul and Silas told all of them the message about the Lord [Jesus. They all believed in him]. Immediately [after that, the jailer and all his family were baptized] {[Paul and Silas] baptized the jailer and all his family}. They were very happy, because now they all believed in God.
Kenaka analalikira mawu a Ambuye kwa iyeyo ndi onse amene anali mʼnyumba mwake.
Usiku womwewo woyangʼanira ndendeyo anawatenga nakawatsuka mabala awo; ndipo pomwepo iye ndi a mʼbanja lake anabatizidwa.
Woyangʼanira ndendeyo anapita nawo ku nyumba yake, nakawapatsa chakudya, ndipo banja lonse linadzazidwa ndi chimwemwe chifukwa anakhulupirira Mulungu.
35 The next morning, the [Roman] officials commanded [some] police officers [to go to the jail to say to the jailer], “[Our bosses] say, ‘Let those [two] prisoners go [now]!’”
Kutacha, woweruza milandu uja anatuma asilikali kwa woyangʼanira ndendeyo kukanena kuti, “Amasuleni anthu aja.”
36 [After the officers went and told that to] the jailer, he [went and] told Paul, “The [Roman] authorities have sent a message [(sg)] saying that I should release you [(sg)] and Silas [from prison]. So you [two] can leave [the jail] now. Now you can go peacefully!”
Woyangʼanira ndendeyo anawuza Paulo kuti, “Woweruza milandu walamula kuti iwe ndi Sila mumasulidwe. Tsopano muzipita. Pitani mumtendere.”
37 But Paul said to the police officers, “The authorities [commanded men to] beat us in front of a crowd before [those authorities] had learned if we [(exc)] had done anything wrong! Then they [ordered men to] shove us into jail! [But that was not legal, because] we [(exc)] are Roman citizens! And now they want [RHQ] to send us away secretly! We will not accept that! Those [Roman] officials must come themselves and [tell us that they are sorry], and take us out [of jail].”
Koma Paulo anati kwa asilikaliwo: “Iwo anatikwapula pa gulu la anthu asanatiweruze, ngakhale kuti ndife nzika za Chiroma natiponya mʼndende. Kodi tsopano akufuna kutitulutsa mwamseri? Ayi! Asiyeni abwere okha kuti adzatitulutse.”
38 So the police officers [went and] told the city authorities [what Paul had said]. When those authorities heard that Paul and Silas were Roman citizens, they were afraid [that someone would report to more important officials what they had done, and as a result they would be punished] {[those officials would punish them]}.
Asilikali aja anakafotokozera woweruza milandu ndipo pamene anamva kuti Paulo ndi Sila anali nzika za Chiroma, anachita mantha.
39 So the city authorities came to Paul and Silas and told them that they were sorry for what they had done to them. The authorities brought them out of the jail, and repeatedly asked them to leave the city [soon].
Iye anabwera kudzawapepesa ndipo anawatulutsa mʼndende, nawapempha kuti achoke mu mzindawo.
40 After Paul and Silas left the jail, they went to Lydia’s house. There they met with her and the [other] believers. They encouraged the believers [to continue trusting in the Lord Jesus], and then the two apostles left [Philippi].
Paulo ndi Sila atatuluka mʼndende, anapita ku nyumba ya Lidiya, kumene anakumana ndi abale nawalimbikitsa. Kenaka anachoka.

< Acts 16 >